< Hoseya 14 >
1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Omvänd dig, Israel, till Herran, din Gud; ty du äst fallen för din misshandels skull.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Tager dessa orden med eder, och vänder eder om till Herran; och säger till honom: Förlåt oss alla synder, och gör oss godt, så vilja vi offra våra läppars oxar.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Assur skall intet hjelpa oss, och vi vilje icke mer rida på hästar, och icke mer säga till våra händers verk: I ären vår Gud; utan låt de faderlösa finna nåd när dig.
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
Så skall jag åter hela deras afträdelse; gerna vill jag hafva dem kär; då skall jag vända mina vrede ifrå dem.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Jag vill vara Israel lika som en dagg, att han skall blomstras såsom en ros, och hans rötter skola utsträcka sig såsom Libanon;
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Och hans grenar utvidga sig, att han skall vara så dägelig som ett oljoträ, och skall gifva en sådana god lukt som Libanon;
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Och skola åter sitta under hans skugga; af korn skola de föda sig, och blomstras lika som ett vinträ; hans åminnelse skall vara lika som vinet på Libanon.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Ephraim, bort med de afgudar. Jag skall bönhöra honom, och leda honom; jag vill vara såsom ett grönt furoträ; på mig skall man finna dina frukt.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Ho är vis, den detta förstår, och klok, den detta märker? Ty Herrans vägar äro rätte, och de rättfärdige vandra deruppå; men öfverträdarena falla deruppå.