< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Converte-te, ó Israel, ao Senhor teu Deus; porque pelos teus pecados tens caído.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Tomai convosco palavras, e convertei-vos ao Senhor: dizei-lhe: Tira toda a iniquidade, e recebe o bem; e pagaremos os bezerros dos nossos lábios.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Não nos salvará a Assyria, não iremos montados em cavalos, e à obra das nossas mãos não diremos mais: Tu és o nosso Deus; porque por ti o órfão alcançará misericórdia.
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
Eu sararei a sua perversão, eu voluntariamente os amarei; porque a minha ira se apartou deles.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Eu serei a Israel como orvalho, ele florescerá como o lírio, e espalhará as suas raízes como o líbano.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Estender-se-ão as suas vergonteas, e a sua glória será como a da oliveira, e cheirará como o líbano.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Voltarão os que se assentarem debaixo da sua sombra; serão vivificados como o trigo, e florescerão como a vide; a sua memória será como o vinho do líbano.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Ephraim então dirá: Que mais tenho eu com os ídolos? eu o tenho ouvido, e olharei para ele: ser-lhe-ei como a faia verde: de mim é achado o teu fruto.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Quem é sábio, para que entenda estas coisas; quem é prudente, para que as saiba? porque os caminhos do Senhor são retos, e os justos andarão neles, mas os transgressores cairão neles.

< Hoseya 14 >