< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
O Izraelu! nawróć się cale do Pana, Boga swego; albowiemeś upadł dla nieprawości swojej.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Weźmijcie z sobą słowa, i nawróćcie się do Pana, mówcie do niego: Odpuść wszystkę nieprawość, a daj to, co jest dobrego, tedyż oddamy cielce warg naszych.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Assur nie wzybawi nas, na koniach jeździć nie będziemy, i nie rzeczemy więcej robocie rąk naszych: Wyście bogowie nasi; bo w tobie sierotka znajduje miłosierdzie.
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
Uzdrowię odwrócenie ich, a rozmiłuję się w nich dobrowolnie; bo się odwróci zapalczywość moja od nich.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Będę Izraelowi jako rosa, że się rozkwitnie jako lilija, a zapuści korzenie swe jako Liban.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Rozrosną się gałęzie jego, a ozdoba jego będzie jako oliwne drzewo, a woń jego jako Libańska.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Nawrócą się, aby siedzieli pod cieniem jego, ożyją jako zboże, i puszczą się jako winna macica, której pamiątka będzie jako wino Libańskie.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Efraimie! cóż mi już do bałwanów? Ja cię wysłucham, i wejrzę na cię; Jam jest jako jodła zielona, ze mnie się owoc twój znalazł.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Kto mądry, niech to zrozumie, a kto roztropny, niech to pozna; bo drogi Pańskie są proste, a sprawiedliwi po nich chodzić będą, ale przestępcy na nich upadną.

< Hoseya 14 >