< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
ای اسرائیل، به سوی خداوند، خدای خود بازگشت کن، زیرا در زیر بار گناهانت خرد شده‌ای.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
نزد خداوند آیید و دعا کنید و گویید: «ای خداوند، گناهان ما را از ما دور کن، به ما رحمت فرموده، ما را بپذیر تا شکرگزاریهای خود را به تو تقدیم کنیم.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
نه آشور می‌تواند ما را نجات دهد و نه قدرت جنگی ما. دیگر هرگز بتهایی را که ساخته‌ایم خدایان خود نخواهیم خواند؛ زیرا ای خداوند، یتیمان از تو رحمت می‌یابند.»
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
خداوند می‌فرماید: «شما را از بت‌پرستی و بی‌ایمانی شفا خواهم بخشید و محبت من حد و مرزی نخواهد داشت، زیرا خشم و غضب من برای همیشه فرو خواهد نشست.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
من همچون باران بر اسرائیل خواهم بارید و او مانند سوسن، خواهد شکفت و مانند سرو آزاد لبنان، در زمین ریشه خواهد دوانید.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
شاخه‌هایش به زیبایی شاخه‌های زیتون گسترده خواهد شد و عطر و بوی آن همچون عطر و بوی جنگلهای لبنان خواهد بود.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
قوم من بار دیگر زیر سایه من استراحت خواهند کرد و مانند گندم گل خواهند داد، و مانند باغی پر آب و تاکستانی پر شکوفه و همچون شراب لبنان معطر خواهند بود.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
«اسرائیل خواهد گفت: مرا با بتها چه کار است؟ و من دعای او را اجابت کرده، مراقب او خواهم بود. من همچون درختی همیشه سبز، در تمام مدت سال به او میوه خواهم داد.»
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
هر که داناست این چیزها را درک کند. آن که فهم دارد گوش دهد، زیرا راههای خداوند راست و درست است و نیکان در آن راه خواهند رفت، ولی بدکاران لغزیده، خواهند افتاد.

< Hoseya 14 >