< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Reviens, Israël, à Yahweh, car tu es tombé par ton iniquité.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Prenez avec vous des paroles, et revenez à Yahweh; dites-lui: « Ôtez toute iniquité et prenez ce qui est bon! Que nous vous offrions, au lieu de taureaux, les paroles de nos lèvres.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Assur ne nous sauvera pas, nous ne monterons pas sur des chevaux; et nous ne dirons plus: « Notre Dieu! » à l’œuvre de nos mains. Ô vous, en qui l’orphelin trouve compassion!
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
Je guérirai leur infidélité, je les aimerai de bon cœur; car ma colère s’est retirée d’eux.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Je serai comme la rosée pour Israël; il croîtra comme le lis, il poussera ses racines comme le Liban.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Ses rejetons s’étendront, sa gloire sera comme celle de l’olivier, et son parfum comme celui du Liban.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Ceux qui viendront se reposer à son ombre feront revivre le froment; ils croîtront comme la vigne; son nom sera comme le vin du Liban.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Éphraïm… qu’aurait-il encore à faire avec les idoles? C’est moi qui lui réponds, qui le regarde; je suis comme un cyprès verdoyant; c’est de moi que procède ton fruit.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Celui qui est sage, qu’il comprenne ces choses, celui qui est intelligent, qu’il les reconnaisse! Car les voies de Yahweh sont droites; les justes y marcheront, mais les rebelles y tomberont.

< Hoseya 14 >