< Hoseya 14 >
1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Return, O Israel, even unto the Lord thy God; for thou hast stumbled through thy iniquity.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Take with you swords, and return to the Lord: say unto him, “Pardon all [our] iniquity, and accept [our return to] good; and let us repay the steers [of sacrifice] with [the prayer of] our lips.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Asshur shall not help us; upon horses will we not ride: and we will no more say, Ye are our gods, to the work of our hands; for in thee alone the fatherless obtaineth mercy.”
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
I will heal their backsliding, I will love them freely; for my anger is turned away from them.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
I will be as the dew unto Israel: he shall bloom as the lily; and he shall strike his roots as [the forests of] Lebanon.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
His suckers shall spread out, and his beauty shall be as that of the olive-tree, and his smell as that of the Lebanon.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
They shall return that sat under his shade; they shall revive as corn, and bloom as the vine: the scent of which shall be as that of the wine of Lebanon.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Ephraim [shall say], What have I to do any more with idols? I have answered, and will observe him; I will be [to him] like a green fir-tree; through me is thy fruit found.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Who is wise, that he may understand these things? intelligent, that he may know them? for righteous are the ways of the Lord; and the just shall walk in them; but the transgressors will stumble through them.