< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Obratiž se, ó Izraeli, cele k Hospodinu Bohu svému, nebo jsi padl příčinou nepravosti své.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Vezměte s sebou slova, a obraťte se k Hospodinu, a rcete jemu: Sejmi všelikou nepravost, a dej to, což dobrého jest, a budemeť se odplaceti volky rtů našich.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Assurť nemůže zachovati nás, na koních nepojedeme, aniž díme více dílu rukou našich: Bůh náš; nebo v tobě smilování nalézá sirotek.
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
Uzdravím odvrácení jejich, budu je milovati dobrovolně; nebo odvrácen bude hněv můj od nich.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Budu jako rosa Izraelovi, zkvetne jako lilium, a hluboce vpustí kořeny své jako Libán.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Rozloží se ratoléstky jeho, a bude jako oliva okrasa jeho, a vůně jeho jako Libánská.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Ti, kteříž by seděli pod stínem jeho, navrátí se, oživou jako obilé, a pučiti se budou jako kmen vinný, jehož památka bude jako vína Libánského.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Efraime, což jest mi již do modl? Já vyslýchati, a patřiti budu na tě; já jsem jako jedle zelenající se, ze mneť ovoce tvé jest.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Kdo jest moudrý, porozuměj těmto věcem, a rozumný poznej je; nebo přímé jsou cesty Hospodinovy, a spravedliví choditi budou po nich, přestupníci pak na nich padnou.

< Hoseya 14 >