< Hoseya 13 >
1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Cuando Efraín habló, hubo temblores. Se exaltó en Israel, pero cuando se hizo culpable a través de Baal, murió.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
Ahora pecan más y más, y se han hecho imágenes fundidas de su plata, hasta los ídolos según su propio entendimiento, todos ellos obra de los artesanos. Dicen de ellos: “Ofrecen sacrificios humanos y besan a los terneros”.
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Por eso serán como la niebla de la mañana, como el rocío que pasa pronto, como la paja que es expulsada con el torbellino de la era, y como el humo de la chimenea.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
“Sin embargo, yo soy Yahvé, tu Dios, desde la tierra de Egipto; y no reconocerás a ningún dios más que a mí, y además de mí no hay ningún salvador.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
Te conocí en el desierto, en la tierra de la gran sequía.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
Según sus pastos, así se llenaron; se llenaron, y su corazón se exaltó. Por eso se han olvidado de mí.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Por eso soy como un león para ellos. Como un leopardo, acecharé el camino.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
Me reuniré con ellos como una osa que se queda sin sus cachorros, y desgarrará la cubierta de su corazón. Allí los devoraré como una leona. El animal salvaje los desgarrará.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Estás destruido, Israel, porque estás en contra de mí, contra su ayudante.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
¿Dónde está ahora vuestro rey para salvaros en todas vuestras ciudades? ¿Y tus jueces, de los que dijiste: ‘Dame un rey y príncipes’?
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
Te he dado un rey en mi ira, y me lo he llevado en mi ira.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
La culpa de Efraín está acumulada. Su pecado está almacenado.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
Los dolores de una mujer de parto caerán sobre él. Es un hijo imprudente, porque cuando es el momento, no viene a la apertura del vientre.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
Los rescataré del poder del Seol. ¡Los redimiré de la muerte! Muerte, ¿dónde están tus plagas? Sheol, ¿dónde está tu destrucción? “La compasión estará oculta a mis ojos. (Sheol )
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Aunque sea fructífero entre sus hermanos, vendrá un viento del este, el aliento de Yahvé subiendo desde el desierto; y su manantial se secará, y su fuente se secará. Saqueará el almacén del tesoro.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Samaria cargará con su culpa, porque se ha rebelado contra su Dios. Caerán por la espada. Sus hijos serán despedazados, y sus mujeres embarazadas serán desgarradas”.