< Hoseya 13 >
1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Quando Ephraim falou, houve tremores. Ele se exaltou em Israel, mas quando ele se tornou culpado através de Baal, ele morreu.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
Agora eles pecam cada vez mais, e se fizeram imagens derretidas de sua prata, mesmo ídolos, de acordo com seu próprio entendimento, todos eles o trabalho dos artesãos. Dizem deles: “Eles oferecem sacrifício humano e beijam os bezerros”.
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Portanto, eles serão como a névoa da manhã, como o orvalho que passa cedo, como o palhiço que é conduzido com o redemoinho para fora da eira, e como a fumaça fora da chaminé.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
“No entanto, eu sou Yahweh, vosso Deus, da terra do Egito; e não reconhecerá nenhum deus além de mim, e, além de mim, não há salvador.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
Eu o conheci no deserto, na terra da grande seca.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
De acordo com seus pastos, assim eles foram preenchidos; eles estavam cheios, e seu coração estava exaltado. Portanto, eles se esqueceram de mim.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Portanto, eu sou como um leão para eles. Como um leopardo, eu me esconderei pelo caminho.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
Vou encontrá-los como um urso que está de luto por seus filhotes, e rasgarão a cobertura de seu coração. Aí os devorarei como uma leoa. O animal selvagem vai rasgá-los.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Você está destruído, Israel, porque você está contra mim, contra seu ajudante.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Onde está seu rei agora, para que ele possa salvá-lo em todas as suas cidades? E seus juízes, dos quais você disse: “Dê-me um rei e príncipes”?
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
Eu lhe dei um rei em minha raiva, e o levaram na minha ira.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
A culpa de Ephraim é armazenada. Seu pecado é armazenado.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
As tristezas de uma mulher que está de parto virão sobre ele. Ele é um filho insensato, pois quando chega a hora, ele não vem para a abertura do útero.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
Eu os resgatarei do poder do Sheol. Eu os resgatarei da morte! Morte, onde estão suas pragas? Sheol, onde está sua destruição? “A compaixão será escondida dos meus olhos”. (Sheol )
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Embora ele seja frutífero entre seus irmãos, um vento leste virá, o sopro de Yahweh vindo do deserto; e sua mola se tornará seca, e sua fonte estará seca. Ele saqueará o depósito do tesouro.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Samaria suportará sua culpa, pois ela se rebelou contra seu Deus. Eles cairão pela espada. Seus bebês serão despedaçados em pedaços, e suas mulheres grávidas serão rasgadas”.