< Hoseya 13 >

1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Dahulu suku Efraim dihormati sehingga apabila ada perintah dari suku itu, suku-suku lain di Israel takut. Tapi suku Efraim berdosa karena menyembah Baal, sebab itu ia akan lenyap.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
Sampai sekarang orang-orang Efraim itu masih terus berbuat dosa; mereka membuat patung-patung perak untuk disembah--patung yang direncanakan oleh akal manusia dan dibentuk oleh tangan manusia. Mereka berkata, "Persembahkanlah kurban kepada patung-patung ini!" Aneh, manusia mencium patung anak sapi!
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Karena itu orang-orang itu akan lenyap seperti kabut atau embun di pagi hari. Mereka akan seperti debu merang yang ditiup angin di pengirikan gandum, dan seperti asap yang keluar dari cerobong.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
TUHAN berkata, "Akulah TUHAN Allahmu, yang membawa kamu keluar dari Mesir. Kamu tidak mempunyai Allah selain Aku. Akulah satu-satunya penyelamatmu.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
Di tanah gersang di padang gurun, Akulah yang menjaga kamu.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
Tapi setelah kamu berada di negeri yang baik, dan kamu kenyang serta puas, kamu menjadi angkuh lalu melupakan Aku.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Karena itu Aku akan menyergap kamu seperti singa. Seperti macan tutul Aku akan menghadang kamu di jalan.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
Aku akan menyerang kamu seperti beruang yang kehilangan anak-anaknya. Aku akan menyobek-nyobek kamu. Seperti singa Aku akan menerkam kamu di tempatmu, dan seperti binatang buas Aku akan mencabik-cabik kamu.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Aku akan menghancurkan kamu, hai bangsa Israel! Dan siapakah yang dapat menolongmu?
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Kamu minta raja dan pemimpin, tapi di manakah mereka semua sekarang? Dapatkah mereka menyelamatkan rakyatmu?
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
Dengan marah Aku memberikan raja kepadamu, dan dengan geram Kutarik mereka kembali."
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
TUHAN berkata, "Dosa dan kesalahan Israel telah dicatat, dan catatannya disimpan.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
Israel mempunyai kesempatan untuk hidup, tapi ia begitu bodoh sehingga tidak menggunakan kesempatan itu. Ia seperti bayi yang sesaat lagi akan lahir tapi tidak mau keluar dari rahim ibu.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
Bangsa ini tidak akan Kuselamatkan dari kuasa dunia orang mati. Hai kematian, sebarkanlah wabahmu! Laksanakanlah pekerjaanmu yang menghancurkan itu! Aku tidak mengasihani bangsa ini lagi. (Sheol h7585)
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Sekalipun Israel makmur seperti rumput yang subur, namun Aku akan mengirim angin timur yang panas dari padang gurun. Angin itu akan mengeringkan segala mata air dan sumur-sumur, sehingga lenyaplah semua yang berharga.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Samaria harus dihukum karena memberontak melawan Aku. Rakyatnya akan tewas dalam pertempuran; anak-anak bayinya akan digilas, dan wanita-wanita hamil dibelah perutnya."

< Hoseya 13 >