< Hoseya 13 >

1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Quand Ephraïm élevait la voix, on tremblait; il était grand en Israël. Il a prévariqué en adorant Baal, et il a péri.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
Et maintenant, ils redoublent leurs fautes; ils se sont fait des idoles avec leur argent, et avec leur industrie, des images; tout cela c’est œuvre d’artiste. C’Est à elles qu’ils s’adressent; et pour rendre hommage à des veaux, ils immolent des hommes.
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Eh bien! ils seront comme la brume du matin et comme la rosée qui se dissipe de bonne heure; comme le fétu tourbillonne hors de l’aire, comme la fumée s’échappe par une lucarne.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
C’Est pourtant moi, l’Eternel, qui fus ton Dieu dès le pays d’Egypte; tout autre Dieu que moi devait t’être inconnu, et il n’est pas de libérateur en dehors de moi.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
C’Est moi qui ai veillé sur toi dans le désert, sur les plages brûlantes.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
Comme ils recevaient la pâture, ils la consommaient; une fois repus, leur cœur s’enfla, et alors ils m’oublièrent.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Aussi suis-je devenu pour eux comme un lion; comme un tigre, je guette au bord du chemin.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
Je fondrai sur eux comme une ourse privée de ses petits, je déchirerai l’enveloppe de leur cœur, et je m’en repaîtrai comme un léopard: les animaux des champs les mettront en pièces.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Ce qui t’a perdu, ô Israël, c’est que tu t’es insurgé contre moi, contre ton protecteur.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Où donc est ton roi? Qu’il te défende contre tant d’ennemis! Où sont tes juges, puisque tu disais "Donne-moi un roi et des chefs!"
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
Je te donne un roi dans ma colère, et je le reprends dans mon indignation.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
Les méfaits d’Ephraïm sont fixés dans mon esprit, ses péchés sont mis en réserve.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
Les douleurs d’une femme en travail lui arrivent; enfant qu’il est, il n’a point de raison, autrement il ne resterait pas attaché au siège de l’enfantement.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
Et je les délivrerais du sépulcre! je les sauverais de la mort! Où sont tes fléaux, ô Mort? Où est ton œuvre de destruction, ô Sépulcre? Que la clémence se dérobe à ma vue! (Sheol h7585)
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Dût-il porter des fruits abondants parmi ses frères, il viendra le vent d’Orient, le vent de l’Eternel, montant du fond du désert, qui tarira sa source et mettra à sec sa fontaine. Il enlèvera ce dépôt de tous les objets précieux.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Périsse Samarie, puisqu’elle a trahi son Dieu! Ils tomberont sous le glaive, leurs jeunes enfants seront mis en pièces, leurs femmes enceintes éventrées.

< Hoseya 13 >