< Hoseya 13 >
1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
For Effraym spak, hidousnesse assailide Israel; and he trespasside in Baal, and was deed.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
And now thei addiden to do synne, and maden to hem a yotun ymage of her siluer, as the licnesse of idols; al is the makyng of crafti men. To these thei seien, A! ye men, offre, and worschipe caluys.
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Therfor thei schulen be as a morewtid cloude, and as the deew of morewtid, that passith forth, as dust rauyschide bi whirlewynd fro the corn floor, and as smoke of a chymenei.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
Forsothe Y am thi Lord God, `that ledde thee fro the loond of Egipt; and thou schalt not knowe God, outakun me, and no sauyour is, outakun me.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
Y knewe thee in the desert, in the lond of wildirnesse.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
Bi her lesewis thei weren fillid, and hadden abundaunce; thei reisiden her herte, and foryaten me.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
And Y schal be as a lionesse to hem, as a parde in the weye of Assiriens.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
Y as a femal bere, whanne the whelps ben rauyschid, schal mete hem; and schal al to-breke the ynnere thingis of the mawe of hem. And Y as a lioun schal waaste hem there; a beeste of the feeld schal al to-rende hem.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Israel, thi perdicioun is of thee; thin help is oneli of me.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Where is thi kyng? moost saue he thee now in alle thi citees; and where ben thi iugis, of whiche thou seidist, Yyue thou to me a kyng, and princes?
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
Y schal yyue to thee a kyng in my strong veniaunce, and Y schal take awei in myn indignacioun.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
The wickidnesse of Effraym is boundun togidere; his synne is hid.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
The sorewis of a womman trauelynge of child schulen come to hym; he is a sone not wijs. For now he schal not stonde in the defoulyng of sones.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
Y schal delyuere hem fro the hoond of deeth, and Y schal ayenbie hem fro deth. Thou deth, Y schal be thi deth; thou helle, Y schal be thi mussel. (Sheol )
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Coumfort is hid fro myn iyen, for he schal departe bitwixe britheren. The Lord schal brynge a brennynge wynd, stiynge fro desert; and it schal make drie the veynes therof, and it schal make desolat the welle therof; and he schal rauysche the tresour of ech desirable vessel.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Samarie perische, for it stiride his God to bittirnesse; perische it bi swerd. The litle children of hem be hurtlid doun, and the wymmen with child therof be koruun.