< Hoseya 13 >
1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Kad je Efrajim govorio, strah je zadavao, jer bijaše on prvak u Izraelu, al' ogriješi se Baalom i poginu.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
I sad još griješe oni od srebra praveć' sebi kipove, kumire po svojoj mašti; svi su oni djelo rukotvorca! Tima - vele - žrtvujte, ljudi neka cjelivaju teoce!
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Zato, bit će oni kao oblak jutarnji, kao rosa koje brzo nestaje, kao pljeva raznesena s gumna, kao dim što kroz otvor izlazi.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
A ja sam Jahve, Bog tvoj sve od zemlje egipatske: drugog Boga osim mene ne ljubi! Osim mene nema spasitelja.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
Ja te ljubljah u pustinji, u zemlji suhoj.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
Ja ih pasoh, i siti bijahu; nasićenima srce se uzoholi; i tako me zaboraviše.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Stoga ću im biti kao lav, kao leopard što na putu vreba;
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
kao medvjedica kojoj ugrabiše mlade, ja ću se na njih baciti, rastrgat' im grudi do srca; k'o lav ću proždrijeti meso njihovo, zvijeri će ih poljske rastrgati.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Uništit ću te, Izraele, i tko će ti pomoći?
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
TÓa gdje ti je kralj da te spasi, gdje tvoji knezovi da te brane - oni za koje si govorio: “Daj mi kralja i knezove!”
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
U gnjevu svom kralja ti dadoh i u srdžbi ti ga uzimam.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
Dobro se čuva bezakonje Efrajimovo, grijeh je njegov dobro pohranjen.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
Dođoše na nj trudovi porodiljski, ali on je ludo čedo, ne izlazi na vrijeme iz utrobe materine!
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
Ja ću ih izbaviti od vlasti Podzemlja, od smrti ću ih spasiti! Gdje je tvoja kuga, o smrti, gdje pomor tvoj, Podzemlje! Samilost se sakri od mojih očiju! (Sheol )
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Tako je rodan među braćom Efrajim, ali će doći vjetar istočni, vjetar Jahvin iz pustinje: isušit će mu izvore, presahnuti studence, opljačkat mu riznicu, blago odnijeti.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Ispaštat će Samarija jer se protiv Boga svoga pobunila. Od mača past će oni, djecu će njihovu smrskati, žene trudne rasporiti.