< Hoseya 12 >
1 Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Efrájim se hrani z vetrom in sledi vzhodnemu vetru, dnevno povečuje laži in opustošenje, sklepa zavezo z Asirci in olje nosi v Egipt.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
Prav tako ima Gospod polemiko z Judom in kaznoval bo Jakoba glede na njegove poti; poplačal mu bo glede na njegova dejanja.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
V maternici je svojega brata prijel za peto in s svojo močjo je imel moč z Bogom.
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
Da, imel je moč nad angelom in je prevladal. Jokal je in ponižno prosil k njemu. Našel ga je v Betelu in tam je [Bog] govoril z nami;
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
celo Gospod Bog nad bojevniki; Gospod je njegov spomenik.
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
Zatorej se obrni k svojemu Bogu, ohranjaj usmiljenje in sodbo in nenehno čakaj na svojega Boga.
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
On je trgovec, v njegovi roki so tehtnice prevare, rad zatira.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
Efrájim je rekel: »Vendar sem postal bogat, pridobil sem si imetje, v vseh mojih naporih ne bodo našli v meni nobene krivičnosti, da bi bila greh.«
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
»Jaz pa, ki sem Gospod, tvoj Bog, od egiptovske dežele, te bom vendarle prisilil, da prebivaš v šotorih kakor v dneh slovesnega praznika.
10 Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
Prav tako sem govoril po prerokih in množil videnja ter po služenju prerokov uporabljal prilike.
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
Ali je v Gileádu krivičnost? Oni so zagotovo ničevost. V Gilgálu žrtvujejo bikce. Da, njihovi oltarji so kakor kupi na brazdah polj.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
Jakob je zbežal v sirsko deželo in Izrael je služil za ženo in za ženo je varoval ovce.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
In po preroku je Gospod Izraela privedel iz Egipta in po preroku je bil obvarovan.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Efrájim ga je silno grenko izzival k jezi, zatorej bo njegovo kri pustil nad njim in njegovo grajo bo njegov Gospod povrnil k njemu.