< Hoseya 12 >
1 Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Jefrem se hrani vjetrom, i ide za ustokom; svaki dan množi laž i pogibao; i hvataju vjeru s Asircem i nose ulje u Misir.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
I s Judom ima Gospod parbu i pohodiæe Jakova prema putovima njegovijem, platiæe mu po djelima njegovijem.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
U utrobi uhvati za petu brata svojega, i u sili svojoj bori se s Bogom;
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
Bori se s anðelom, i nadjaèa; plaka, i moli mu se; naðe ga u Vetilju, i ondje govori s nama.
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
Ali je Gospod Bog nad vojskama, Gospod mu je spomen.
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
Ti dakle obrati se k Bogu svojemu, èuvaj milost i pravdu, i uzdaj se vazda u Boga svojega.
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
Trgovac je Jefrem, u ruci su mu mjerila lažna, milo mu je da èini krivo.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
I govori Jefrem: baš se obogatih, stekoh blago, ni u kom trudu mom neæe mi naæi nepravde koja bi bila grijeh.
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
A ja sam Gospod Bog tvoj od zemlje Misirske, još æu ti dati da sjediš u šatorima kao o praznicima.
10 Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
I govoriæu preko proroka, i umnožiæu utvare, i davaæu prièu preko proroka.
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
Doista je Galad bezakonje, postaše sama taština; u Galgalu prinose junce na žrtvu, i oltari su im kao gomile kamenja po brazdama na njivi mojoj.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
I Jakov pobježe u zemlju Sirsku, i Izrailj služi za ženu, i za ženu èuva ovce.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
I prorokom izvede Gospod Izrailja iz Misira, i prorokom èuva ga.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Jefrem ga ljuto razgnjevi; zato æe ostaviti na njemu krv njegovu, i vratiæe mu sramotu njegovu Gospod njegov.