< Hoseya 12 >

1 Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Ephraïm se repaît de vent et poursuit un air brûlant; tout le jour il multiplie le mensonge et la dévastation; il a fait alliance avec les Assyriens et il portait de l’huile en Egypte.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
Voici donc venir le jugement du Seigneur avec Juda, et sa visite sur Jacob; il lui rendra selon ses voies et ses inventions.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
Dans le sein maternel il supplanta son frère; par sa force il lutta avec l’ange.
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
Et il prévalut contre l’ange et il fut fortifié; il pleura, et le pria: il le trouva à Béthel, et là le Seigneur nous parla.
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
Et le Seigneur, le Dieu des armées, le Seigneur devint l’objet de son souvenir.
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
Et toi, Israël, à ton Dieu tu te convertiras; garde la miséricorde et le jugement, et espère en ton Dieu, toujours.
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
Quant à Chanaan, dans sa main est une balance trompeuse; il a aimé l’oppression.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
Et Ephraïm a dit: Cependant je suis devenu riche, j’ai trouvé une idole pour moi; aucun de mes travaux ne trouvera l’iniquité par laquelle j’ai péché.
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
Et moi, je suis le Seigneur ton Dieu, depuis que je t’ai retiré de la terre d’Egypte; je te ferai encore demeurer dans des tabernacles comme aux jours de fête.
10 Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
Et j’ai parlé aux prophètes, et c’est moi qui ai multiplié les visions; et par le ministère des prophètes j’ai été assimilé aux hommes.
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
Si Galaad était une idole, c’est donc en vain qu’ils sacrifiaient aux bœufs de Galgal; car leurs autels sont comme des monceaux de pierre sur les sillons des champs.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
Jacob a fui dans la contrée de Syrie, et Israël a servi pour une femme, et pour une autre femme il a servi.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
Par un prophète, le Seigneur a tiré Israël de l’Egypte, et par un prophète il a été conservé.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Par ses plaintes amères, Ephraïm m’a provoqué au courroux; et son sang retombera sur lui, et son opprobre, le Seigneur le lui rendra.

< Hoseya 12 >