< Hoseya 12 >

1 Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Effraym fedith wynd, and sueth heete. Al dai he multiplieth leesyng, and distriyng; and he made boond of pees with Assiriens, and bar oile in to Egipt.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
Therfor the doom of the Lord is with Juda, and visityng is on Jacob; bi the weies of hym, and bi the fyndyngis of hym he schal yelde to hym.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
In the wombe he supplauntide his brother, and in his strengthe he was dressid with the aungel.
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
And he was strong to the aungel, and was coumfortid; he wepte, and preiede hym; in Bethel he foond hym, and there he spak with vs.
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
And the Lord God of oostis, the Lord, is the memorial of hym.
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
And thou schalt turne to thi God. Kepe thou merci and doom, and hope thou euere in thi God.
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
Chanaan louyde fals caleng, a gileful balaunce in his hond.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
And Effraym seide, Netheles Y am maad riche, Y haue founde an idol to me; alle my trauelis schulen not fynde to me the wickidnesse, whiche Y synnede.
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
And Y am thi Lord God fro the lond of Egipt; yit Y schal make thee to sitte in tabernaclis, as in the daies of feeste.
10 Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
And Y spak bi profetis, and Y multiplied profesie, and Y was licned in the hond of profetis.
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
If Galaad worschipith an idol, therfor thei erren in veyn offryng to oxis in Galgal; for whi and the auteris of hem schulen be as heepis on the forewis of the feeld.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
Jacob fledde in to the cuntrei of Sirie, and Israel seruyde for a wijf, and seruyde, ether kepte, for a wijf.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
But bi a profete the Lord ledde Israel out of Egipt, and bi a profete he was kept.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Effraym terride me to wrathfulnesse in hise bitternessis, and the blood of hym schal come on hym; and his Lord schal restore to hym the schenschipe of him.

< Hoseya 12 >