< Hoseya 12 >

1 Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Ephraim to pasture spirit: breath and to pursue east all [the] day lie and violence to multiply and covenant with Assyria to cut: make(covenant) and oil to/for Egypt to conduct
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
and strife to/for LORD with Judah and to/for to reckon: punish upon Jacob like/as way: conduct his like/as deed his to return: pay to/for him
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
in/on/with belly: womb to assail [obj] brother: male-sibling his and in/on/with strength his to strive with God
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
and to reign to(wards) messenger: angel and be able to weep and be gracious to/for him Bethel Bethel to find him and there to speak: speak with us
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
and LORD God [the] Hosts LORD memorial his
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
and you(m. s.) in/on/with God your to return: return kindness and justice to keep: careful and to await to(wards) God your continually
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
merchant in/on/with hand his balance deceit to/for to oppress to love: lover
8 Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
and to say Ephraim surely to enrich to find strength to/for me all toil my not to find to/for me iniquity: crime which sin
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
and I LORD God your from land: country/planet Egypt still to dwell you in/on/with tent like/as day meeting: festival
10 Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
and to speak: speak upon [the] prophet and I vision to multiply and in/on/with hand: by [the] prophet to resemble
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
if Gilead evil: wickedness surely vanity: vain to be in/on/with Gilgal cattle to sacrifice also altar their like/as heap upon furrow field
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
and to flee Jacob land: country Aram and to serve Israel in/on/with woman: wife and in/on/with woman: wife to keep: guard
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
and in/on/with prophet to ascend: establish LORD [obj] Israel from Egypt and in/on/with prophet to keep: guard
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
to provoke Ephraim bitterness and blood his upon him to leave and reproach his to return: pay to/for him lord his

< Hoseya 12 >