< Hoseya 12 >

1 Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Efraim lægger sig efter Vind og jager efter Østenvejr, den hele Dag formerer han Løgn og Voldsgerning; og de slutte Pagt med Assyrien, og Olie føres til Ægypten.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
Og Herren har Trætte med Juda, og han er rede til at hjemsøge Jakob efter hans Veje og betale ham efter hans Idrætter.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
I Moders Liv holdt han sin Broder om Hælen, og i sin Manddoms Kraft kæmpede han med Gud.
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
Ja, han kæmpede med en Engel og sejrede, han græd og bad ham om Naade; han fandt ham i Bethel, og der talte han med os.
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
Og Herren, Hærskarernes Gud — „Herren‟ er hans Ihukommelses Navn.
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
Og du, du skal omvende dig til din Gud; bevar Miskundhed og Ret, og vent stedse paa din Gud!
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
I Kanaans Haand er der Falskheds Vægtskaale; han har Lyst til at forfordele.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
Og Efraim sagde: Jeg er dog bleven rig, jeg har vundet mig Formue; alle mine Arbejder paadrage mig ingen Overtrædelse, som maatte være Synd.
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
Men jeg er Herren din Gud fra Ægyptens Land af: Jeg vil endnu lade dig bo i Telte som paa Højtidens Dage.
10 Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
Og jeg har talt til Profeterne, og jeg har givet mange Syner, og ved Profeterne fremsatte jeg Lignelser.
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
Er Gilead Uretfærdighed, saa skulle de blive aldeles til intet; de have ofret Øksne i Gilgal, derfor skulle ogsaa deres Altre vorde som Stenhobe ved Furerne paa Marken.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
Og Jakob flyede til Arams Land, og Israel tjente for en Hustru; ja, for en Hustru maatte han være Hyrde.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
Og ved en Profet førte Herren Israel op af Ægypten, og ved en Profet blev det bevaret.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Efraim har vakt bitter Harme; men hans Herre skal lade hans Blodskyld blive paa ham og betale ham hans Forhaanelse.

< Hoseya 12 >