< Hoseya 12 >

1 Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Ephraim loh khohli dongah luem tih kanghawn a hloem. Hnin takuem ah laithae tih rhoelrhanah te a ping sak. Assyria neh paipi a saii uh tih Egypt la situi a khuen.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
BOEIPA he Judah neh tuituknah om. Jakob te a longpuei bangla a cawh vetih a khoboe bangla anih te a thuung ni.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
Bungko khuiah a maya te a uelh sak tih Pathen te a thahuem neh a hnueih.
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
Puencawn te khaw a hnueih tih a noeng. Rhap tih anih te a hloep. Amah te Bethel ah a hmuh tih mamih taengah pahoi a thui.
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
Yahweh ngawn tah caempuei Pathen la a om dongah amah mingthen khaw Yahweh ni.
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
Tedae nang tah na Pathen taengla mael laeh. Sitlohnah neh tiktamnah he ngaithuen lamtah na Pathen te lamtawn yoeyah lah.
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
Hnoyoi loh a kut dongah thailatnah cooi a khueh tih hnaemtaek ham a lungnah.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
Ephraim loh, “Ka boei ngawn, kamah hamla thahuem ka dang, ka thaphu boeih ni, ka khuiah tholhnah la thaesainah hmuh uh mahpawh,” a ti.
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
Egypt kho lamkah parhi te nangmih kah Pathen Yahweh kamah long ni nang te dap khuiah tingtunnah khohnin kah bangla koep kho kan sak sak eh.
10 Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
Tonghma rhoek lamloh kan thui tih ka mangthui khaw yet coeng. Tonghma rhoek kut lamlong khaw ka puet sak.
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
Gilead kah boethae a om atah Gilgal ah om khaw a poeyoek. Vaito a nawn uh akhaw amih kah hmueihtuk te lai kong ah lungkuk bangla om.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
Jakob te Aram khohmuen la yong coeng. Israel he huta hamla thotat tih a yuu hamla a dawn.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
BOEIPA loh Israel te Egypt lamloh tonghma kut neh a khuen tih tonghma kut neh a ngaithuen.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Ephraim loh kosidung te a veet dongah a thii te amah soah coe ni. A kokhahnah te a boei loh amah taengah a thuung ni.

< Hoseya 12 >