< Hoseya 11 >

1 “Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
“Bere a Israel yɛ abofra no, na medɔ no, na Misraim na mefrɛɛ me babarima fii.
2 Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
Nanso mpɛn dodow a mefrɛɛ Israel no, saa ara na woguan fii me nkyɛn. Wɔbɔɔ afɔre maa Baal ahoni, na wɔhyew nnuhuam maa nsɛsode.
3 Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
Me na migyigyee Efraim taataa, turuu wɔn wɔ me basa so; nanso wɔnkae sɛ me na mesaa wɔn yare.
4 Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
Me de ayamye hama ne ɔdɔ dii wɔn anim; miyii konnua no fii wɔn kɔn mu na mekotow maa wɔn aduan dii.
5 “Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
“Wɔbɛsan akɔ Misraim, na Asiria adi wɔn so, esiane sɛ wɔannu wɔn ho nti.
6 Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
Afoa bedi ahim wɔ wɔn kuropɔn mu na ɛbɛsɛe wɔn apon akyi adaban na wɔn nhyehyɛe to betwa.
7 Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
Me nkurɔfo asi no pi sɛ wɔbɛtwe wɔn ho afi me nkyɛn. Sɛ mpo wosu frɛ me Onyankopɔn Ɔsorosoroni no mpo a meremma wɔn so ɔkwan biara so.
8 “Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
“Ɛbɛyɛ dɛn na meyi wo ama, Efraim? Ɛbɛyɛ dɛn ma meyi wo ama, Israel? Ɛbɛyɛ dɛn na mɛyɛ wo sɛ Adma? Ɛbɛyɛ dɛn na mɛyɛ wo sɛ Seboim? Me koma asakra wɔ me mu; na mʼahummɔbɔ ahwanyan.
9 Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
Merenyɛ mʼabufuwhyew so ade, na merennan me ho nsɛe Efraim bio. Meyɛ Onyankopɔn na menyɛ onipa. Meyɛ Ɔkronkronni a ɔwɔ mo mu. Meremma wɔ abufuw mu.
10 Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
Wobedi Awurade akyi. Ɔbɛbobɔ mu te sɛ gyata. Na sɛ ɔbobɔ mu a, ne mma de ahopopo befi atɔe aba.
11 Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
Wɔde ahopopo bɛba te sɛ nnomaa a wofi Misraim, te sɛ mmorɔnoma a wofi Asiria. Mɛbɔ wɔn atenase wɔ wɔn afi mu,” sɛnea Awurade se ni.
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
Efraim de atoro atwa me ho ahyia, Israelfi nso wɔde nnaadaa. Yuda abɔ Onyankopɔn so ko mpo ɔde tia Ɔkronkronni nokwafo no.

< Hoseya 11 >