< Hoseya 11 >

1 “Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
“Ka Israel ne pod nyathi, ne ahere, kendo ne aluongo wuoda ka agolo Misri.
2 Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
To kaka ne amedo luongo Israel e kaka nomedo dhi mabor koda. Negichiwo misengini ne Baal kendo wangʼo ubani ne kido molosi.
3 Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
An owuon ema napuonjo Efraim wuotho, ka amakogi gi bedegi, to ne ok gifwenyo ni ne en An mane ochangogi.
4 Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
Ne atelonegi gi ngʼwono mathoth kaachiel gihera ma ok rum; ne agolo jok mapek e ngʼutgi kendo akulora piny mondo apidhgi.
5 “Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
“Donge ginidog Misri kendo Asuria nobedi gi loch kuomgi, nikech gitamore weyo richogi?
6 Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
Ligangla nomil e miechgi madongo manoketh lodi mag rangeyegi, kendo chenro duto magin-go norum.
7 Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
Joga oramo chuth mondo oweya. Kata giluong Nyasaye Man Malo Moloyo, to ok notingʼ-gi malo e yo moro amora.
8 “Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
“Ere kaka anyalo jwangʼou, Efraim? Ere kaka dabolu Israel? Ere kaka datiu ka Adma? Ere kaka damiu ubed machal gi Zeboim? Ok anyal timonu kamano; nikech aseloko pacha kendo akechou.
9 Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
Ok anaol mirimba mager bende ok analokra mi aketh Efraim bende. Nimar an Nyasaye, ok an dhano, Jal Maler e dieru. Ok anabi gi mirima.
10 Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
Gibiro luwo Jehova Nyasaye, noruti ka sibuor. Kuruto, to nyithinde duto nobi ire katetni kagiwuok yo podho chiengʼ.
11 Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
Ginibi ire ka gitetni ka winy moa Misri, ka akuche moa Asuria. Anami gibed e miechgi,” Jehova Nyasaye owacho.
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
Efraim oselwora gi miriambo, od jo-Israel en kar wuond. Juda ok winj Nyasaye; adier ok giwinj Jal Maler ma ja-adiera.

< Hoseya 11 >