< Hoseya 10 >

1 Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
Izrael jest vinný kmen prázdný, ovoce skládá sobě. Èím více mívá ovoce svého, tím více rozmnožuje oltáře, a čím lepší jest země jeho, tím více vzdělává obrazy.
2 Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
Klade díly srdce jejich, pročež vinni jsou. Onť poboří oltáře jejich, popléní obrazy jejich,
3 Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
Poněvadž i říkají: Nemáme žádného krále, nýbrž aniž se bojíme Hospodina, a král co by nám učinil?
4 Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
Mluví slova, klnouce se lživě, když činí smlouvu, a soud podobný jedu roste na záhonech polí mých.
5 Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
Z příčiny jalovic Betavenských děsiti se budou obyvatelé Samařští, když kvíliti bude nad nimi lid jejich i kněží jejich, (kteříž příčinou jejich nyní pléší), proto že sláva jejich zastěhuje se od nich.
6 Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
Ano i sám lid do Assyrie zaveden bude v dar králi, kterýž obhájce býti měl; Efraim hanbu ponese, a Izrael styděti se bude za své předsevzetí.
7 Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
Vyhlazen bude král Samařský jako pěna na svrchku vody.
8 Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
Vypléněny budou také výsosti Avenu, hřích Izraelských, trní a hloží zroste na oltářích jejich. I dějí horám: Přikrejte nás, a pahrbkům: Padněte na nás.
9 “Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
Ode dnů Gabaa hřešil jsi, Izraeli. Tamť jsou ostáli, nepostihla jich v Gabaa válka proti nešlechetným.
10 Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
A protož podlé líbosti své svíži je; nebo sberou se na ně národové k svázání jich, pro dvojí nepravost jejich.
11 Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
Nebo Efraim jest jalovička, kteráž byla vyučována; mlatbu miluje, ačkoli jsem já nastupoval na tučný krk její, abych k jízdě užíval Efraima, Juda aby oral, a Jákob vláčil. A říkal jsem:
12 Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
Rozsívejte sobě k spravedlnosti, žněte k milosrdenství, ořte sobě ouhor, poněvadž čas jest k hledání Hospodina, ažby přišel a dštil vám spravedlností.
13 Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
Ale orali jste bezbožnost, žali jste nepravost, jedli jste ovoce lži; nebo doufáš v cestu svou a ve množství reků svých.
14 phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
Protož povstane rozbroj mezi lidem tvým, i každá pevnost tvá zpuštěna bude, tak jako zpustil Salman Bet Arbel v den boje; matky s syny rozrážíny budou.
15 Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.
Aj, toť vám způsobí Bethel pro přílišnou nešlechetnost vaši; na svitání docela vyhlazen bude král Izraelský.

< Hoseya 10 >