< Hoseya 1 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
Parole du Seigneur qui fut adressée à Osée, fils de Bééri, dans les jours d’Ozias, de Joathan, d’Achaz et d’Ezéchias, rois de Juda, et dans les jours de Jéroboam, fils de Joas, roi d’Israël.
2 Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
Commencement des paroles du Seigneur par Osée; et le Seigneur dit à Osée: Va, prends pour toi une femme de fornications, et des enfants de fornications; parce que forniquant la terre forniquera en se séparant du Seigneur.
3 Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
Et il alla, et il prit Gomer, fille de Débelaïm; et elle conçut, et elle lui enfanta un fils.
4 Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
Et le Seigneur dit à Osée: Appelle son nom Jezrahel; parce qu’encore un peu de temps, et je visiterai le sang de Jezrahel sur la maison de Jéhu, et je ferai cesser le royaume de la maison d’Israël.
5 Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
Et en ce jour-là, je briserai l’arc d’Israël dans la vallée de Jezrahel.
6 Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
Et elle conçut encore, et elle enfanta une fille. Et le Seigneur dit à Osée: Appelle son nom, Sans miséricorde; parce qu’à l’avenir je n’aurai plus de pitié pour la maison d’Israël, mais que je les oublierai entièrement.
7 Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
Et j’aurai pitié de la maison de Juda, et je les sauverai par le Seigneur leur Dieu, et je ne les sauverai pas par l’arc, par le glaive, et par la guerre, et par les chevaux et par les cavaliers.
8 Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
Et Gomer sevra sa fille qui était appelée Sans miséricorde. Et elle conçut et elle enfanta un fils.
9 Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
Et Dieu dit: Appelle son nom, Non mon peuple, parce que vous n’êtes plus mon peuple, et que moi je ne serai pas pour vous.
10 “Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
Et le nombre des enfants d’Israël sera comme le sable de la mer, qui est sans mesure, et qui ne se comptera pas, et dans le lieu où il leur sera dit: Vous n’êtes pas mon peuple, il leur sera dit: Vous êtes les fils du Dieu vivant.
11 Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”
Et les fils de Juda et les fils d’Israël se réuniront ensemble; et ils se donneront un seul chef, et ils s’élèveront de la terre, parce que grand est le jour de Jezrahel.

< Hoseya 1 >