< Hoseya 1 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
[I am] Hosea, the son of Beeri. Yahweh gave me these messages [at various times] during the years that Uzziah, Jotham, Ahaz, and Hezekiah were the kings of Judah, and Jeroboam the son of Jehoash was the King of Israel.
2 Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
When Yahweh first [began to] give messages to me [to tell to the people of Israel], he said to me, “Go and marry a prostitute. But [some of] her children will be born as a result of her having sex with men to whom she is not married. That will illustrate how the people of Israel have turned away from me and worship (idols/other gods).”
3 Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
So I married Gomer, the daughter of Diblaim. She became pregnant and gave birth to my son.
4 Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
Yahweh said to me, “Give him the name Jezreel, [which means ‘God scatters’], because I will soon punish the descendants [MTY] of [King] Jehu [by scattering them], because he killed many of my people at Jezreel [town]. [Some day] I will end the kingdom of Israel,
5 Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
by destroying the power [MTY] of [the army of] Israel in Jezreel Valley.”
6 Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
[Later] Gomer became pregnant [again], and she gave birth to a daughter. Yahweh said to me “Give her the name Lo-ruhamah, [which means ‘not loved],’ because I will no longer [show that I] love the people [MET] of Israel, and I will not forgive them [for the sins that they have committed].
7 Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
But I will [show that I] love the people [MTY] of Judah [by saving them from their enemies]. However, it will not be by weapons and armies or horses and chariots that I will save them. Instead, it will be by [the power that I], Yahweh their God, [have].”
8 Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
After Gomer had (weaned/stopped breast-feeding) Lo-ruhamah, she became pregnant again, and she gave birth to another son.
9 Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
Yahweh said “Give him the name Lo-ammi, [which means 'not my people', ] because the people of Israel are no [longer my people], and I am not their God.
10 “Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
But [some day] the people of Israel will be [as numerous] as [SIM] the [grains of] sand on the seashore; no one will be able to count them. Now [I] am saying to them, ‘You are not my people,’ but then people will say to them, ‘[You are the] children of God who is all-powerful.’
11 Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”
[At that time], the people of Judah and the people of Israel will unite. They will appoint one leader for all of them, and they will return from the countries [to which they have been (exiled/forced to go)]. That will be a great time; Jezreel [also means ‘God plants’, and it will be as though God will plant them in this country again].”

< Hoseya 1 >