< Ahebri 1 >
1 Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri.
God, who in ancient days spoke to our forefathers in many distinct messages and by various methods through the Prophets,
2 Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. (aiōn )
has at the end of these days spoken to us through a Son, who is the pre-destined Lord of the universe, and through whom He made the Ages. (aiōn )
3 Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero.
He brightly reflects God's glory and is the exact representation of His being, and upholds the universe by His all-powerful word. After securing man's purification from sin He took His seat at the right hand of the Majesty on high,
4 Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.
having become as far superior to the angels as the Name He possesses by inheritance is more excellent than theirs.
5 Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati, “Iwe ndiwe mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.” Kapena kunenanso kuti, “Ine ndidzakhala abambo ake; iye adzakhala mwana wanga.”
For to which of the angels did God ever say, "My Son art Thou: I have this day become Thy Father;" and again, "I will be a Father to Him, and He shall be My Son"?
6 Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati, “Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”
But speaking of the time when He once more brings His Firstborn into the world, He says, "And let all God's angels worship Him."
7 Iye ponena za angelo akuti, “Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo, amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”
Moreover of the angels He says, "He changes His angels into winds, and His ministering servants into a flame of fire."
8 Koma za Mwana wake akuti, “Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya, ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu. (aiōn )
But of His Son, He says, "Thy throne, O God, is for ever and for ever, and the sceptre of Thy Kingdom is a sceptre of absolute justice. (aiōn )
9 Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”
Thou hast loved righteousness and hated lawlessness; therefore God, Thy God, has anointed Thee with the oil of gladness beyond Thy companions."
10 Mulungu akutinso, “Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi; ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
It is also of His Son that God says, "Thou, O Lord, in the beginning didst lay the foundations of the earth, and the heavens are the work of Thy hands.
11 Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire. Izo zidzatha ngati zovala.
The heavens will perish, but Thou remainest; and they will all grow old like a garment,
12 Mudzazipindapinda ngati chofunda; ndipo zidzasinthidwa ngati chovala. Koma Inu simudzasintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.”
and, as though they were a mantle Thou wilt roll them up; yes, like a garment, and they will undergo change. But Thou art the same, and Thy years will never come to an end."
13 Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti, “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditapanga adani ako kukhale chopondapo mapazi ako.”
To which of the angels has He ever said, "Sit at My right hand till I make Thy foes a footstool for Thy feet"?
14 Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?
Are not all angels spirits that serve Him--whom He sends out to render service for the benefit of those who, before long, will inherit salvation?