< Ahebri 1 >

1 Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri.
Efter at Gud fordum havde talt mange Gange og på mange Måder, til Fædrene ved Profeterne,
2 Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. (aiōn g165)
så har han ved Slutningen af disse Dage talt til os ved sin Søn, hvem han har sat til Arving af alle Ting, ved hvem han også har skabt Verden; (aiōn g165)
3 Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero.
han, som - efterdi han er hans Herligheds Glans og hans Væsens udtrykte Billede og bærer alle Ting med sin Krafts Ord - efter at have gjort Renselse fra Synderne har sat sig ved Majestætens højre Hånd i det høje,
4 Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.
idet han er bleven så meget ypperligere end Englene, som han har arvet et herligere Navn fremfor dem.
5 Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati, “Iwe ndiwe mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.” Kapena kunenanso kuti, “Ine ndidzakhala abambo ake; iye adzakhala mwana wanga.”
Thi til hvilken af Englene sagde han nogen Sinde: "Du er min Søn, jeg har født dig i Dag"? og fremdeles: "Jeg skal være ham en Fader, og han skal være mig en Søn"?
6 Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati, “Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”
Og når han atter indfører den førstefødte i Verden, hedder det: "Og alle Guds Engle skulle tilbede ham".
7 Iye ponena za angelo akuti, “Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo, amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”
Og om Englene hedder det: "Han gør sine Engle til Vinde og sine Tjenere til Ildslue";
8 Koma za Mwana wake akuti, “Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya, ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu. (aiōn g165)
men om Sønnen: "Din Trone, o Gud! står i al Evighed, og Rettens Kongestav er dit Riges Kongestav. (aiōn g165)
9 Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”
Du elskede Retfærdighed og hadede Lovløshed, derfor har Gud, din Gud, salvet dig med Glædens Olie fremfor dine Medbrødre".
10 Mulungu akutinso, “Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi; ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
Og: "Du, Herre! har i Begyndelsen grundfæstet Jorden, og Himlene ere dine Hænders Gerninger.
11 Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire. Izo zidzatha ngati zovala.
De skulle forgå, men du bliver; og de skulle til Hobe ældes som et Klædebon,
12 Mudzazipindapinda ngati chofunda; ndipo zidzasinthidwa ngati chovala. Koma Inu simudzasintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.”
ja, som et Klæde skal du sammenrulle dem, og de skulle omskiftes; men du er den samme, og dine År skulle ikke få Ende".
13 Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti, “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditapanga adani ako kukhale chopondapo mapazi ako.”
Men til hvilken af Englene sagde han nogen Sinde: "Sæt dig ved min højre Hånd, indtil jeg får lagt dine Fjender som en Skammel for dine Fødder"?
14 Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?
Ere de ikke alle tjenende Ånder, som udsendes til Hjælp for deres Skyld, der skulle arve Frelse?

< Ahebri 1 >