< Ahebri 9 >

1 Pangano loyamba lija linali ndi malamulo okhudza chipembedzo, ndi malo opembedzeramo omangidwa ndi anthu.
Certainly, the former also had the justifications of worship and a holy place for that age.
2 Anthu ankamanga chihema. Mʼchipinda choyamba munali choyikapo nyale, tebulo ndi buledi woperekedwa kwa Mulungu. Chipinda chimenechi chinkatchedwa Malo Opatulika.
For a tabernacle was made at first, in which were the lampstand, and the table, and the bread of the Presence, which is called Holy.
3 Kuseri kwa chinsalu chotchinga chachiwiri kunkatchedwa Malo Opatulika kwambiri.
Then, beyond the second veil, was the tabernacle, which is called the Holy of Holies,
4 Mʼmenemo munali guwa lansembe lagolide lofukizirapo lubani. Munalinso Bokosi la Chipangano lokutidwa ndi golide. Mʼbokosimo munali mʼphika wagolide mʼmene ankasungiramo mana ndi ndodo ya Aaroni imene inaphuka ija, ndiponso miyala ya pangano.
having a golden censer, and the ark of the testament, covered all around and on every part with gold, in which was a golden urn containing manna, and the rod of Aaron which had blossomed, and the tablets of the testament.
5 Pamwamba pa bokosilo panali zifanizo za angelo otchedwa akerubi aulemerero, ataphimba chivundikiro cha bokosilo chimene chinali malo okhululukirapo machimo. Koma nʼzosatheka tsopano kufotokoza zinthu mwatsatanetsatane.
And over the ark were the Cherubim of glory, overshadowing the propitiatory. There is not enough time to speak about each of these things.
6 Zinthu zonsezi zitakonzedwa, ansembe ankalowamo mʼchipinda choyamba chija nthawi ndi nthawi kumatumikiramo.
Yet truly, once such things were placed together, in the first part of the tabernacle, the priests were, indeed, continually entering, so as to carry out the duties of the sacrifices.
7 Koma Mkulu wa ansembe yekha ndiye ankalowa chipinda chachiwiri chija kamodzi kokha pa chaka. Iye sankalowamo wopanda magazi. Magaziwo ankapereka nsembe kwa Mulungu chifukwa cha iye mwini ndiponso chifukwa cha machimo a anthu amene ankachita mosazindikira.
But into the second part, once a year, the high priest alone entered, not without blood, which he offered on behalf of the neglectful offenses of himself and of the people.
8 Mwa njira imeneyi Mzimu Woyera ankaonetsa kuti njira yolowera ku malo opatulika inali isanaonetsedwe pamene Chihema choyamba chinali chilipo.
In this way, the Holy Spirit is signifying that the way to what is most holy was not yet made manifest, not while the first tabernacle was still standing.
9 Zimenezi nʼzofanizira chabe, ndipo zinkalozera nthawi ino, kusonyeza kuti mphatso ndi nsembe zimene zinkaperekedwa sizinkachotsa chikumbumtima cha wopembedzayo.
And this is a parable for the present time. Accordingly, those gifts and sacrifices that are offered are not able, as concerns the conscience, to make perfect those things that serve only as food and drink,
10 Inali nkhani ya zakudya, ya zakumwa ndi ya miyambo yosiyanasiyana ya masambidwe. Anali malamulo akunja kokha mpaka pa nthawi imene anakonzanso zonse mwatsopano.
as well as the various washings and justices of the flesh, which were imposed upon them until the time of correction.
11 Koma Khristu atafika monga Mkulu wa ansembe wa zinthu zokoma zimene zilipo tsopano, Iye analowa mʼChihema chachikulu ndiponso changwiro chimene sichinamangidwe ndi munthu, ndiye kuti sichili pansi pano.
But Christ, standing as the High Priest of future good things, through a greater and more perfect tabernacle, one not made by hand, that is, not of this creation,
12 Iye sanalowemo ndi magazi ambuzi yayimuna, ana angʼombe amphongo, koma analowa Malo Opatulika kamodzi kokha ndi magazi ake, atatikonzera chipulumutso chosatha. (aiōnios g166)
entered once into the Holy of Holies, having obtained eternal redemption, neither by the blood of goats, nor of calves, but by his own blood. (aiōnios g166)
13 Ngati magazi ambuzi yayimuna, angʼombe yayimuna ndi phulusa la mwana wangʼombe wamkazi zimati zikawazidwa pa odetsedwa zimawayeretsa kotero kuti amakhala oyeretsedwa ku thupi,
For if the blood of goats and oxen, and the ashes of a calf, when these are sprinkled, sanctify those who have been defiled, in order to cleanse the flesh,
14 nʼkoposa kotani magazi a Khristu, amene mwa Mzimu wamuyaya anadzipereka yekha kwa Mulungu kukhala nsembe yopanda chilema. Iye adzayeretsa chikumbumtima chathu pochotsa ntchito za imfa, kuti ife titumikire Mulungu wamoyo. (aiōnios g166)
how much more will the blood of Christ, who through the Holy Spirit has offered himself, immaculate, to God, cleanse our conscience from dead works, in order to serve the living God? (aiōnios g166)
15 Pa chifukwa chimenechi Khristu ndi mʼkhalapakati wa pangano latsopano, kuti iwo amene anayitanidwa alandire chuma chamuyaya, pakuti Iye tsopano anafa ngati dipo lomasula iwo ku machimo amene anachita ali pansi pa pangano loyamba lija. (aiōnios g166)
And thus he is the Mediator of the new testament, so that, by his death, he intercedes for the redemption of those transgressions which were under the former testament, so that those who have been called may receive the promise of an eternal inheritance. (aiōnios g166)
16 Ngati munthu alemba pangano losiyira ena chuma, pafunika kutsimikiza kuti wolemba panganolo wamwaliradi,
For where there is a testament, it is necessary for the death of the one who testifies to intervene.
17 chifukwa pangano lotere limakhala ndi mphamvu ngati wolembayo wamwalira. Siligwira ntchito pamene wolembayo ali ndi moyo.
For a testament is confirmed by death. Otherwise, it as yet has no force, as long as the one who testifies lives.
18 Nʼchifukwa chake pangano loyamba lija silinachitike popanda kukhetsa magazi.
Therefore, indeed, the first was not dedicated without blood.
19 Mose atawawuza anthu onse malamulo, anatenga magazi a ana angʼombe amphongo ndi ambuzi yayimuna pamodzi ndi madzi, ubweya wofiira ndiponso chitsamba chotchedwa hisope, ndi kuwaza pa buku ndi anthu onse.
For when every commandment of the law had been read by Moses to the entire people, he took up the blood of calves and goats, with water and with scarlet wool and hyssop, and he sprinkled both the book itself and the entire people,
20 Iye anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Mulungu wakulamulirani kuti mulisunge.”
saying: “This is the blood of the testament which God has commanded for you.”
21 Momwemonso Mose anawaza magazi pa Chihema chija ndiponso pa zipangizo zonse zogwiritsa ntchito pa chipembedzo.
And even the tabernacle, and all the vessels for the ministry, he similarly sprinkled with blood.
22 Monga mwa malamulo titha kunena kuti, pafupifupi zinthu zonse zimayeretsedwa ndi magazi ndipo popanda kukhetsa magazi palibe kukhululukidwa machimo.
And nearly everything, according to the law, is to be cleansed with blood. And without the shedding of blood, there is no remission.
23 Tsono panafunika kuti zinthu zingofanizira zenizeni za kumwamba, ziyeretsedwe ndi nsembe zimenezi, koma zinthu za kumwamba zenizenizo kuti ziyeretsedwe panafunika nsembe zina zoposa zimenezo.
Therefore, it is necessary for the examples of heavenly things to be cleansed, just as, indeed, these things were. Yet the heavenly things are themselves better sacrifices than these.
24 Pakuti Khristu sanalowe mʼmalo opatulika omangidwa ndi anthu amene anali chifaniziro cha malo enieniwo. Iye analowa kumwamba kwenikweniko kuti azionekera pamaso pa Mulungu chifukwa cha ife.
For Jesus did not enter by means of holy things made with hands, mere examples of the true things, but he entered into Heaven itself, so that he may appear now before the face of God for us.
25 Iye sanalowe kumwamba kuti azikadziperekanso nsembe kachiwiri monga momwe mkulu wa ansembe ankachitira chaka ndi chaka ku Malo Opatulika kwambiri ndi magazi amene sanali ake.
And he did not enter so as to offer himself repeatedly, as the high priest enters into the Holy of Holies each year, with the blood of another.
26 Zikanatero bwenzi Khristu atamva zowawa kambirimbiri chilengedwere cha dziko lapansi. Koma tsopano anaoneka kamodzi kokha chifukwa cha onse pa nthawi yotsiriza kuti achotse tchimo podzipereka yekha nsembe. (aiōn g165)
Otherwise, he would need to have suffered repeatedly since the beginning of the world. But now, one time, at the consummation of the ages, he has appeared in order to destroy sin though his own sacrifice. (aiōn g165)
27 Popeza kunayikika kwa munthu kufa kamodzi ndipo kenaka kuweruzidwa,
And in the same manner as it has been appointed for men to die one time, and after this, to be judged,
28 momwemonso Khristu anadzipereka nsembe kamodzi kokha kuchotsa machimo a anthu ambiri. Ndipo Iye adzaonekanso kachiwiri, osati kudzachotsa tchimo, koma kudzapereka chipulumutso kwa amene akumudikira.
so also Christ was offered, one time, in order to empty the sins of so many. He shall appear a second time without sin, for those who await him, unto salvation.

< Ahebri 9 >