< Ahebri 8 >

1 Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba.
Now in connexion with what we have been saying the chief point is that we have a High Priest who has taken His seat at the right hand of the throne of God's Majesty in the heavens,
2 Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.
and ministers in the Holy place and in the true tabernacle which not man, but the Lord pitched.
3 Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka.
Every High Priest, however, is appointed to offer both bloodless gifts and sacrifices. Therefore this High Priest also must have some offering to present.
4 Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo.
If then He were still on earth, He would not be a priest at all, since here there are already those who present the offerings in obedience to the Law,
5 Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.”
and serve a copy and type of the heavenly things, just as Moses was divinely instructed when about to build the tabernacle. For God said, "See that you make everything in imitation of the pattern shown you on the mountain."
6 Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.
But, as a matter of fact, the ministry which Christ has obtained is all the nobler a ministry, in that He is at the same time the negotiator of a sublimer covenant, based upon sublimer promises.
7 Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake.
For if that first Covenant had been free from imperfection, there would have been no attempt to introduce another.
8 Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati, “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
For, being dissatisfied with His people, God says, "'There are days coming,' says the Lord, 'When I will establish with the house of Israel and with the house of Judah a new Covenant--
9 Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo, pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija ndipo Ine sindinawasamalire, akutero Ambuye.
a Covenant unlike the one which I made with their forefathers on the day when I took them by the hand to lead them out from the land of Egypt; for they would not remain faithful to that.' 'So I turned from them,' says the Lord.
10 Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli: Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye, Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo, ndi kulemba mʼmitima mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
'But this is the Covenant that I will covenant with the house of Israel after those days,' says the Lord: I will put My laws into their minds and will write them upon their hearts. And I will indeed be their God and they shall be My People.
11 Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake, kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye chifukwa onse adzandidziwa, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.
And there shall be no need for them to teach each one his fellow citizen and each one his brother, saying, Know the Lord. For all will know Me from the least of them to the greatest;
12 Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo, ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
Because I will be merciful to their wrongdoings, and their sins I will remember no longer.'"
13 Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.
By using the words, "a new Covenant," He has made the first one obsolete; but whatever is decaying and showing signs of old age is not far from disappearing altogether.

< Ahebri 8 >