< Ahebri 7 >

1 Melikizedeki ameneyu anali mfumu ya ku Salemu, ndiponso wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba. Anakumana ndi Abrahamu pamene ankabwerera kuchokera ku nkhondo atagonjetsa mafumu aja, Melikizedeki anakumana naye namudalitsa.
ཤཱལམསྱ རཱཛཱ སཪྻྭོཔརིསྠསྱེཤྭརསྱ ཡཱཛཀཤྩ སན྄ ཡོ ནྲྀཔཏཱིནཱཾ མཱརཎཱཏ྄ པྲཏྱཱགཏམ྄ ཨིབྲཱཧཱིམཾ སཱཀྵཱཏྐྲྀཏྱཱཤིཥཾ གདིཏཝཱན྄,
2 Ndipo Abrahamu anamupatsa chakhumi cha zonse anafunkha. Choyamba dzina la Melikizedeki likutanthauza, “Mfumu ya chilungamo,” kenakanso, “Mfumu ya Salemu,” kutanthauza, “Mfumu ya mtendere.”
ཡསྨཻ ཙེབྲཱཧཱིམ྄ སཪྻྭདྲཝྱཱཎཱཾ དཤམཱཾཤཾ དཏྟཝཱན྄ ས མལྐཱིཥེདཀ྄ སྭནཱམྣོ྅རྠེན པྲཐམཏོ དྷརྨྨརཱཛཿ པཤྩཱཏ྄ ཤཱལམསྱ རཱཛཱརྠཏཿ ཤཱནྟིརཱཛོ བྷཝཏི།
3 Alibe abambo kapena mayi, alibe chiyambi kapena chitsiriziro cha moyo wake. Iye ali ngati Mwana wa Mulungu ndipo akupitirira kukhala wansembe wamuyaya.
ཨཔརཾ ཏསྱ པིཏཱ མཱཏཱ ཝཾཤསྱ ནིརྞཡ ཨཱཡུཥ ཨཱརམྦྷོ ཛཱིཝནསྱ ཤེཥཤྩཻཏེཥཱམ྄ ཨབྷཱཝོ བྷཝཏི, ཨིཏྠཾ ས ཨཱིཤྭརཔུཏྲསྱ སདྲྀཤཱིཀྲྀཏཿ, ས ཏྭནནྟཀཱལཾ ཡཱཝད྄ ཡཱཛཀསྟིཥྛཏི།
4 Mukuona tsono kuti munthuyo anali wamkulu ndithu, pakuti Abrahamu kholo lathu anamupatsa chakhumi cha zimene anafunkha.
ཨཏཨེཝཱསྨཱཀཾ པཱུཪྻྭཔུརུཥ ཨིབྲཱཧཱིམ྄ ཡསྨཻ ལུཋིཏདྲཝྱཱཎཱཾ དཤམཱཾཤཾ དཏྟཝཱན྄ ས ཀཱིདྲྀཀ྄ མཧཱན྄ ཏད྄ ཨཱལོཙཡཏ།
5 Tsono lamulo likuti, ana a Levi amene amakhala ansembe azilandira chakhumi kuchokera kwa Aisraeli, abale awo ngakhale kuti abale awowo ndi ochokera kwa Abrahamu.
ཡཱཛཀཏྭཔྲཱཔྟཱ ལེཝེཿ སནྟཱནཱ ཝྱཝསྠཱནུསཱརེཎ ལོཀེབྷྱོ྅རྠཏ ཨིབྲཱཧཱིམོ ཛཱཏེབྷྱཿ སྭཱིཡབྷྲཱཏྲྀབྷྱོ དཤམཱཾཤགྲཧཎསྱཱདེཤཾ ལབྡྷཝནྟཿ།
6 Melikizedeki sanali wochokera kwa Levi, komabe analandira chakhumi kuchokera kwa Abrahamu nadalitsa Abrahamuyo amene analandira malonjezo a Mulungu.
ཀིནྟྭསཽ ཡདྱཔི ཏེཥཱཾ ཝཾཤཱཏ྄ ནོཏྤནྣསྟཐཱཔཱིབྲཱཧཱིམོ དཤམཱཾཤཾ གྲྀཧཱིཏཝཱན྄ པྲཏིཛྙཱནཱམ྄ ཨདྷིཀཱརིཎམ྄ ཨཱཤིཥཾ གདིཏཝཱཾཤྩ།
7 Mosakayika konse, munthu amene amadalitsa ndi wamkulu kuposa amene akudalitsidwayo.
ཨཔརཾ ཡཿ ཤྲེཡཱན྄ ས ཀྵུདྲཏརཱཡཱཤིཥཾ དདཱཏཱིཏྱཏྲ ཀོ྅པི སནྡེཧོ ནཱསྟི།
8 Ansembe amene amalandira chakhumi amafa, choncho Melikizedeki ndi wamkulu kuwaposa iwo chifukwa Malemba amamuchitira umboni kuti ndi wamoyo.
ཨཔརམ྄ ཨིདཱནཱིཾ ཡེ དཤམཱཾཤཾ གྲྀཧླནྟི ཏེ མྲྀཏྱོརདྷཱིནཱ མཱནཝཱཿ ཀིནྟུ ཏདཱནཱིཾ ཡོ གྲྀཧཱིཏཝཱན྄ ས ཛཱིཝཏཱིཏིཔྲམཱཎཔྲཱཔྟཿ།
9 Wina angathe kunena kuti Levi, amene amalandira chakhumi, anapereka chakhumicho kudzera mwa Abrahamu,
ཨཔརཾ དཤམཱཾཤགྲཱཧཱི ལེཝིརཔཱིབྲཱཧཱིམྡྭཱརཱ དཤམཱཾཤཾ དཏྟཝཱན྄ ཨེཏདཔི ཀཐཡིཏུཾ ཤཀྱཏེ།
10 chifukwa pamene Melikizedeki anakumana ndi Abrahamu nʼkuti Levi ali mʼthupi la kholo lake.
ཡཏོ ཡདཱ མལྐཱིཥེདཀ྄ ཏསྱ པིཏརཾ སཱཀྵཱཏ྄ ཀྲྀཏཝཱན྄ ཏདཱནཱིཾ ས ལེཝིཿ པིཏུརུརསྱཱསཱིཏ྄།
11 Kukanatheka kukhala wangwiro mwa unsembe wa Levi, pakuti Malamulo anapatsidwa kwa anthu mwa unsembe wa Levi, nʼchifukwa chiyani panafunikanso wansembe wina kuti abwere, wofanana ndi Melikizedeki, osati Aaroni?
ཨཔརཾ ཡསྱ སམྦནྡྷེ ལོཀཱ ཝྱཝསྠཱཾ ལབྡྷཝནྟསྟེན ལེཝཱིཡཡཱཛཀཝརྒེཎ ཡདི སིདྡྷིཿ སམབྷཝིཥྱཏ྄ ཏརྷི ཧཱརོཎསྱ ཤྲེཎྱཱ མདྷྱཱད྄ ཡཱཛཀཾ ན ནིརཱུཔྱེཤྭརེཎ མལྐཱིཥེདཀཿ ཤྲེཎྱཱ མདྷྱཱད྄ ཨཔརསྱཻཀསྱ ཡཱཛཀསྱོཏྠཱཔནཾ ཀུཏ ཨཱཝཤྱཀམ྄ ཨབྷཝིཥྱཏ྄?
12 Pakuti pamene unsembe usintha, malamulonso amayenera kusintha.
ཡཏོ ཡཱཛཀཝརྒསྱ ཝིནིམཡེན སུཏརཱཾ ཝྱཝསྠཱཡཱ ཨཔི ཝིནིམཡོ ཛཱཡཏེ།
13 Ambuye athu Yesu, amene mawuwa akunena za Iye, anali wa fuko lina, ndipo palibe aliyense wochokera fuko lakelo amene anatumikira pa guwa lansembe.
ཨཔརཉྩ ཏད྄ ཝཱཀྱཾ ཡསྱོདྡེཤྱཾ སོ྅པརེཎ ཝཾཤེན སཾཡུཀྟཱ྅སྟི ཏསྱ ཝཾཤསྱ ཙ ཀོ྅པི ཀདཱཔི ཝེདྱཱཿ ཀརྨྨ ན ཀྲྀཏཝཱན྄།
14 Pakuti nʼzodziwika bwino kuti Ambuye athu anachokera fuko la Yuda. Kunena za fuko limeneli, Mose sananenepo kanthu za ansembe.
ཝསྟུཏསྟུ ཡཾ ཝཾཤམདྷི མཱུསཱ ཡཱཛཀཏྭསྱཻཀཱཾ ཀཐཱམཔི ན ཀཐིཏཝཱན྄ ཏསྨིན྄ ཡིཧཱུདཱཝཾཤེ྅སྨཱཀཾ པྲབྷུ རྫནྨ གྲྀཧཱིཏཝཱན྄ ཨིཏི སུསྤཥྚཾ།
15 Ndipo zimene tanenazi zimamveka bwino ngati tiona kuti pafika wansembe wina wofanana ndi Melikizedeki.
ཏསྱ སྤཥྚཏརམ྄ ཨཔརཾ པྲམཱཎམིདཾ ཡཏ྄ མལྐཱིཥེདཀཿ སཱདྲྀཤྱཝཏཱཔརེཎ ཏཱདྲྀཤེན ཡཱཛཀེནོདེཏཝྱཾ,
16 Yesu sanakhale wansembe chifukwa cha malamulo monga mwa mabadwidwe ake koma mwamphamvu ya moyo wosatha.
ཡསྱ ནིརཱུཔཎཾ ཤརཱིརསམྦནྡྷཱིཡཝིདྷིཡུཀྟཡཱ ཝྱཝསྠཱཡཱ ན བྷཝཏི ཀིནྟྭཀྵཡཛཱིཝནཡུཀྟཡཱ ཤཀྟྱཱ བྷཝཏི།
17 Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn g165)
ཡཏ ཨཱིཤྭར ཨིདཾ སཱཀྵྱཾ དཏྟཝཱན྄, ཡཐཱ, "ཏྭཾ མཀླཱིཥེདཀཿ ཤྲེཎྱཱཾ ཡཱཛཀོ྅སི སདཱཏནཿ། " (aiōn g165)
18 Choncho lamulo loyamba lachotsedwa chifukwa linali lofowoka ndi lopanda phindu.
ཨནེནཱགྲཝརྟྟིནོ ཝིདྷེ དུརྦྦལཏཱཡཱ ནིཥྥལཏཱཡཱཤྩ ཧེཏོརརྠཏོ ཝྱཝསྠཡཱ ཀིམཔི སིདྡྷཾ ན ཛཱཏམིཏིཧེཏོསྟསྱ ལོཔོ བྷཝཏི།
19 Tsono Malamulo sangathe kusandutsa chilichonse kukhala changwiro, koma mʼmalo mwake mwalowa chiyembekezo chabwino, chimenechi timayandikira nacho kwa Mulungu.
ཡཡཱ ཙ ཝཡམ྄ ཨཱིཤྭརསྱ ནིཀཊཝརྟྟིནོ བྷཝཱམ ཨེཏཱདྲྀཤཱི ཤྲེཥྛཔྲཏྱཱཤཱ སཾསྠཱཔྱཏེ།
20 Izi sizinachitiketu wopanda lumbiro. Ena ankakhala ansembe popanda lumbiro.
ཨཔརཾ ཡཱིཤུཿ ཤཔཐཾ ཝིནཱ ན ནིཡུཀྟསྟསྨཱདཔི ས ཤྲེཥྛནིཡམསྱ མདྷྱསྠོ ཛཱཏཿ།
21 Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn g165)
ཡཏསྟེ ཤཔཐཾ ཝིནཱ ཡཱཛཀཱ ཛཱཏཱཿ ཀིནྟྭསཽ ཤཔཐེན ཛཱཏཿ ཡཏཿ ས ཨིདམུཀྟཿ, ཡཐཱ,
22 Chifukwa cha lumbiroli, Yesu wakhala Nkhoswe ya Pangano lopambana.
"པརམེཤ ཨིདཾ ཤེཔེ ན ཙ ཏསྨཱནྣིཝརྟྶྱཏེ། ཏྭཾ མལྐཱིཥེདཀཿ ཤྲེཎྱཱཾ ཡཱཛཀོ྅སི སདཱཏནཿ། " (aiōn g165)
23 Tsono ansembe akale aja analipo ambiri, popeza imfa imawalepheretsa kupitiriza ntchitoyi.
ཏེ ཙ བཧཝོ ཡཱཛཀཱ ཨབྷཝན྄ ཡཏསྟེ མྲྀཏྱུནཱ ནིཏྱསྠཱཡིཏྭཱཏ྄ ནིཝཱརིཏཱཿ,
24 Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn g165)
ཀིནྟྭསཱཝནནྟཀཱལཾ ཡཱཝཏ྄ ཏིཥྛཏི ཏསྨཱཏ྄ ཏསྱ ཡཱཛཀཏྭཾ ན པརིཝརྟྟནཱིཡཾ། (aiōn g165)
25 Chifukwa chake Iye amapulumutsa kwathunthu amene amabwera kwa Mulungu kudzera mwa Iyeyo. Iye ali ndi moyo nthawi zonse kuti adziwapempherera iwo.
ཏཏོ ཧེཏོ ཪྻེ མཱནཝཱསྟེནེཤྭརསྱ སནྣིདྷིཾ གཙྪནྟི ཏཱན྄ ས ཤེཥཾ ཡཱཝཏ྄ པརིཏྲཱཏུཾ ཤཀྣོཏི ཡཏསྟེཥཱཾ ཀྲྀཏེ པྲཱརྠནཱཾ ཀརྟྟུཾ ས སཏཏཾ ཛཱིཝཏི།
26 Uyu ndi Mkulu wa ansembe amene tikumufuna chifukwa ndi woyera, wopanda choyipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kuposa zonse zakumwambaku.
ཨཔརམ྄ ཨསྨཱཀཾ ཏཱདྲྀཤམཧཱཡཱཛཀསྱ པྲཡོཛནམཱསཱིད྄ ཡཿ པཝིཏྲོ ྅ཧིཾསཀོ ནིཥྐལངྐཿ པཱཔིབྷྱོ བྷིནྣཿ སྭརྒཱདཔྱུཙྩཱིཀྲྀཏཤྩ སྱཱཏ྄།
27 Kusiyana ndi akulu a ansembe ena aja, Yesu sanafunike kupereka nsembe tsiku ndi tsiku poyamba chifukwa cha machimo ake, ndipo kenaka chifukwa cha machimo a anthu ena. Iye anadzipereka nsembe chifukwa cha machimo awo kamodzi kokha pamene anadzipereka yekha.
ཨཔརཾ མཧཱཡཱཛཀཱནཱཾ ཡཐཱ ཏཐཱ ཏསྱ པྲཏིདིནཾ པྲཐམཾ སྭཔཱཔཱནཱཾ ཀྲྀཏེ ཏཏཿ པརཾ ལོཀཱནཱཾ པཱཔཱནཱཾ ཀྲྀཏེ བལིདཱནསྱ པྲཡོཛནཾ ནཱསྟི ཡཏ ཨཱཏྨབལིདཱནཾ ཀྲྀཏྭཱ ཏད྄ ཨེཀཀྲྀཏྭསྟེན སམྤཱདིཏཾ།
28 Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn g165)
ཡཏོ ཝྱཝསྠཡཱ ཡེ མཧཱཡཱཛཀཱ ནིརཱུཔྱནྟེ ཏེ དཽརྦྦལྱཡུཀྟཱ མཱནཝཱཿ ཀིནྟུ ཝྱཝསྠཱཏཿ པརཾ ཤཔཐཡུཀྟེན ཝཱཀྱེན ཡོ མཧཱཡཱཛཀོ ནིརཱུཔིཏཿ སོ ྅ནནྟཀཱལཱརྠཾ སིདྡྷཿ པུཏྲ ཨེཝ། (aiōn g165)

< Ahebri 7 >