< Ahebri 7 >
1 Melikizedeki ameneyu anali mfumu ya ku Salemu, ndiponso wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba. Anakumana ndi Abrahamu pamene ankabwerera kuchokera ku nkhondo atagonjetsa mafumu aja, Melikizedeki anakumana naye namudalitsa.
Ngoba uMelkizedeki lo, inkosi yeSalema, umpristi kaNkulunkulu oPhezukonke, owahlangabeza uAbrahama mhla ebuya ekubulaleni amakhosi, wasembusisa,
2 Ndipo Abrahamu anamupatsa chakhumi cha zonse anafunkha. Choyamba dzina la Melikizedeki likutanthauza, “Mfumu ya chilungamo,” kenakanso, “Mfumu ya Salemu,” kutanthauza, “Mfumu ya mtendere.”
uAbrahama laye wamabela okwetshumi kwakho konke; kuqala uphendulelwa ngokuthi inkosi yokulunga, emva kwalokhu besekuthiwa futhi inkosi yeSalema, okuyikuthi inkosi yokuthula;
3 Alibe abambo kapena mayi, alibe chiyambi kapena chitsiriziro cha moyo wake. Iye ali ngati Mwana wa Mulungu ndipo akupitirira kukhala wansembe wamuyaya.
engelayise, engelanina, engelasendo, engelakuqala kwensuku kumbe ukuphela kwempilo, kodwa esenziwe wafanana leNdodana kaNkulunkulu, uhlala engumpristi laphakade.
4 Mukuona tsono kuti munthuyo anali wamkulu ndithu, pakuti Abrahamu kholo lathu anamupatsa chakhumi cha zimene anafunkha.
Bonani-ke ukuthi mkhulu kangakanani lo, ngitsho uAbrahama ukhokho amnika okwetshumi kwezimpango.
5 Tsono lamulo likuti, ana a Levi amene amakhala ansembe azilandira chakhumi kuchokera kwa Aisraeli, abale awo ngakhale kuti abale awowo ndi ochokera kwa Abrahamu.
Lalabo abavela emadodaneni kaLevi abemukela ubupristi balomlayo wokwemukela okwetshumi ebantwini ngokomthetho, okuyikuthi kubafowabo, lanxa bevela ekhalweni lukaAbrahama;
6 Melikizedeki sanali wochokera kwa Levi, komabe analandira chakhumi kuchokera kwa Abrahamu nadalitsa Abrahamuyo amene analandira malonjezo a Mulungu.
kodwa yena ongabalelwa osendweni lwabo, wemukela okwetshumi kuAbrahama, wasembusisa lowo owayelezithembiso.
7 Mosakayika konse, munthu amene amadalitsa ndi wamkulu kuposa amene akudalitsidwayo.
Njalo kungelakuphikwa ngitsho ukuthi: Omncinyane ubusiswa ngomkhulu.
8 Ansembe amene amalandira chakhumi amafa, choncho Melikizedeki ndi wamkulu kuwaposa iwo chifukwa Malemba amamuchitira umboni kuti ndi wamoyo.
Lapha-ke abantu abafayo bemukela okwetshumi; kodwa lapho esemukela lowo okufakazwa ngaye ukuthi uyaphila.
9 Wina angathe kunena kuti Levi, amene amalandira chakhumi, anapereka chakhumicho kudzera mwa Abrahamu,
Kungatshiwo-ke, uLevi laye owemukela okwetshumi wanikela okwetshumi ngoAbrahama;
10 chifukwa pamene Melikizedeki anakumana ndi Abrahamu nʼkuti Levi ali mʼthupi la kholo lake.
ngoba wayesesekhalweni lukayise, mhla uMelkizedeki emhlangabeza.
11 Kukanatheka kukhala wangwiro mwa unsembe wa Levi, pakuti Malamulo anapatsidwa kwa anthu mwa unsembe wa Levi, nʼchifukwa chiyani panafunikanso wansembe wina kuti abwere, wofanana ndi Melikizedeki, osati Aaroni?
Ngakho-ke uba kwakukhona ukuphelela ngobupristi bukaLevi (ngoba isizwe sanikwa umlayo ngaphansi kwabo), kwakusaswelekelani ukuthi kuvele omunye umpristi ngokohlobo lukaMelkizedeki, lokungatshiwo ngokwendlela kaAroni?
12 Pakuti pamene unsembe usintha, malamulonso amayenera kusintha.
Ngoba uba ubupristi buphendulwa, kuyadingeka ukuthi kube khona lokuphendulwa komlayo.
13 Ambuye athu Yesu, amene mawuwa akunena za Iye, anali wa fuko lina, ndipo palibe aliyense wochokera fuko lakelo amene anatumikira pa guwa lansembe.
Ngoba lowo okukhulunywa ngaye lezizinto ungowesinye isizwe, okungabanga khona kuso owanakekela ilathi.
14 Pakuti nʼzodziwika bwino kuti Ambuye athu anachokera fuko la Yuda. Kunena za fuko limeneli, Mose sananenepo kanthu za ansembe.
Ngoba kusobala ukuthi iNkosi yethu yavela koJuda, isizwe uMozisi angakhulumanga lutho ngaso mayelana lobupristi.
15 Ndipo zimene tanenazi zimamveka bwino ngati tiona kuti pafika wansembe wina wofanana ndi Melikizedeki.
Njalo kusesobala ngokwengezelelwe kakhulu, uba sekusima omunye umpristi njengokofuzo lukaMelkizedeki,
16 Yesu sanakhale wansembe chifukwa cha malamulo monga mwa mabadwidwe ake koma mwamphamvu ya moyo wosatha.
ongenziwanga ngokomthetho wesimiso senyama, kodwa ngokwamandla empilo engelakuphela;
17 Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn )
ngoba ufakaza esithi: Wena ungumpristi kuze kube nininini ngokohlobo lukaMelkizedeki. (aiōn )
18 Choncho lamulo loyamba lachotsedwa chifukwa linali lofowoka ndi lopanda phindu.
Ngoba ukubekwa eceleni komthetho wokuqala kwenziwa ngenxa yobuthakathaka lokungasizi lutho kwawo;
19 Tsono Malamulo sangathe kusandutsa chilichonse kukhala changwiro, koma mʼmalo mwake mwalowa chiyembekezo chabwino, chimenechi timayandikira nacho kwa Mulungu.
ngoba umlayo kawuzanga wenze ulutho luphelele, kodwa uyisingeniso sethemba elingcono, esisondela ngalo kuNkulunkulu.
20 Izi sizinachitiketu wopanda lumbiro. Ena ankakhala ansembe popanda lumbiro.
Njalo okungangokuthi kenziwanga ngaphandle kwesifungo,
21 Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn )
(ngoba bona baba ngabapristi ngaphandle kwesifungo, kodwa yena ngesifungo, ngalowo owathi kuye: INkosi yafunga njalo kayiyikuzisola yathi: Wena ungumpristi kuze kube nininini ngokohlobo lukaMelkizedeki; ) (aiōn )
22 Chifukwa cha lumbiroli, Yesu wakhala Nkhoswe ya Pangano lopambana.
ngalokho uJesu waba yisibambiso sesivumelwano esingcono.
23 Tsono ansembe akale aja analipo ambiri, popeza imfa imawalepheretsa kupitiriza ntchitoyi.
Lalabo babebanengi ababa ngabapristi, ngoba bavinjelwa yikufa ukuthi bahlale njalo;
24 Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn )
kodwa lo, ngenxa yokuthi uhlala kuze kube phakade, ulobupristi obungadluliyo. (aiōn )
25 Chifukwa chake Iye amapulumutsa kwathunthu amene amabwera kwa Mulungu kudzera mwa Iyeyo. Iye ali ndi moyo nthawi zonse kuti adziwapempherera iwo.
Ngenxa yalokho laye ulamandla okusindisa ngokupheleleyo abeza kuNkulunkulu ngaye, lokhu ephilela njalo ukubanxusela.
26 Uyu ndi Mkulu wa ansembe amene tikumufuna chifukwa ndi woyera, wopanda choyipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kuposa zonse zakumwambaku.
Ngoba umpristi omkhulu onjalo usifanele, ongcwele, ongelacala, ongelasici, owehlukaniswe lezoni, lowenziwa waphakama kulamazulu;
27 Kusiyana ndi akulu a ansembe ena aja, Yesu sanafunike kupereka nsembe tsiku ndi tsiku poyamba chifukwa cha machimo ake, ndipo kenaka chifukwa cha machimo a anthu ena. Iye anadzipereka nsembe chifukwa cha machimo awo kamodzi kokha pamene anadzipereka yekha.
ongadingi insuku ngensuku, njengabapristi abakhulu, ukunikela imihlatshelo esenzela ezakhe izono kuqala, emva kwalokho ezabantu; ngoba lokho wakwenza kanye mhla ezinikela yena.
28 Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn )
Ngoba umlayo uyamisa abantu babe ngabapristi abakhulu, abalobuthakathaka; kodwa ilizwi lesifungo elalandela umlayo lamisa iNdodana ephelelisiweyo kuze kube nininini. (aiōn )