< Ahebri 7 >

1 Melikizedeki ameneyu anali mfumu ya ku Salemu, ndiponso wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba. Anakumana ndi Abrahamu pamene ankabwerera kuchokera ku nkhondo atagonjetsa mafumu aja, Melikizedeki anakumana naye namudalitsa.
Thi denne Melkisedek, Konge i Salem, den højeste Guds Præst, som gik Abraham i Møde, da han vendte tilbage fra Kongernes Nederlag, og velsignede ham,
2 Ndipo Abrahamu anamupatsa chakhumi cha zonse anafunkha. Choyamba dzina la Melikizedeki likutanthauza, “Mfumu ya chilungamo,” kenakanso, “Mfumu ya Salemu,” kutanthauza, “Mfumu ya mtendere.”
hvem også Abraham gav Tiende af alt, og som, når hans Navn udlægges, først er Retfærdigheds Konge, dernæst også Salems Konge, det er: Freds Konge,
3 Alibe abambo kapena mayi, alibe chiyambi kapena chitsiriziro cha moyo wake. Iye ali ngati Mwana wa Mulungu ndipo akupitirira kukhala wansembe wamuyaya.
uden Fader, uden Moder, uden Slægtregister, uden Dages Begyndelse og uden Livs Ende, men gjort lig med Guds Søn, - han forbliver Præst for bestandig.
4 Mukuona tsono kuti munthuyo anali wamkulu ndithu, pakuti Abrahamu kholo lathu anamupatsa chakhumi cha zimene anafunkha.
Ser dog, hvor stor denne er, hvem endog Patriarken Abraham gav Tiende af Byttet.
5 Tsono lamulo likuti, ana a Levi amene amakhala ansembe azilandira chakhumi kuchokera kwa Aisraeli, abale awo ngakhale kuti abale awowo ndi ochokera kwa Abrahamu.
Og hine, som, idet de høre til Levi Sønner, få Præstedømmet, have et Bud om at tage Tiende efter Loven af Folket, det er af deres Brødre, endskønt disse ere udgåede af Abrahams Lænd;
6 Melikizedeki sanali wochokera kwa Levi, komabe analandira chakhumi kuchokera kwa Abrahamu nadalitsa Abrahamuyo amene analandira malonjezo a Mulungu.
men han, som ikke regner sin Slægt fra dem, har taget Tiende af Abraham og har velsignet den, som havde Forjættelserne.
7 Mosakayika konse, munthu amene amadalitsa ndi wamkulu kuposa amene akudalitsidwayo.
Men uden al Modsigelse er det den ringere, som velsignes af den ypperligere.
8 Ansembe amene amalandira chakhumi amafa, choncho Melikizedeki ndi wamkulu kuwaposa iwo chifukwa Malemba amamuchitira umboni kuti ndi wamoyo.
Og her er det dødelige Mennesker, som tager Tiende; men der er det en, om hvem der vidnes, at han lever.
9 Wina angathe kunena kuti Levi, amene amalandira chakhumi, anapereka chakhumicho kudzera mwa Abrahamu,
Ja, så at sige, har endog Levi, som tager Tiende, igennem Abraham givet Tiende;
10 chifukwa pamene Melikizedeki anakumana ndi Abrahamu nʼkuti Levi ali mʼthupi la kholo lake.
thi han var endnu i Faderens Lænd, da Melkisedek gik denne i Møde.
11 Kukanatheka kukhala wangwiro mwa unsembe wa Levi, pakuti Malamulo anapatsidwa kwa anthu mwa unsembe wa Levi, nʼchifukwa chiyani panafunikanso wansembe wina kuti abwere, wofanana ndi Melikizedeki, osati Aaroni?
Hvis der altså var Fuldkommelse at få ved det levitiske Præstedømme (thi på Grundlag af dette har jo Folket fået Loven), hvilken Trang var der da yderligere til, at en anden Slags Præst skulde opstå efter Melkisedeks Vis og ikke nævnes efter Arons Vis?
12 Pakuti pamene unsembe usintha, malamulonso amayenera kusintha.
Når nemlig Præstedømmet omskiftes, sker der med Nødvendighed også en Omskiftelse af Loven.
13 Ambuye athu Yesu, amene mawuwa akunena za Iye, anali wa fuko lina, ndipo palibe aliyense wochokera fuko lakelo amene anatumikira pa guwa lansembe.
Thi han, om hvem dette siges, har hørt til en anden Stamme, af hvilken ingen har taget Vare på Alteret.
14 Pakuti nʼzodziwika bwino kuti Ambuye athu anachokera fuko la Yuda. Kunena za fuko limeneli, Mose sananenepo kanthu za ansembe.
thi det er vitterligt, at af Juda er vor Herre oprunden, og for den Stammes Vedkommende har Moses intet talt om Præster.
15 Ndipo zimene tanenazi zimamveka bwino ngati tiona kuti pafika wansembe wina wofanana ndi Melikizedeki.
Og det bliver end ydermere klart, når der i Lighed med Melkisedek opstår en anden Slags Præst,
16 Yesu sanakhale wansembe chifukwa cha malamulo monga mwa mabadwidwe ake koma mwamphamvu ya moyo wosatha.
som ikke er bleven det efter et kødeligt Buds Lov, men efter et uopløseligt Livs Kraft.
17 Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn g165)
Thi han får det Vidnesbyrd: "Du er Præst til evig Tid efter Melkisedeks Vis." (aiōn g165)
18 Choncho lamulo loyamba lachotsedwa chifukwa linali lofowoka ndi lopanda phindu.
Thi vel sker der Ophævelse af et forudgående Bud, fordi det var svagt og unyttigt
19 Tsono Malamulo sangathe kusandutsa chilichonse kukhala changwiro, koma mʼmalo mwake mwalowa chiyembekezo chabwino, chimenechi timayandikira nacho kwa Mulungu.
(thi Loven har ikke fuldkommet noget); men der sker Indførelse af et bedre Håb, ved hvilket vi nærme os til Gud.
20 Izi sizinachitiketu wopanda lumbiro. Ena ankakhala ansembe popanda lumbiro.
Og så vist som det ikke er sket uden Ed,
21 Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn g165)
(thi hine ere blevne Præster uden Ed, men denne med Ed, ved den, som siger til ham: "Herren svor, og han skal ikke angre det: Du er Præst til evig Tid"): (aiōn g165)
22 Chifukwa cha lumbiroli, Yesu wakhala Nkhoswe ya Pangano lopambana.
så vist er Jesus bleven Borgen for en bedre Pagt.
23 Tsono ansembe akale aja analipo ambiri, popeza imfa imawalepheretsa kupitiriza ntchitoyi.
Og hine ere blevne Præster, flere efter hinanden, fordi de ved Døden hindredes i at vedblive;
24 Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn g165)
men denne har et uforgængeligt Præstedømme, fordi han bliver til evig Tid, (aiōn g165)
25 Chifukwa chake Iye amapulumutsa kwathunthu amene amabwera kwa Mulungu kudzera mwa Iyeyo. Iye ali ndi moyo nthawi zonse kuti adziwapempherera iwo.
hvorfor han også kan fuldkomment frelse dem, som komme til Gud ved ham, efterdi han lever altid til at gå i Forbøn for dem.
26 Uyu ndi Mkulu wa ansembe amene tikumufuna chifukwa ndi woyera, wopanda choyipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kuposa zonse zakumwambaku.
Thi en sådan Ypperstepræst var det også, som sømmede sig for os, en from, uskyldig, ubesmittet, adskilt fra Syndere og ophøjet over Himlene;
27 Kusiyana ndi akulu a ansembe ena aja, Yesu sanafunike kupereka nsembe tsiku ndi tsiku poyamba chifukwa cha machimo ake, ndipo kenaka chifukwa cha machimo a anthu ena. Iye anadzipereka nsembe chifukwa cha machimo awo kamodzi kokha pamene anadzipereka yekha.
en, som ikke hver Dag har nødig, som Ypperstepræsterne, at frembære Ofre først for sine egne Synder, derefter for Folkets; thi dette gjorde han een Gang for alle, da han ofrede sig selv.
28 Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn g165)
Thi Loven indsætter til Ypperstepræster Mennesker, som have Skrøbelighed; men Edens Ord, som kom senere end Loven, indsætter en Søn, som er fuldkommet til evig Tid: (aiōn g165)

< Ahebri 7 >