< Ahebri 6 >
1 Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu,
therefore to release: leave the/this/who the/this/who beginning the/this/who Christ word upon/to/against the/this/who perfection to bear/lead not again foundation to lay/throw down repentance away from dead work and faith upon/to/against God
2 za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios )
baptism (teaching *NK(o)*) laying on and/both hand resurrection and/both dead and judgment eternal (aiōnios )
3 Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.
and this/he/she/it (to do/make: do *NK(o)*) if indeed to permit the/this/who God
4 Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera.
unable for the/this/who once to illuminate to taste and/both the/this/who free gift the/this/who heavenly and partaker to be spirit/breath: spirit holy
5 Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn )
and good to taste God declaration power and/both to ensue an age: age (aiōn )
6 Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.
and to defect again to restore toward repentance to recrucify themself the/this/who son the/this/who God and to disgrace
7 Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa.
earth: country for the/this/who to drink the/this/who upon/to/against it/s/he to come/go often rain and to give birth to crop suitable that through/because of which and to farm to partake praise away from the/this/who God
8 Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.
to bring/carry out then a thorn and thistle failing and curse near which the/this/who goal/tax toward burning
9 Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso.
to persuade then about you beloved the/this/who greater and to have/be salvation if: even though and thus(-ly) to speak
10 Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano.
no for unjust the/this/who God to forget the/this/who work you and (the/this/who labor *K*) the/this/who love which to show toward the/this/who name it/s/he to serve the/this/who holy: saint and to serve
11 Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera.
to long for then each you the/this/who it/s/he to show diligence to/with the/this/who assurance the/this/who hope until goal/tax
12 Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.
in order that/to not dull to be imitator then the/this/who through/because of faith and patience to inherit the/this/who promise
13 Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti,
the/this/who for Abraham to profess the/this/who God since according to none to have/be great to swear to swear according to themself
14 “Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
to say (if: surely *N(k)O*) certainly to praise/bless to praise/bless you and to multiply to multiply you
15 Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.
and thus(-ly) to have patience to obtain the/this/who promise
16 Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse.
a human (on the other hand *k*) for according to the/this/who great to swear and all it/s/he dispute end toward confirmation the/this/who oath
17 Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro.
in/on/among which more excessive to plan the/this/who God to show/prove the/this/who heir the/this/who promise the/this/who unchangeable the/this/who plan it/s/he to guarantee oath
18 Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira.
in order that/to through/because of two thing unchangeable in/on/among which unable to lie (the/this/who *n*) God strong encouragement to have/be the/this/who to flee to grasp/seize the/this/who to set before hope
19 Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga.
which as/when anchor to have/be the/this/who soul secure and/both and firm and to enter toward the/this/who inner the/this/who curtain
20 Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn )
where(-ever) forerunner above/for me to enter Jesus according to the/this/who order Melchizedek high-priest to be toward the/this/who an age: eternity (aiōn )