< Ahebri 5 >
1 Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuchokera pakati pa anthu ndipo amayikidwa kuti aziwayimirira pamaso pa Mulungu, kuti azipereka mphatso ndi nsembe chifukwa cha machimo.
Thi hver Ypperstepræst tages iblandt Mennesker og indsættes for Mennesker til Tjenesten for Gud, for at han skal frembære baade Gaver og Slagtofre for Synder,
2 Popeza kuti iye mwini ali ndi zofowoka zake, amatha kuwalezera mtima amene ali osadziwa ndi osochera.
som en, der kan bære over med de vankundige og vildfarende, eftersom han ogsaa selv er stedt i Skrøbelighed
3 Chifukwa cha ichi, iye amadziperekera nsembe chifukwa cha machimo ake omwe ndiponso chifukwa cha machimo a anthu ena.
og for dens Skyld maa frembære Syndoffer, som for Folket saaledes ogsaa for sig selv.
4 Palibe amene amadzipatsa yekha ulemu wotere, koma amachita kuyitanidwa ndi Mulungu monga momwe anayitanidwira Aaroni.
Og ingen tager sig selv den Ære, men han kaldes af Gud, ligesom jo ogsaa Aron.
5 Nʼchifukwa chake Khristu sanadzipatse yekha ulemu wokhala Mkulu wa ansembe. Koma Mulungu anamuwuza kuti, “Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.”
Saaledes har ej heller Kristus tillagt sig selv den Ære at blive Ypperstepræst, men den, som sagde til ham: „Du er min Søn, jeg har født dig i Dag,”
6 Ndipo penanso anati, “Iwe ndiwe wansembe mpaka muyaya, monga mwa unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn )
som han jo ogsaa siger et andet Sted: „Du er Præst til evig Tid, efter Melkisedeks Vis,” (aiōn )
7 Yesu, pa nthawi imene anali munthu pa dziko lapansi pano, anapereka mapemphero ake ndi zopempha mofuwula ndi misozi kwa Iye amene akanamupulumutsa ku imfa, ndipo anamumvera chifukwa anagonjera modzipereka.
han, som i sit Køds Dage med stærkt Raab og Taarer frembar Bønner og ydmyge Begæringer til den, der kunde frelse ham fra Døden, og blev bønhørt i sin Angest,
8 Ngakhale Iye anali Mwana wa Mulungu anaphunzira kumvera pomva zowawa.
og saaledes, endskønt han var Søn, lærte han Lydighed af det, han led,
9 Atasanduka wangwiro kotheratu, anakhala gwero la chipulumutso chosatha kwa onse omvera Iye. (aiōnios )
og efter at være fuldkommet blev Aarsag til evig Frelse for alle dem, som lyde ham, (aiōnios )
10 Ndipo Mulungu anamuyika kukhala Mkulu wa ansembe, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.
idet han af Gud blev kaldt Ypperstepræst efter Melkisedeks Vis.
11 Tili ndi zambiri zoti tinganene pa zimenezi, koma ndi zovuta kukufotokozerani chifukwa ndinu ochedwa kuphunzira.
Herom have vi meget at sige, og det er vanskeligt at forklare, efterdi I ere blevne sløve til at høre.
12 Ngakhale kuti pa nthawi ino munayenera kukhala aphunzitsi, pakufunikabe munthu wina kuti abwerezenso kudzakuphunzitsani maphunziro oyambira a choonadi cha Mulungu. Ndinu ofunika mkaka osati chakudya cholimba!
Thi skønt I efter Tiden endog burde være Lærere, trænge I atter til, at man skal lære eder Begyndelsesgrundene i Guds Ord, og I ere blevne saadanne, som trænge til Mælk og ikke til fast Føde.
13 Aliyense amene amangodya mkaka okha, akanali mwana wakhanda, sakudziwa bwino chiphunzitso cha chilungamo.
Thi hver, som faar Mælk, er ukyndig i den rette Tale, thi han er spæd;
14 Koma chakudya cholimba ndi cha anthu okhwima msinkhu, amene pogwiritsa ntchito nzeru zawo, aphunzira kusiyanitsa chabwino ndi choyipa.
men for de fuldkomne er den faste Føde, for dem, som paa Grund af deres Erfaring have Sanserne øvede til at skelne mellem godt og ondt.