< Ahebri 4 >

1 Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo.
Lader os derfor, da der endnu står en Forjættelse tilbage om at indgå til hans Hvile, vogte os for, at nogen af eder skal mene, at han er kommen for silde.
2 Pakuti Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa ife, monganso iwo aja; koma iwo sanapindule nawo uthengawo chifukwa anangomva koma osakhulupirira.
Thi også os er der forkyndt godt Budskab ligesom hine; men Ordet, som de hørte, hjalp ikke dem, fordi det ikke var forenet med Troen hos dem, som hørte det.
3 Tsono ife amene takhulupirira talowa mu mpumulo, monga momwe Mulungu akunenera kuti, “Ndili wokwiya ndinalumbira kuti, ‘Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.’” Ananena zimenezi ngakhale anali atatsiriza kale ntchito yolenga dziko lapansi.
Thi vi gå ind til Hvilen, vi, som ere komne til Troen, efter hvad han har sagt: "Så svor jeg i min Vrede: Sandelig, de skulle ikke gå ind til min Hvile", omendskønt Gerningerne vare fuldbragte fra Verdens Grundlæggelse.
4 Pena pake wayankhula za tsiku lachisanu ndi chiwiri mʼmawu awa: “Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, Mulungu anapumula ku ntchito zake zonse.”
Thi han har et Sted sagt om den syvende Dag således: "Og Gud hvilede på den syvende Dag fra alle sine Gerninger."
5 Pa ndime inonso akunena za zomwezo pamene akuti, “Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.”
Og fremdeles på dette Sted: "Sandelig, de skulle ikke gå ind til min Hvile."
6 Popeza kwatsalabe kuti ena adzalowe mu mpumulowo, koma aja anayamba kumva Uthenga Wabwino sanalowe chifukwa cha kusamvera kwawo.
Efterdi der altså står tilbage, at nogle skulle gå ind til den, og de, hvem der først blev forkyndt godt Budskab, ikke gik ind for deres Genstridigheds Skyld:
7 Nʼchifukwa chake Mulungu anayikanso tsiku lina limene analitcha “Lero.” Patapita nthawi yayitali Iye anayankhula za tsiku lomweli kudzera mwa Davide, monga ndinanena kale kuti, “Lero mukamva mawu ake, musawumitse mitima yanu.”
så bestemmer han atter en Dag: "I Dag", siger han ved David så lang Tid efter, (som ovenfor sagt): "I Dag, når I høre hans Røst, da forhærder ikke eders Hjerter!"
8 Ngati Yoswa akanalowetsa anthu mu mpumulo, Mulungu sakananena pambuyo pake za tsiku lina.
Thi dersom Josva havde skaffet dem Hvile, da vilde han ikke tale om en anden Dag siden efter.
9 Kotero tsono kwatsala mpumulo wa Sabata kwa anthu a Mulungu;
Altså er der en Sabbatshvile tilbage for Guds Folk.
10 Pakuti aliyense amene analowa mu mpumulo wa Mulungu anapuma pa ntchito zake, monga momwe Mulungu anachitira.
Thi den, som er gået ind til hans Hvile, også han har fået Hvile fra sine Gerninger, ligesom Gud fra sine.
11 Tiyeni tsono tiyesetse kulowa mu mpumulo, kuti pasapezeke wina aliyense wolephera potsatira chitsanzo chawo cha kusamvera.
Lader os derfor gøre os Flid for at gå ind til hin Hvile, for at ikke nogen skal falde ved den samme Genstridighed, som hine gave Eksempel på.
12 Paja Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amalowa mpaka molumikizirana moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana fundo ndi mafuta a mʼmafupa. Amaweruza malingaliro ndi zokhumba za mʼmitima.
Thi Guds Ord er levende og kraftigt og skarpere end noget tveægget Sværd og trænger igennem, indtil det deler Sjæl og Ånd, Ledemod såvel som Marv, og dømmer over Hjertets Tanker og Råd.
13 Palibe kanthu kobisika pamaso pa Mulungu. Zinthu zonse zili poyera ndi zovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.
Og ingen Skabning er usynlig for hans Åsyn; men alle Ting ere nøgne og udspændte for hans Øjne, hvem vi stå til Regnskab.
14 Popeza kuti tili ndi Mkulu wa ansembe wopambana, amene analowa kale kumwamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tiyeni tigwiritsitse chikhulupiriro chathu chimene timavomereza.
Efterdi vi altså have en stor Ypperstepræst, som er gået igennem Himlene, Jesus, Guds Søn, da lader os holde fast ved Bekendelsen!
15 Pakuti sitili ndi Mkulu wa ansembe amene sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofowoka zathu. Koma tili naye amene anayesedwa mʼnjira zonse monga ife, koma sanachimwe.
Thi vi have ikke en Ypperstepræst, som ej kan have Medlidenhed med vore Skrøbeligheder, men en sådan, som er fristet i alle Ting i Lighed med os, dog uden Synd.
16 Tiyeni tsono tiyandikire ku mpando waufumu, wachisomo mopanda mantha, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo chotithandiza pa nthawi yeniyeni.
Derfor lader os træde frem med Frimodighed for Nådens Trone, for at vi kunne få Barmhjertighed og finde Nåde til betimelig Hjælp.

< Ahebri 4 >