< Ahebri 4 >

1 Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo.
Lader os derfor, da der endnu staar en Forjættelse tilbage om at indgaa til hans Hvile, vogte os for, at nogen af eder skal mene, at han er kommen for silde.
2 Pakuti Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa ife, monganso iwo aja; koma iwo sanapindule nawo uthengawo chifukwa anangomva koma osakhulupirira.
Thi ogsaa os er der forkyndt godt Budskab ligesom hine; men Ordet, som de hørte, hjalp ikke dem, fordi det ikke var forenet med Troen hos dem, som hørte det.
3 Tsono ife amene takhulupirira talowa mu mpumulo, monga momwe Mulungu akunenera kuti, “Ndili wokwiya ndinalumbira kuti, ‘Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.’” Ananena zimenezi ngakhale anali atatsiriza kale ntchito yolenga dziko lapansi.
Thi vi gaa ind til Hvilen, vi, som ere komne til Troen, efter hvad han har sagt: „Saa svor jeg i min Vrede: Sandelig, de skulle ikke gaa ind til min Hvile,” omendskønt Gerningerne vare fuldbragte fra Verdens Grundlæggelse.
4 Pena pake wayankhula za tsiku lachisanu ndi chiwiri mʼmawu awa: “Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, Mulungu anapumula ku ntchito zake zonse.”
Thi han har et Sted sagt om den syvende Dag saaledes: „Og Gud hvilede paa den syvende Dag fra alle sine Gerninger.”
5 Pa ndime inonso akunena za zomwezo pamene akuti, “Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.”
Og fremdeles paa dette Sted: „Sandelig, de skulle ikke gaa ind til min Hvile.”
6 Popeza kwatsalabe kuti ena adzalowe mu mpumulowo, koma aja anayamba kumva Uthenga Wabwino sanalowe chifukwa cha kusamvera kwawo.
Efterdi der altsaa staar tilbage, at nogle skulle gaa ind til den, og de, hvem der først blev forkyndt godt Budskab, ikke gik ind for deres Genstridigheds Skyld:
7 Nʼchifukwa chake Mulungu anayikanso tsiku lina limene analitcha “Lero.” Patapita nthawi yayitali Iye anayankhula za tsiku lomweli kudzera mwa Davide, monga ndinanena kale kuti, “Lero mukamva mawu ake, musawumitse mitima yanu.”
Saa bestemmer han atter en Dag: „I Dag,” siger han ved David lang Tid efter, (som ovenfor sagt): „I Dag, naar I høre hans Røst, da forhærder ikke eders Hjerter!”
8 Ngati Yoswa akanalowetsa anthu mu mpumulo, Mulungu sakananena pambuyo pake za tsiku lina.
Thi dersom Josva havde skaffet dem Hvile, da Vilde han ikke tale om en anden Dag siden efter.
9 Kotero tsono kwatsala mpumulo wa Sabata kwa anthu a Mulungu;
Altsaa er der en Sabbatshvile tilbage for Guds Folk.
10 Pakuti aliyense amene analowa mu mpumulo wa Mulungu anapuma pa ntchito zake, monga momwe Mulungu anachitira.
Thi den, som er gaaet ind til hans Hvile, Ogsaa han har faaet Hvile fra sine Gerninger, ligesom Gud fra sine.
11 Tiyeni tsono tiyesetse kulowa mu mpumulo, kuti pasapezeke wina aliyense wolephera potsatira chitsanzo chawo cha kusamvera.
Lader os derfor gøre os Flid for at gaa ind til hin Hvile, for at ikke nogen skal falde ved den samme Genstridighed, som hine gave Eksempel paa.
12 Paja Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amalowa mpaka molumikizirana moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana fundo ndi mafuta a mʼmafupa. Amaweruza malingaliro ndi zokhumba za mʼmitima.
Thi Guds Ord er levende og kraftigt og skarpere end noget tveægget Sværd og trænger igennem, indtil det deler Sjæl og Aand, Ledemod saavel som Marv, og dømmer over Hjertets Tanker og Raad.
13 Palibe kanthu kobisika pamaso pa Mulungu. Zinthu zonse zili poyera ndi zovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.
Og ingen Skabning er usynlig for hans Aasyn; men alle Ting ere nøgne og udspændte for hans Øjne, hvem vi staa til Regnskab.
14 Popeza kuti tili ndi Mkulu wa ansembe wopambana, amene analowa kale kumwamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tiyeni tigwiritsitse chikhulupiriro chathu chimene timavomereza.
Efterdi vi altsaa have en stor Ypperstepræst, som er gaaet igennem Himlene, Jesus, Guds Søn, da lader os holde fast ved Bekendelsen!
15 Pakuti sitili ndi Mkulu wa ansembe amene sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofowoka zathu. Koma tili naye amene anayesedwa mʼnjira zonse monga ife, koma sanachimwe.
Thi vi have ikke en Ypperstepræst, som ej kan have Medlidenhed med vore Skrøbeligheder, men en saadan, som er fristet i alle Ting i Lighed med os, dog uden Synd.
16 Tiyeni tsono tiyandikire ku mpando waufumu, wachisomo mopanda mantha, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo chotithandiza pa nthawi yeniyeni.
Derfor lader os træde frem med Frimodighed for Naadens Trone, for at vi kunne faa Barmhjertighed og finde Naade til betimelig Hjælp.

< Ahebri 4 >