< Ahebri 4 >
1 Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo.
Hatdawkvah, Cathut e kâhatnae dawk kâen thainae a lawkkam ao nahlangva, nangmouh thung dawk hoi kâen laipalah tami buet touh hai ao hoeh nahanlah kâhruetcuet awh sei.
2 Pakuti Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa ife, monganso iwo aja; koma iwo sanapindule nawo uthengawo chifukwa anangomva koma osakhulupirira.
Bangkongtetpawiteh, maimouh haiyah ahnimanaw patetvanlah kamthang kahawi hah thai awh toe. Hatei, ahnimouh ni a thai awh e kamthang lawk teh ahnimae thungvah, yuemnae hoi a kâkalawt hoeh dawkvah aphu awmhoeh.
3 Tsono ife amene takhulupirira talowa mu mpumulo, monga momwe Mulungu akunenera kuti, “Ndili wokwiya ndinalumbira kuti, ‘Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.’” Ananena zimenezi ngakhale anali atatsiriza kale ntchito yolenga dziko lapansi.
Ka yuem e maimanaw teh Cathut e kâhatnae dawk kâen awh. Cakathoung dawk, Ahnimouh teh kaie kâhatnae dawk kâen mahoeh telah ka lungkhuek teh thoe ka bo e patetlah ao. Hatei, athawnaw teh talaivan kamtawng nah a cum e lah ao toe.
4 Pena pake wayankhula za tsiku lachisanu ndi chiwiri mʼmawu awa: “Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, Mulungu anapumula ku ntchito zake zonse.”
Asari hnin hoi kâkuen lah, Cathut ni hno pueng koung a cum hnukkhu, asari hnin vah duem a kâhat telah Cakathoung ni hmuen buet touh koe a dei.
5 Pa ndime inonso akunena za zomwezo pamene akuti, “Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.”
Hahoi, ahnimouh teh kaie kâhatnae dawk kâen awh mahoeh, telah bout a ti.
6 Popeza kwatsalabe kuti ena adzalowe mu mpumulowo, koma aja anayamba kumva Uthenga Wabwino sanalowe chifukwa cha kusamvera kwawo.
Hatdawkvah, hote kâhatnae thungvah kâen thainae teh, atangawnnaw hanelah ao rah. Lunghawinae kamthang kahawi teh hmaloe ka thai e naw ni a yuem awh hoeh dawkvah kâen awh hoeh toe.
7 Nʼchifukwa chake Mulungu anayikanso tsiku lina limene analitcha “Lero.” Patapita nthawi yayitali Iye anayankhula za tsiku lomweli kudzera mwa Davide, monga ndinanena kale kuti, “Lero mukamva mawu ake, musawumitse mitima yanu.”
Hatdawkvah, Cathut ni hnin hnin touh hah sahnin telah a dei teh a kum moi asaw hnukkhu, ahmaloe a dei e patetlah sahnin a lawk na thai awh pawiteh, na lungpata sak awh hanh telah Devit hno lahoi a dei.
8 Ngati Yoswa akanalowetsa anthu mu mpumulo, Mulungu sakananena pambuyo pake za tsiku lina.
Joshua ni ahnimouh kâhatnae poe katang pawiteh, hat hnukkhu, alouke hnin hah Cathut ni a dei han namaw.
9 Kotero tsono kwatsala mpumulo wa Sabata kwa anthu a Mulungu;
Hatdawkvah, Cathut e miphunnaw hanlah kâhatnae phun touh ao rah.
10 Pakuti aliyense amene analowa mu mpumulo wa Mulungu anapuma pa ntchito zake, monga momwe Mulungu anachitira.
Bangkongtetpawiteh, Cathut ni athawnaw hah a cum teh duem a kâhat e patetlah Bawipa e kâhatnae dawkvah ka kâen e tami hai thawnaw a cum vaiteh duem a kâhat van han.
11 Tiyeni tsono tiyesetse kulowa mu mpumulo, kuti pasapezeke wina aliyense wolephera potsatira chitsanzo chawo cha kusamvera.
Isarel taminaw ni yuemnae lungthin tawn laipalah a tâlaw awh e patetlah maimouh ni tâlaw laipalah hote kâhatnae dawk kâen hanlah kâpanki awh sei.
12 Paja Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amalowa mpaka molumikizirana moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana fundo ndi mafuta a mʼmafupa. Amaweruza malingaliro ndi zokhumba za mʼmitima.
Cathut e lawk teh a hring, tahloi avoivang kahran e hlak a hran. Hringnae hoi muitha, hru kâletlout hoi rakhing totouh a thut teh a racei thai. Lungthin pouknae pueng hai a panue thai.
13 Palibe kanthu kobisika pamaso pa Mulungu. Zinthu zonse zili poyera ndi zovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.
Sak e hnonaw pueng dawkvah Cathut hmalah ka kamnuek hoeh e buet touh boehai awm hoeh. Bangpuengpa teh, Bawipa e hmalah ka ngue e awm laipalah pheng a kamnue. Maimouh pueng teh hote Bawipa ni akung na khei awh han.
14 Popeza kuti tili ndi Mkulu wa ansembe wopambana, amene analowa kale kumwamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tiyeni tigwiritsitse chikhulupiriro chathu chimene timavomereza.
Atu kalvan kho ka kâen e Vaihma Kacue, Cathut Capa Jisuh teh maimouh koe kalenpounge Vaihma Kacue lah ao dawkvah, maimouh ni yuemnae lawk dawk kacaklah awm awh sei.
15 Pakuti sitili ndi Mkulu wa ansembe amene sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofowoka zathu. Koma tili naye amene anayesedwa mʼnjira zonse monga ife, koma sanachimwe.
Bangkongtetpawiteh, maimouh thayounnae kapanuekkhaikung Vaihma Kacue tawn awh. Ahni teh maimouh patetlah tacueknae aphunphun a kâhmo. Hatei, yonnae tawn hoeh.
16 Tiyeni tsono tiyandikire ku mpando waufumu, wachisomo mopanda mantha, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo chotithandiza pa nthawi yeniyeni.
Hatdawkvah, maimouh teh a pahrennae hoi a lungmanae naw hah coe awh teh panki nah tueng nah kabawpnae hmu nahanlah lungtang nalaihoi lungmanae bawitungkhung koe rek hnai awh haw sei.