< Ahebri 13 >
1 Pitirizani kukondana monga abale.
Let brotherly love continue.
2 Musayiwale kusamalira alendo, pakuti pochita zimenezi anthu ena anasamalira angelo amene samawadziwa.
Be not forgetful to entertain strangers: for thereby some have entertained angels unawares.
3 Muzikumbukira amene ali mʼndende ngati kuti inunso ndi omangidwa, ndiponso amene akusautsidwa ngati inunso mukuvutika.
Remember them that are in bonds, as bound with them; and them which suffer adversity, as being yourselves also in the body.
4 Ukwati muziwulemekeza nonse, ndipo mwamuna ndi mkazi azikhala wokhulupirika, pakuti anthu adama ndi achigololo Mulungu adzawalanga.
Marriage is honourable in all, and the bed undefiled: but whoremongers and adulterers YHWH will judge.
5 Mtima wanu usakonde ndalama koma mukhutitsidwe ndi zimene muli nazo, chifukwa Mulungu anati, “Sadzakusiyani, kapena kukutayani konse.”
Let your conversation be without covetousness; and be content with such things as ye have: for he hath said, I will never leave thee, nor forsake thee.
6 Kotero ife tikunena molimba mtima kuti, “Ambuye ndiye mthandizi wanga; sindidzachita mantha. Munthu angandichitenji ine?”
So that we may boldly say, YHWH is my helper, and I will not fear what man shall do unto me.
7 Muzikumbukira atsogoleri anu, amene amakulalikirani Mawu a Mulungu. Ganizirani zamoyo wawo ndipo tsatirani chikhulupiriro chawo.
Remember them which have the rule over you, who have spoken unto you the word of YHWH: whose faith follow, considering the end of their conversation.
8 Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse. (aiōn )
Yahushua the Messiah the same yesterday, and to day, and for ever. (aiōn )
9 Musasocheretsedwe ndi ziphunzitso zosiyanasiyana zachilendo. Nʼkwabwino kuti mitima yathu ilimbikitsidwe ndi chisomo osati ndi chakudya, chimene sichipindulitsa iwo amene amachidya.
Be not carried about with divers and strange doctrines. For it is a good thing that the heart be established with favour; not with meats, which have not profited them that have been occupied therein.
10 Ife tili ndi guwa lansembe, ndipo ansembe otumikira mʼtenti cha Ayuda, saloledwa kudya zochokera pamenepo.
We have an altar, whereof they have no right to eat which serve the tabernacle.
11 Mkulu wa ansembe amatenga magazi kukapereka nsembe chifukwa cha machimo, koma nyamayo imawotchedwa kunja kwa msasa.
For the bodies of those beasts, whose blood is brought into the sanctuary by the high priest for sin, are burned without the camp.
12 Nʼchifukwa chakenso Yesu anafera kunja kwa mzinda kuti ayeretse anthu ake kudzera mʼmagazi ake.
Wherefore Yahushua also, that he might sanctify the people with his own blood, suffered without the gate.
13 Tiyeni tsono, tipite kwa iye kunja kwa msasa, titasenza chitonzo chake.
Let us go forth therefore unto him without the camp, bearing his reproach.
14 Pakuti ife tilibe mzinda wokhazikika koma tikudikira mzinda umene ukubwera.
For here have we no continuing city, but we seek one to come.
15 Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake.
By him therefore let us offer the sacrifice of praise to YHWH continually, that is, the fruit of our lips giving thanks to his name.
16 Ndipo musayiwale kumachita zabwino ndi kuthandiza ena, pakuti Mulungu amakondwera ndi nsembe zotere.
But to do good and to communicate forget not: for with such sacrifices YHWH is well pleased.
17 Muzimvera atsogoleri anu ndi kugonjera ulamuliro wawo, iwo amakuyangʼanirani monga anthu amene adzayenera kufotokoza za ntchito yawo pamaso pa Mulungu. Muziwamvera kuti agwire ntchito yawo ndi chimwemwe osati molemedwa pakuti izi sizingakupindulireni.
Obey them that have the rule over you, and submit yourselves: for they watch for your souls, as they that must give account, that they may do it with joy, and not with grief: for that is unprofitable for you.
18 Mutipempherere ifenso. Pakuti tikutsimikiza kuti tili ndi chikumbumtima changwiro ndipo timafuna kuchita zinthu zonse mwaulemu.
Pray for us: for we trust we have a good conscience, in all things willing to live honestly.
19 Ine ndikukupemphani kuti mundipempherere kuti Mulungu andibwezere kwa inu msanga.
But I beseech you the rather to do this, that I may be restored to you the sooner.
20 Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, (aiōnios )
Now the Elohim of peace, that brought again from the dead our Master Yahushua, that great shepherd of the sheep, through the blood of the everlasting covenant, (aiōnios )
21 akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni. (aiōn )
Make you perfect in every good work to do his will, working in you that which is wellpleasing in his sight, through Yahushua the Messiah; to whom be glory for ever and ever. amein. (aiōn )
22 Ndikukupemphani abale kuti mulandire mawu anga achilimbikitso, pakuti ndakulemberani mwachidule.
And I beseech you, brethren, suffer the word of exhortation: for I have written a letter unto you in few words.
23 Ine ndikufuna kuti inu mudziwe kuti mʼbale wathu Timoteyo wamasulidwa. Ngati iye angafike msanga ndibwera naye kudzakuonani.
Know ye that our brother Timothy is set at liberty; with whom, if he come shortly, I will see you.
24 Mupereke moni kwa atsogoleri anu onse ndiponso kwa anthu onse a Mulungu. Abale ochokera ku Italiya akupereka moni.
Salute all them that have the rule over you, and all the saints. They of Italy salute you.
25 Chisomo chikhale ndi inu nonse.
Favour be with you all. amein.