< Ahebri 13 >
1 Pitirizani kukondana monga abale.
Let the charity of the brotherhood abide in you.
2 Musayiwale kusamalira alendo, pakuti pochita zimenezi anthu ena anasamalira angelo amene samawadziwa.
And hospitality do not forget; for by this some, being not aware of it, have entertained angels.
3 Muzikumbukira amene ali mʼndende ngati kuti inunso ndi omangidwa, ndiponso amene akusautsidwa ngati inunso mukuvutika.
Remember them that are in bands, as if you were bound with them; and them that labour, as being yourselves also in the body.
4 Ukwati muziwulemekeza nonse, ndipo mwamuna ndi mkazi azikhala wokhulupirika, pakuti anthu adama ndi achigololo Mulungu adzawalanga.
Marriage honourable in all, and the bed undefiled. For fornicators and adulterers God will judge.
5 Mtima wanu usakonde ndalama koma mukhutitsidwe ndi zimene muli nazo, chifukwa Mulungu anati, “Sadzakusiyani, kapena kukutayani konse.”
Let your manners be without covetousness, contented with such things as you have; for he hath said: I will not leave thee, neither will I forsake thee.
6 Kotero ife tikunena molimba mtima kuti, “Ambuye ndiye mthandizi wanga; sindidzachita mantha. Munthu angandichitenji ine?”
So that we may confidently say: The Lord is my helper: I will not fear what man shall do to me.
7 Muzikumbukira atsogoleri anu, amene amakulalikirani Mawu a Mulungu. Ganizirani zamoyo wawo ndipo tsatirani chikhulupiriro chawo.
Remember your prelates who have spoken the word of God to you; whose faith follow, considering the end of their conversation,
8 Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse. (aiōn )
Jesus Christ, yesterday, and today; and the same for ever. (aiōn )
9 Musasocheretsedwe ndi ziphunzitso zosiyanasiyana zachilendo. Nʼkwabwino kuti mitima yathu ilimbikitsidwe ndi chisomo osati ndi chakudya, chimene sichipindulitsa iwo amene amachidya.
Be not led away with various and strange doctrines. For it is best that the heart be established with grace, not with meats; which have not profited those that walk in them.
10 Ife tili ndi guwa lansembe, ndipo ansembe otumikira mʼtenti cha Ayuda, saloledwa kudya zochokera pamenepo.
We have an altar, whereof they have no power to eat who serve the tabernacle.
11 Mkulu wa ansembe amatenga magazi kukapereka nsembe chifukwa cha machimo, koma nyamayo imawotchedwa kunja kwa msasa.
For the bodies of those beasts, whose blood is brought into the holies by the high priest for sin, are burned without the camp.
12 Nʼchifukwa chakenso Yesu anafera kunja kwa mzinda kuti ayeretse anthu ake kudzera mʼmagazi ake.
Wherefore Jesus also, that he might sanctify the people by his own blood, suffered without the gate.
13 Tiyeni tsono, tipite kwa iye kunja kwa msasa, titasenza chitonzo chake.
Let us go forth therefore to him without the camp, bearing his reproach.
14 Pakuti ife tilibe mzinda wokhazikika koma tikudikira mzinda umene ukubwera.
For we have not here a lasting city, but we seek one that is to come.
15 Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake.
By him therefore let us offer the sacrifice of praise always to God, that is to say, the fruit of lips confessing to his name.
16 Ndipo musayiwale kumachita zabwino ndi kuthandiza ena, pakuti Mulungu amakondwera ndi nsembe zotere.
And do not forget to do good, and to impart; for by such sacrifices God’s favour is obtained.
17 Muzimvera atsogoleri anu ndi kugonjera ulamuliro wawo, iwo amakuyangʼanirani monga anthu amene adzayenera kufotokoza za ntchito yawo pamaso pa Mulungu. Muziwamvera kuti agwire ntchito yawo ndi chimwemwe osati molemedwa pakuti izi sizingakupindulireni.
Obey your prelates, and be subject to them. For they watch as being to render an account of your souls; that they may do this with joy, and not with grief. For this is not expedient for you.
18 Mutipempherere ifenso. Pakuti tikutsimikiza kuti tili ndi chikumbumtima changwiro ndipo timafuna kuchita zinthu zonse mwaulemu.
Pray for us. For we trust we have a good conscience, being willing to behave ourselves well in all things.
19 Ine ndikukupemphani kuti mundipempherere kuti Mulungu andibwezere kwa inu msanga.
And I beseech you the more to do this, that I may be restored to you the sooner.
20 Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, (aiōnios )
And may the God of peace, who brought again from the dead the great pastor of the sheep, our Lord Jesus Christ, in the blood of the everlasting testament, (aiōnios )
21 akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni. (aiōn )
Fit you in all goodness, that you may do his will; doing in you that which is well pleasing in his sight, through Jesus Christ, to whom is glory for ever and ever. Amen. (aiōn )
22 Ndikukupemphani abale kuti mulandire mawu anga achilimbikitso, pakuti ndakulemberani mwachidule.
And I beseech you, brethren, that you suffer this word of consolation. For I have written to you in a few words.
23 Ine ndikufuna kuti inu mudziwe kuti mʼbale wathu Timoteyo wamasulidwa. Ngati iye angafike msanga ndibwera naye kudzakuonani.
Know ye that our brother Timothy is set at liberty: with whom (if he come shortly) I will see you.
24 Mupereke moni kwa atsogoleri anu onse ndiponso kwa anthu onse a Mulungu. Abale ochokera ku Italiya akupereka moni.
Salute all your prelates, and all the saints. The brethren from Italy salute you.
25 Chisomo chikhale ndi inu nonse.
Grace be with you all. Amen.