< Ahebri 12 >

1 Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.
Therefore, surrounded as we are by such a vast cloud of witnesses, let us fling aside every encumbrance and the sin that so readily entangles our feet. And let us run with patient endurance the race that lies before us,
2 Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu.
simply fixing our gaze upon Jesus, our Prince Leader in the faith, who will also award us the prize. He, for the sake of the joy which lay before Him, patiently endured the cross, looking with contempt upon its shame, and afterwards seated Himself-- where He still sits--at the right hand of the throne of God.
3 Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima.
Therefore, if you would escape becoming weary and faint-hearted, compare your own sufferings with those of Him who endured such hostility directed against Him by sinners.
4 Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.
In your struggle against sin you have not yet resisted so as to endanger your lives;
5 Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa: “Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.
and you have quite forgotten the encouraging words which are addressed to you as sons, and which say, "My son, do not think lightly of the Lord's discipline, and do not faint when He corrects you;
6 Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”
for those whom the Lord loves He disciplines: and He scourges every son whom He acknowledges."
7 Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga?
The sufferings that you are enduring are for your discipline. God is dealing with you as sons; for what son is there whom his father does not discipline?
8 Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo.
And if you are left without discipline, of which every true son has had a share, that shows that you are bastards, and not true sons.
9 Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo?
Besides this, our earthly fathers used to discipline us and we treated them with respect, and shall we not be still more submissive to the Father of our spirits, and live?
10 Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima.
It is true that they disciplined us for a few years according as they thought fit; but He does it for our certain good, in order that we may become sharers in His own holy character.
11 Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.
Now, at the time, discipline seems to be a matter not for joy, but for grief; yet it afterwards yields to those who have passed through its training a result full of peace--namely, righteousness.
12 Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka.
Therefore strengthen the drooping hands and paralysed knees,
13 Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.
and make straight paths for your feet, so that what is lame may not be put entirely out of joint
14 Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye.
but may rather be restored. Persistently strive for peace with all men, and for that growth in holiness apart from which no one will see the Lord.
15 Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri.
Be carefully on your guard lest there be any one who falls back from the grace of God; lest any root bearing bitter fruit spring up and cause trouble among you, and through it the whole brotherhood be defiled;
16 Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake.
lest there be a fornicator, or an ungodly person like Esau, who, in return for a single meal, parted with the birthright which belonged to him.
17 Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.
For you know that even afterwards, when he wished to secure the blessing, he was rejected; for he found no opportunity for undoing what he had done, though he sought the blessing earnestly with tears.
18 Inu simunafike ku phiri limene mungathe kulikhudza, loyaka moto wa mdima bii, la mphepo yamkuntho;
For you have not come to a material object all ablaze with fire, and to gloom and darkness and storm and trumpet-blast and the sound of words--
19 limene pali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mawu. Anthu amene amamva mawuwo anapempha kuti asawayankhulenso mawu ena.
a sound of such a kind that those who heard it entreated that no more should be added.
20 Iwo anachita mantha ndi lamulo lija lakuti, “Ngakhale nyama ikangokhudza phirilo, iphedwe ndi miyala.”
For they could not endure the order which had been given, "Even a wild beast, if it touches the mountain, shall be stoned to death;"
21 Maonekedwenso a Mose anali woopsa kwambiri, ngakhale Mose yemwe anati, “Ine ndinachita mantha ndi kunjenjemera.”
and so terrible was the scene that Moses said, "I tremble with fear."
22 Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ku mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wakumwamba. Mwafika mu msonkhano wa angelo osangalala osawerengeka.
On the contrary you have come to Mount Zion, and to the city of the ever-living God, the heavenly Jerusalem, to countless hosts of angels,
23 Mwafika mu mpingo wa ana oyamba kubadwa, amene mayina awo analembedwa kumwamba. Inu mwafika kwa Mulungu, woweruza anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama ndi osandutsidwa kukhala angwiro.
to the great festal gathering and Church of the first-born, whose names are recorded in Heaven, and to a Judge who is God of all, and to the spirits of righteous men made perfect,
24 Kwa Yesu mʼkhalapakati wa pangano latsopano, ndiponso mwafika ku magazi owazidwa amene amayankhula mawu abwino kuposa magazi a Abele.
and to Jesus the negotiator of a new Covenant, and to the sprinkled blood which speaks in more gracious tones than that of Abel.
25 Chenjerani kuti musakane kumvera amene akuyankhula nanu. Anthu amene anakana kumvera iye amene anawachenjeza uja pa dziko lapansi pano, sanapulumuke ku chilango ayi, nanga tsono ife tidzapulumuka bwanji ngati tikufulatira wotichenjeza wochokera kumwamba?
Be careful not to refuse to listen to Him who is speaking to you. For if they of old did not escape unpunished when they refused to listen to him who spoke on earth, much less shall we escape who turn a deaf ear to Him who now speaks from Heaven.
26 Pa nthawiyo mawu ake anagwedeza dziko lapansi, koma tsopano Iye walonjeza kuti, “Kamodzi kenanso ndidzagwedeza osati dziko lapansi lokha komanso thambo.”
His voice then shook the earth, but now we have His promise, "Yet again I will, once for all, cause not only the earth to tremble, but Heaven also."
27 Mawu akuti, “Kamodzi kenanso,” akuonetsa kuchotsedwa kwa zimene zitha kugwedezeka, zonse zolengedwa, kotero kuti zimene sizingatheke kugwedezeka zitsale.
Here the words "Yet again, once for all" denote the removal of the things which can be shaken--created things--in order that the things which cannot be shaken may remain.
28 Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha.
Therefore, receiving, as we now do, a kingdom which cannot be shaken, let us cherish thankfulness so that we may ever offer to God an acceptable service, with godly reverence and awe.
29 Pakuti Mulungu wathu ndi moto wonyeketsa.
For our God is also a consuming fire.

< Ahebri 12 >