< Ahebri 12 >

1 Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.
Therefore we also, having so great a cloud of witnesses surrounding us, having put off every weight and cleverly entangling sin, let us run by perseverance the contest being set before us.
2 Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu.
Looking to Jesus the pathfinder and perfecter of the faith, who, against the joy set before him, endured a cross, having despised the shame, and has sat down at the right hand of the throne of God.
3 Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima.
For consider the man who endured such hostility against him by sinners, so that ye may not be weary in your souls, being disheartened.
4 Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.
Ye have not yet resisted as far as blood, struggling against sin.
5 Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa: “Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.
And have ye forgotten the exhortation that reasons with you as with sons, My son, do not disparage the chastening of the Lord, nor become disheartened when punished by him?
6 Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”
For whom the Lord loves he chastens. And he whips every son whom he receives.
7 Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga?
Because of chastening ye endure; God is treating you as with sons, for what son is there whom a father does not chasten?
8 Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo.
And if ye are without chastening, of which all have become participants, then ye are bastards, and not sons.
9 Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo?
Besides, we indeed have had chastisers-the fathers of our flesh-and we were turned around. Shall we not much more be subordinate to the Father of the spirits, and we will live?
10 Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima.
For those men indeed for a few days chastened us according to that which seemed good to them, but he for that which is advantageous, in order to be partakers of his holiness.
11 Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.
But of course no chastening for the present seems to be of joy but of sorrow, yet afterward it yields peaceable fruit of righteousness to those who have been trained by it.
12 Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka.
Therefore lift up the drooping hands, and the feeble knees,
13 Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.
and make straight paths for your feet, so that what is lame may not be turned away, but may be healed instead.
14 Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye.
Pursue peace with all men, and the sanctification without which no man will see the Lord.
15 Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri.
Looking carefully lest any man fall short, away from the grace of God, lest any root of bitterness sprouting up would cause trouble, and by this many may be defiled,
16 Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake.
lest a fornicator or profane man like Esau, who, in place of one meal sold his birthright.
17 Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.
For ye also know that wanting afterward to inherit the blessing, he was rejected, for he found no place of repentance, though having sought it with tears.
18 Inu simunafike ku phiri limene mungathe kulikhudza, loyaka moto wa mdima bii, la mphepo yamkuntho;
For ye have not come to a mountain being felt, and which burned with fire, and to darkness, and gloom, and a tempest,
19 limene pali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mawu. Anthu amene amamva mawuwo anapempha kuti asawayankhulenso mawu ena.
and a sound of a trumpet, and a voice of words, of which those who heard begged that a word not be added to them.
20 Iwo anachita mantha ndi lamulo lija lakuti, “Ngakhale nyama ikangokhudza phirilo, iphedwe ndi miyala.”
For they did not bear that which was commanded, if even a beast should touch the mountain, it shall be stoned.
21 Maonekedwenso a Mose anali woopsa kwambiri, ngakhale Mose yemwe anati, “Ine ndinachita mantha ndi kunjenjemera.”
And so fearful was that which was made visible, that Moses said, I am terrified and trembling.
22 Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ku mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wakumwamba. Mwafika mu msonkhano wa angelo osangalala osawerengeka.
But ye have come to mount Zion, and to the city of a living God, a heavenly Jerusalem, and to myriads of agents,
23 Mwafika mu mpingo wa ana oyamba kubadwa, amene mayina awo analembedwa kumwamba. Inu mwafika kwa Mulungu, woweruza anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama ndi osandutsidwa kukhala angwiro.
to a festal gathering and assembly of firstborn sons who were enrolled in the heavens, and to God, a Judge of all, and to spirits of righteous men who were made fully perfect,
24 Kwa Yesu mʼkhalapakati wa pangano latsopano, ndiponso mwafika ku magazi owazidwa amene amayankhula mawu abwino kuposa magazi a Abele.
and to Jesus a mediator of a new covenant, and to blood of sprinkling that speaks better than Abel.
25 Chenjerani kuti musakane kumvera amene akuyankhula nanu. Anthu amene anakana kumvera iye amene anawachenjeza uja pa dziko lapansi pano, sanapulumuke ku chilango ayi, nanga tsono ife tidzapulumuka bwanji ngati tikufulatira wotichenjeza wochokera kumwamba?
Watch, that ye not refuse him who speaks. For if those men did not escape, having refused him who spoke a divine message on earth, much more we, those who turn away from him from the heavens,
26 Pa nthawiyo mawu ake anagwedeza dziko lapansi, koma tsopano Iye walonjeza kuti, “Kamodzi kenanso ndidzagwedeza osati dziko lapansi lokha komanso thambo.”
whose voice then shook the earth. But now he has promised, saying, Yet once, I shake not only the earth, but also the heaven.
27 Mawu akuti, “Kamodzi kenanso,” akuonetsa kuchotsedwa kwa zimene zitha kugwedezeka, zonse zolengedwa, kotero kuti zimene sizingatheke kugwedezeka zitsale.
And the, Yet once, signifies the removal of the things being shaken-as of things that were made-so that the things not being shaken may remain.
28 Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha.
Therefore, receiving an immovable kingdom, we may have grace, through which we may serve God acceptably with reverence and awe.
29 Pakuti Mulungu wathu ndi moto wonyeketsa.
For our God is also a consuming fire.

< Ahebri 12 >