< Ahebri 11 >
1 Tsopano chikhulupiriro ndi kusakayika konse pa zinthu zimene tikuziyembekeza, ndi kutsimikiza kuti zinthu zimene sitiziona zilipo ndithu.
১ৱিশ্ৱাস আশংসিতানাং নিশ্চযঃ, অদৃশ্যানাং ৱিষযাণাং দৰ্শনং ভৱতি|
2 Ndi chikhulupiriro chimenechi makolo athu akale anayamikidwa.
২তেন ৱিশ্ৱাসেন প্ৰাঞ্চো লোকাঃ প্ৰামাণ্যং প্ৰাপ্তৱন্তঃ|
3 Ndi chikhulupiriro timazindikira kuti dziko lapansi ndi la mmwamba zinapangidwa ndi Mawu a Mulungu, ndikuti zinthu zoonekazi zinachokera ku zinthu zosaoneka. (aiōn )
৩অপৰম্ ঈশ্ৱৰস্য ৱাক্যেন জগন্ত্যসৃজ্যন্ত, দৃষ্টৱস্তূনি চ প্ৰত্যক্ষৱস্তুভ্যো নোদপদ্যন্তৈতদ্ ৱযং ৱিশ্ৱাসেন বুধ্যামহে| (aiōn )
4 Ndi chikhulupiriro Abele anapereka kwa Mulungu nsembe yoposa imene Kaini anapereka. Ndi chikhulupiriro anatchedwa munthu wolungama Mulungu atayamikira zopereka zake. Ngakhale iye anafa, akuyankhulabe chifukwa cha chikhulupiriro chakecho.
৪ৱিশ্ৱাসেন হাবিল্ ঈশ্ৱৰমুদ্দিশ্য কাবিলঃ শ্ৰেষ্ঠং বলিদানং কৃতৱান্ তস্মাচ্চেশ্ৱৰেণ তস্য দানান্যধি প্ৰমাণে দত্তে স ধাৰ্ম্মিক ইত্যস্য প্ৰমাণং লব্ধৱান্ তেন ৱিশ্ৱাসেন চ স মৃতঃ সন্ অদ্যাপি ভাষতে|
5 Ndi chikhulupiriro Enoki anatengedwa wamoyo, motero iye sanalawe imfa; sanapezeke chifukwa Mulungu anamutenga. Pakuti asanatengedwe anayamikiridwa kuti ankakondweretsa Mulungu.
৫ৱিশ্ৱাসেন হনোক্ যথা মৃত্যুং ন পশ্যেৎ তথা লোকান্তৰং নীতঃ, তস্যোদ্দেশশ্চ কেনাপি ন প্ৰাপি যত ঈশ্ৱৰস্তং লোকান্তৰং নীতৱান্, তৎপ্ৰমাণমিদং তস্য লোকান্তৰীকৰণাৎ পূৰ্ৱ্ৱং স ঈশ্ৱৰায ৰোচিতৱান্ ইতি প্ৰমাণং প্ৰাপ্তৱান্|
6 Ndipo popanda chikhulupiriro nʼkosatheka kukondweretsa Mulungu, chifukwa aliyense amene amabwera kwa Iye ayenera kukhulupirira kuti Mulungu alipodi ndi kuti Iye amapereka mphotho kwa amene akumufunitsitsa.
৬কিন্তু ৱিশ্ৱাসং ৱিনা কোঽপীশ্ৱৰায ৰোচিতুং ন শক্নোতি যত ঈশ্ৱৰোঽস্তি স্ৱান্ৱেষিলোকেভ্যঃ পুৰস্কাৰং দদাতি চেতিকথাযাম্ ঈশ্ৱৰশৰণাগতৈ ৰ্ৱিশ্ৱসিতৱ্যং|
7 Ndi chikhulupiriro, Nowa atachenjezedwa za zinthu zimene zinali zisanaoneke, anachita mantha napanga chombo kuti apulumutsire banja lake. Ndi chikhulupiriro chake anatsutsa dziko lapansi ndipo analandira chilungamo chimene chimabwera ndi chikhulupiriro.
৭অপৰং তদানীং যান্যদৃশ্যান্যাসন্ তানীশ্ৱৰেণাদিষ্টঃ সন্ নোহো ৱিশ্ৱাসেন ভীৎৱা স্ৱপৰিজনানাং ৰক্ষাৰ্থং পোতং নিৰ্ম্মিতৱান্ তেন চ জগজ্জনানাং দোষান্ দৰ্শিতৱান্ ৱিশ্ৱাসাৎ লভ্যস্য পুণ্যস্যাধিকাৰী বভূৱ চ|
8 Ndi chikhulupiriro Abrahamu atayitanidwa kuti apite ku dziko limene anamulonjeza kuti lidzakhala lake, anamvera ndi kupita, ngakhale sanadziwe kumene ankapita.
৮ৱিশ্ৱাসেনেব্ৰাহীম্ আহূতঃ সন্ আজ্ঞাং গৃহীৎৱা যস্য স্থানস্যাধিকাৰস্তেন প্ৰাপ্তৱ্যস্তৎ স্থানং প্ৰস্থিতৱান্ কিন্তু প্ৰস্থানসমযে ক্ক যামীতি নাজানাৎ|
9 Ndi chikhulupiriro chomwecho anakhala ngati mlendo mʼdziko lija limene Mulungu anamulonjeza. Anakhala mʼmatenti monganso anachitira Isake ndi Yakobo, amene nawonso analonjezedwanso.
৯ৱিশ্ৱাসেন স প্ৰতিজ্ঞাতে দেশে পৰদেশৱৎ প্ৰৱসন্ তস্যাঃ প্ৰতিজ্ঞাযাঃ সমানাংশিভ্যাম্ ইস্হাকা যাকূবা চ সহ দূষ্যৱাস্যভৱৎ|
10 Pakuti amadikira mudzi wokhala ndi maziko, umene mmisiri ndi womanga wake ndi Mulungu.
১০যস্মাৎ স ঈশ্ৱৰেণ নিৰ্ম্মিতং স্থাপিতঞ্চ ভিত্তিমূলযুক্তং নগৰং প্ৰত্যৈক্ষত|
11 Ndi chikhulupiriro Sara analandira mphamvu zokhala ndi pakati ngakhale kuti zaka zake zobala mwana zinali zitapita kale, popeza anamutenga amene analonjeza kukhala wokhulupirika.
১১অপৰঞ্চ ৱিশ্ৱাসেন সাৰা ৱযোতিক্ৰান্তা সন্ত্যপি গৰ্ভধাৰণায শক্তিং প্ৰাপ্য পুত্ৰৱত্যভৱৎ, যতঃ সা প্ৰতিজ্ঞাকাৰিণং ৱিশ্ৱাস্যম্ অমন্যত|
12 Nʼchifukwa chake mwa munthu mmodzi, amene anali ngati wakufa, munatuluka mibado yochuluka ngati nyenyezi ndi yosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
১২ততো হেতো ৰ্মৃতকল্পাদ্ একস্মাৎ জনাদ্ আকাশীযনক্ষত্ৰাণীৱ গণনাতীতাঃ সমুদ্ৰতীৰস্থসিকতা ইৱ চাসংখ্যা লোকা উৎপেদিৰে|
13 Onsewa anakhalabe mwachikhulupiriro mpaka anafa. Iwo sanalandire zimene Mulungu anawalonjeza; iwo anangozionera chapatali ndi kuzilandira. Ndipo iwo anavomereza kuti analidi alendo ndi osakhazikika pa dziko lapansi.
১৩এতে সৰ্ৱ্ৱে প্ৰতিজ্ঞাযাঃ ফলান্যপ্ৰাপ্য কেৱলং দূৰাৎ তানি নিৰীক্ষ্য ৱন্দিৎৱা চ, পৃথিৱ্যাং ৱযং ৱিদেশিনঃ প্ৰৱাসিনশ্চাস্মহ ইতি স্ৱীকৃত্য ৱিশ্ৱাসেন প্ৰাণান্ তত্যজুঃ|
14 Anthu amene amanena zinthu zotere amaonekeratu kuti akufuna dziko lawo lenileni.
১৪যে তু জনা ইত্থং কথযন্তি তৈঃ পৈতৃকদেশো ঽস্মাভিৰন্ৱিষ্যত ইতি প্ৰকাশ্যতে|
15 Akanakhala kuti akuganizira za dziko limene analisiya akanapeza mpata obwerera kwawo.
১৫তে যস্মাদ্ দেশাৎ নিৰ্গতাস্তং যদ্যস্মৰিষ্যন্ তৰ্হি পৰাৱৰ্ত্তনায সমযম্ অলপ্স্যন্ত|
16 Mʼmalo mwake, iwo amafunitsitsa dziko labwino, ndilo lakumwamba. Nʼchifukwa chake Mulungu sachita manyazi kutchedwa Mulungu wawo, pakuti Iye anawalonjeza mudzi.
১৬কিন্তু তে সৰ্ৱ্ৱোৎকৃষ্টম্ অৰ্থতঃ স্ৱৰ্গীযং দেশম্ আকাঙ্ক্ষন্তি তস্মাদ্ ঈশ্ৱৰস্তানধি ন লজ্জমানস্তেষাম্ ঈশ্ৱৰ ইতি নাম গৃহীতৱান্ যতঃ স তেষাং কৃতে নগৰমেকং সংস্থাপিতৱান্|
17 Ndi chikhulupiriro Abrahamu, Mulungu atamuyesa, anapereka Isake ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu anamulonjeza, anakhala wokonzeka kupereka nsembe mwana wake mmodzi yekhayo.
১৭অপৰম্ ইব্ৰাহীমঃ পৰীক্ষাযাং জাতাযাং স ৱিশ্ৱাসেনেস্হাকম্ উৎসসৰ্জ,
18 Za mwana ameneyu Mulungu anamuwuza iye kuti, “Zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.”
১৮ৱস্তুত ইস্হাকি তৱ ৱংশো ৱিখ্যাস্যত ইতি ৱাগ্ যমধি কথিতা তম্ অদ্ৱিতীযং পুত্ৰং প্ৰতিজ্ঞাপ্ৰাপ্তঃ স উৎসসৰ্জ|
19 Abrahamu amazindikira kuti Mulungu angathe kuukitsa akufa, ndipo tingathe kunena mofanizira kuti iye analandiranso Isake ngati wouka kwa akufa.
১৯যত ঈশ্ৱৰো মৃতানপ্যুত্থাপযিতুং শক্নোতীতি স মেনে তস্মাৎ স উপমাৰূপং তং লেভে|
20 Ndi chikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau pa zatsogolo lawo.
২০অপৰম্ ইস্হাক্ ৱিশ্ৱাসেন যাকূব্ এষাৱে চ ভাৱিৱিষযানধ্যাশিষং দদৌ|
21 Ndi chikhulupiriro, pamene Yakobo ankamwalira anadalitsa ana awiri a Yosefe, ndipo anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
২১অপৰং যাকূব্ মৰণকালে ৱিশ্ৱাসেন যূষফঃ পুত্ৰযোৰেকৈকস্মৈ জনাযাশিষং দদৌ যষ্ট্যা অগ্ৰভাগে সমালম্ব্য প্ৰণনাম চ|
22 Ndi chikhulupiriro Yosefe ali pafupi kumwalira anayankhula za kutuluka kwa Aisraeli mu Igupto ndipo anawawuza zoti adzachite ndi mafupa ake.
২২অপৰং যূষফ্ চৰমকালে ৱিশ্ৱাসেনেস্ৰাযেল্ৱংশীযানাং মিসৰদেশাদ্ বহিৰ্গমনস্য ৱাচং জগাদ নিজাস্থীনি চাধি সমাদিদেশ|
23 Ndi chikhulupiriro Mose atabadwa makolo ake anamubisa miyezi itatu, chifukwa iwo anaona kuti mwanayo anali wokongola ndipo sanaope konse lamulo la mfumu.
২৩নৱজাতো মূসাশ্চ ৱিশ্ৱাসাৎ ত্ৰান্ মাসান্ স্ৱপিতৃভ্যাম্ অগোপ্যত যতস্তৌ স্ৱশিশুং পৰমসুন্দৰং দৃষ্টৱন্তৌ ৰাজাজ্ঞাঞ্চ ন শঙ্কিতৱন্তৌ|
24 Ndi chikhulupiriro Mose atakula, anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao.
২৪অপৰং ৱযঃপ্ৰাপ্তো মূসা ৱিশ্ৱাসাৎ ফিৰৌণো দৌহিত্ৰ ইতি নাম নাঙ্গীচকাৰ|
25 Iye anasankha kuzunzika nawo limodzi anthu a Mulungu kuposa kusangalala ndi zokondweretsa za uchimo kwa nthawi yochepa.
২৫যতঃ স ক্ষণিকাৎ পাপজসুখভোগাদ্ ঈশ্ৱৰস্য প্ৰজাভিঃ সাৰ্দ্ধং দুঃখভোগং ৱৱ্ৰে|
26 Anaona kuti kuzunzika chifukwa cha Khristu kunali kwa mtengowapatali kuposa chuma cha ku Igupto, chifukwa amaona mphotho ya mʼtsogolo.
২৬তথা মিসৰদেশীযনিধিভ্যঃ খ্ৰীষ্টনিমিত্তাং নিন্দাং মহতীং সম্পত্তিং মেনে যতো হেতোঃ স পুৰস্কাৰদানম্ অপৈক্ষত|
27 Ndi chikhulupiriro anachoka ku Igupto wosaopa ukali wa mfumu. Iye anapirira chifukwa anamuona Mulungu amene ndi wosaonekayo.
২৭অপৰং স ৱিশ্ৱাসেন ৰাজ্ঞঃ ক্ৰোধাৎ ন ভীৎৱা মিসৰদেশং পৰিতত্যাজ, যতস্তেনাদৃশ্যং ৱীক্ষমাণেনেৱ ধৈৰ্য্যম্ আলম্বি|
28 Ndi chikhulupiriro anachita Paska ndi kuwaza magazi, kuti mngelo wowononga ana oyamba kubadwa asaphe ana oyamba kubadwa a Aisraeli.
২৮অপৰং প্ৰথমজাতানাং হন্তা যৎ স্ৱীযলোকান্ ন স্পৃশেৎ তদৰ্থং স ৱিশ্ৱাসেন নিস্তাৰপৰ্ৱ্ৱীযবলিচ্ছেদনং ৰুধিৰসেচনঞ্চানুষ্ঠিতাৱান্|
29 Ndi chikhulupiriro Aisraeli anawoloka Nyanja Yofiira ngati pa mtunda powuma, koma Aigupto atayesa kutero anamizidwa.
২৯অপৰং তে ৱিশ্ৱাসাৎ স্থলেনেৱ সূফ্সাগৰেণ জগ্মুঃ কিন্তু মিস্ৰীযলোকাস্তৎ কৰ্ত্তুম্ উপক্ৰম্য তোযেষু মমজ্জুঃ|
30 Ndi chikhulupiriro mpanda wa Yeriko unagwa, Aisraeli atawuzungulira kasanu ndi kawiri.
৩০অপৰঞ্চ ৱিশ্ৱাসাৎ তৈঃ সপ্তাহং যাৱদ্ যিৰীহোঃ প্ৰাচীৰস্য প্ৰদক্ষিণে কৃতে তৎ নিপপাত|
31 Ndi chikhulupiriro Rahabe, mkazi wadama sanaphedwe pamodzi ndi osamvera aja chifukwa analandira bwino ozonda aja ku nyumba kwake.
৩১ৱিশ্ৱাসাদ্ ৰাহব্নামিকা ৱেশ্যাপি প্ৰীত্যা চাৰান্ অনুগৃহ্যাৱিশ্ৱাসিভিঃ সাৰ্দ্ধং ন ৱিননাশ|
32 Kodi ndinenenso chiyani? Nthawi yandichepera yoti ndinene za Gideoni, Baraki, Samsoni, Yefita, Davide, Samueli ndi aneneri,
৩২অধিকং কিং কথযিষ্যামি? গিদিযোনো বাৰকঃ শিম্শোনো যিপ্তহো দাযূদ্ শিমূযেলো ভৱিষ্যদ্ৱাদিনশ্চৈতেষাং ৱৃত্তান্তকথনায মম সমযাভাৱো ভৱিষ্যতি|
33 amene ndi chikhulupiriro anagonjetsa mafumu, anakhazikitsa chilungamo ndi kulandira zimene zinalonjezedwa. Anatseka pakamwa pa mikango,
৩৩ৱিশ্ৱাসাৎ তে ৰাজ্যানি ৱশীকৃতৱন্তো ধৰ্ম্মকৰ্ম্মাণি সাধিতৱন্তঃ প্ৰতিজ্ঞানাং ফলং লব্ধৱন্তঃ সিংহানাং মুখানি ৰুদ্ধৱন্তো
34 anazimitsa moto waukali, ndipo anapulumuka osaphedwa ndi lupanga. Anali ofowoka koma analandira mphamvu; anasanduka amphamvu pa nkhondo, nathamangitsa magulu a ankhondo a adani awo.
৩৪ৱহ্নেৰ্দাহং নিৰ্ৱ্ৱাপিতৱন্তঃ খঙ্গধাৰাদ্ ৰক্ষাং প্ৰাপ্তৱন্তো দৌৰ্ব্বল্যে সবলীকৃতা যুদ্ধে পৰাক্ৰমিণো জাতাঃ পৰেষাং সৈন্যানি দৱযিতৱন্তশ্চ|
35 Amayi ena analandira anthu awo amene anafa, ataukitsidwanso. Enanso anazunzidwa ndipo anakana kumasulidwa, kuti adzaukenso ndi moyo wabwino.
৩৫যোষিতঃ পুনৰুত্থানেন মৃতান্ আত্মজান্ লেভিৰে, অপৰে চ শ্ৰেষ্ঠোত্থানস্য প্ৰাপ্তেৰাশযা ৰক্ষাম্ অগৃহীৎৱা তাডনেন মৃতৱন্তঃ|
36 Ena anawaseka ndi kuwakwapula, pamenenso ena anamangidwa ndi kupita ku ndende.
৩৬অপৰে তিৰস্কাৰৈঃ কশাভি ৰ্বন্ধনৈঃ কাৰযা চ পৰীক্ষিতাঃ|
37 Anagendedwa miyala; anachekedwa pakati; ena anaphedwa ndi lupanga. Iwo anayendayenda atavala zikopa zankhosa ndi zikopa zambuzi, umphawi okhaokha, ozunzidwa ndi kuvutitsidwa.
৩৭বহৱশ্চ প্ৰস্তৰাঘাতৈ ৰ্হতাঃ কৰপত্ৰৈ ৰ্ৱা ৱিদীৰ্ণা যন্ত্ৰৈ ৰ্ৱা ক্লিষ্টাঃ খঙ্গধাৰৈ ৰ্ৱা ৱ্যাপাদিতাঃ| তে মেষাণাং ছাগানাং ৱা চৰ্ম্মাণি পৰিধায দীনাঃ পীডিতা দুঃখাৰ্ত্তাশ্চাভ্ৰাম্যন্|
38 Dziko lapansi silinawayenere. Anayendayenda mʼzipululu ndi mapiri, ndiponso mʼmapanga ndi mʼmaenje.
৩৮সংসাৰো যেষাম্ অযোগ্যস্তে নিৰ্জনস্থানেষু পৰ্ৱ্ৱতেষু গহ্ৱৰেষু পৃথিৱ্যাশ্ছিদ্ৰেষু চ পৰ্য্যটন্|
39 Onsewa anayamikidwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo, komabe palibe wa iwo amene analandira zimene analonjezedwa.
৩৯এতৈঃ সৰ্ৱ্ৱৈ ৰ্ৱিশ্ৱাসাৎ প্ৰমাণং প্ৰাপি কিন্তু প্ৰতিজ্ঞাযাঃ ফলং ন প্ৰাপি|
40 Mulungu anatikonzera ife kanthu koposa, kuti iwo asayesedwe angwiro popanda ife.
৪০যতস্তে যথাস্মান্ ৱিনা সিদ্ধা ন ভৱেযুস্তথৈৱেশ্ৱৰেণাস্মাকং কৃতে শ্ৰেষ্ঠতৰং কিমপি নিৰ্দিদিশে|