< Ahebri 11 >

1 Tsopano chikhulupiriro ndi kusakayika konse pa zinthu zimene tikuziyembekeza, ndi kutsimikiza kuti zinthu zimene sitiziona zilipo ndithu.
Ulyeteho ni lioli yalinayo umntu lwagolela ahantu ahamo hudandamazu. Ahantu hasanga haoneshe awe uyinga lioli.
2 Ndi chikhulupiriro chimenechi makolo athu akale anayamikidwa.
Nantele awababu wetu waheteshe kwa lweteho lwao.
3 Ndi chikhulupiriro timazindikira kuti dziko lapansi ndi la mmwamba zinapangidwa ndi Mawu a Mulungu, ndikuti zinthu zoonekazi zinachokera ku zinthu zosaoneka. (aiōn g165)
Kwa lweteho timenye aje munsi wahawombwelwe hundajizwa zya Ngolobhe, aje hala hahawoneha sagahahagombwilwe afume huvintu vivioneha. (aiōn g165)
4 Ndi chikhulupiriro Abele anapereka kwa Mulungu nsembe yoposa imene Kaini anapereka. Ndi chikhulupiriro anatchedwa munthu wolungama Mulungu atayamikira zopereka zake. Ngakhale iye anafa, akuyankhulabe chifukwa cha chikhulupiriro chakecho.
Ihali kwa lweteho lwa Habili ahafumizizye Ungolobhe isadaka inyinza hushile u Kaini. Husababu eyo ahasombwelwe aje alinuugolosu. Ungolobhe ahasombele. Huje ahaletile izawadi, U Habili ayanga hata nkafyiye.
5 Ndi chikhulupiriro Enoki anatengedwa wamoyo, motero iye sanalawe imfa; sanapezeke chifukwa Mulungu anamutenga. Pakuti asanatengedwe anayamikiridwa kuti ankakondweretsa Mulungu.
U Henoko ahali nulweteho ahengwilwe humwanya sagaahalolile ufye. “Sagaahawoneshe, kwa vile ilinenwa juu yake kuwa alimpendeza Ungolobhe ahamwenjile” humwanya.
6 Ndipo popanda chikhulupiriro nʼkosatheka kukondweretsa Mulungu, chifukwa aliyense amene amabwera kwa Iye ayenera kukhulupirira kuti Mulungu alipodi ndi kuti Iye amapereka mphotho kwa amene akumufunitsitsa.
Bila lweteho sagauwajie hugwezye Ungolobhe, yawala hwa Ngolobhe ahnaziwa awe nulweteho aje Ungolobhe. Akhala naje ahuwapela izawadi wala wawahumwanzo.
7 Ndi chikhulupiriro, Nowa atachenjezedwa za zinthu zimene zinali zisanaoneke, anachita mantha napanga chombo kuti apulumutsire banja lake. Ndi chikhulupiriro chake anatsutsa dziko lapansi ndipo analandira chilungamo chimene chimabwera ndi chikhulupiriro.
Ihali hulweteho aje uNuhu, ahasundilwe nu Ngolobhe humambo gasaga gahaoneshe, ishishi ya Ngolobhe ihagombile. Mbongoso yahukombole ikhaya yakwe. Ahawombile esho ahalonjile munsi, ahawa mlithi wa lioli eyo ihezele ashilile ulweteho.
8 Ndi chikhulupiriro Abrahamu atayitanidwa kuti apite ku dziko limene anamulonjeza kuti lidzakhala lake, anamvera ndi kupita, ngakhale sanadziwe kumene ankapita.
Ihali lweteho aje u Abrahimu, alipoitwa alitii na kwenda mahali ambapo alipaswa kupokea kama lwahakwiziwe aheteshe ahawalile ahaposhe ulithi ahasongoe bila amanye aje awala hwii.
9 Ndi chikhulupiriro chomwecho anakhala ngati mlendo mʼdziko lija limene Mulungu anamulonjeza. Anakhala mʼmatenti monganso anachitira Isake ndi Yakobo, amene nawonso analonjezedwanso.
Ihali lweteho ahiishi hunsi aje jenu. Ahakheye hu mahema peka nu Isaka nu Yakobo, walithi awamwao wa ndagano yiyile.
10 Pakuti amadikira mudzi wokhala ndi maziko, umene mmisiri ndi womanga wake ndi Mulungu.
Huje ahasowenye ahwenje umji wapime na wazenje yu Ngolobhe yuyo.
11 Ndi chikhulupiriro Sara analandira mphamvu zokhala ndi pakati ngakhale kuti zaka zake zobala mwana zinali zitapita kale, popeza anamutenga amene analonjeza kukhala wokhulupirika.
Ihali lweteho aje Ibrahimu, nu Sala yuyo wahaposheye ingovu zya amyemye ulwanda lakini wahali wagogolo hani wahombile Ungolowe aje golosu. Ahawasowezezye umwana wishilume.
12 Nʼchifukwa chake mwa munthu mmodzi, amene anali ngati wakufa, munatuluka mibado yochuluka ngati nyenyezi ndi yosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Huje afume hwamuntu oyo weka yahakaribiye afye wahapapwa awana wasagawazye. Wahali wichi nazi inzota zya humwanya na msanga wa hu bahari.
13 Onsewa anakhalabe mwachikhulupiriro mpaka anafa. Iwo sanalandire zimene Mulungu anawalonjeza; iwo anangozionera chapatali ndi kuzilandira. Ndipo iwo anavomereza kuti analidi alendo ndi osakhazikika pa dziko lapansi.
Ewe wonti wahafyiye nu lwetiko sagawahaposhea ulusuwelo. Ila wahalolile wahakalibisizye hwahutali waheteshe aje wahali wajenu aje washila shila munsi yao wewo.
14 Anthu amene amanena zinthu zotere amaonekeratu kuti akufuna dziko lawo lenileni.
Wala wawayanganga amambo nazi engo awashe wahuanza insi yao wewo.
15 Akanakhala kuti akuganizira za dziko limene analisiya akanapeza mpata obwerera kwawo.
Lioli nkawasewenga insi yawahafumile indi walininafasi ya wele, wangelikuwa na nafasi ya kurejea.
16 Mʼmalo mwake, iwo amafunitsitsa dziko labwino, ndilo lakumwamba. Nʼchifukwa chake Mulungu sachita manyazi kutchedwa Mulungu wawo, pakuti Iye anawalonjeza mudzi.
Eshi shileho wanyonywa insi yilishinza ya humwanya. Eshi Ungolobhe sangaalola isoni akwiziwe Ngolobhi wao yuyo agombile umji khaajili yao.
17 Ndi chikhulupiriro Abrahamu, Mulungu atamuyesa, anapereka Isake ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu anamulonjeza, anakhala wokonzeka kupereka nsembe mwana wake mmodzi yekhayo.
Ihali ilweteho u Abrahamu ahapata ingelo, ahafumya u Isaka. Umwene ahapashela ulusuwelo husheshelo, ahafumizye umwana wakwe weka,
18 Za mwana ameneyu Mulungu anamuwuza iye kuti, “Zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.”
yuyuyo ahayangwile, “Afume hwa Isaka ishikholoshakwe azakwiziwe.”
19 Abrahamu amazindikira kuti Mulungu angathe kuukitsa akufa, ndipo tingathe kunena mofanizira kuti iye analandiranso Isake ngati wouka kwa akufa.
U Ablaimu ahamenye aje Ungolobhe ahali ni ngovu wa huzyosye u Isaka afume hufyiye, ahayanjile hukabila ya shitenda wili ahaposheye.
20 Ndi chikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau pa zatsogolo lawo.
Ihali lweteho aje u Isaka ahasaile uYakobo nu Esau ahusu amambo gagahuenza.
21 Ndi chikhulupiriro, pamene Yakobo ankamwalira anadalitsa ana awiri a Yosefe, ndipo anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
Ihali lweteho aje uYakobo lwahali lwahali karibu afye ahasaile awana wa Yusufu wekaweka. U Yakobo ahaputile ahategemee humwanya yi ndesa yakwe.
22 Ndi chikhulupiriro Yosefe ali pafupi kumwalira anayankhula za kutuluka kwa Aisraeli mu Igupto ndipo anawawuza zoti adzachite ndi mafupa ake.
Ihali lweteho aje u Yusufu uwakati wakwe wa malishe lwahakalibia ahayenje aje afume hwawana wa Israeli huMisri ahawalajizya ahweje peka amafupa gakwe,
23 Ndi chikhulupiriro Mose atabadwa makolo ake anamubisa miyezi itatu, chifukwa iwo anaona kuti mwanayo anali wokongola ndipo sanaope konse lamulo la mfumu.
Ihali lweteho aje uMusa iwahapapwilwe wahafisile amezi gatatu na awazazi wakwe wahanolile aje mwana usanga ya hali mwinza, sagawaahongope indajizwo izwa mwene.
24 Ndi chikhulupiriro Mose atakula, anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao.
Ihali lweteho aje uMusa lwahali muntu ugosi ahakhanile akwiziwe mwana wa nendi wa Farao.
25 Iye anasankha kuzunzika nawo limodzi anthu a Mulungu kuposa kusangalala ndi zokondweretsa za uchimo kwa nthawi yochepa.
Pamande ahasaluye ahale na malawa peka na wantu wa Ngolobhe saga ahasungwenzye ianasa imbiwi izya papepe.
26 Anaona kuti kuzunzika chifukwa cha Khristu kunali kwa mtengowapatali kuposa chuma cha ku Igupto, chifukwa amaona mphotho ya mʼtsogolo.
Ahasewele isoni ya hufuante uKristi aje uutajili ugosi kuliko imali ya Mmisri ahakazile amaso ahunye izawadi husiku zizihwenza.
27 Ndi chikhulupiriro anachoka ku Igupto wosaopa ukali wa mfumu. Iye anapirira chifukwa anamuona Mulungu amene ndi wosaonekayo.
Ihali lweteho aje uMusa ahahepile huMisri. Sagaahogope ilioyo lya mwene, ahuenye gasanga gawoneha.
28 Ndi chikhulupiriro anachita Paska ndi kuwaza magazi, kuti mngelo wowononga ana oyamba kubadwa asaphe ana oyamba kubadwa a Aisraeli.
Ihali lweteho aje ahaikhente ipasaka na atonyelezwe idada, aje umiwi yananganya awawapapwe awahwande awashilume apotwe huwa khante, awaIsraeli.
29 Ndi chikhulupiriro Aisraeli anawoloka Nyanja Yofiira ngati pa mtunda powuma, koma Aigupto atayesa kutero anamizidwa.
Ihali lweteho aje wahashilile pahati yi isumbi ya shamu aje mahali pumu. Awamisri lwawahajezya ashile wahamililwe.
30 Ndi chikhulupiriro mpanda wa Yeriko unagwa, Aisraeli atawuzungulira kasanu ndi kawiri.
Ihali lwetiho aje uluwumba wa Yeriko wahagwiye pasi, wahazwongolile isiku saba.
31 Ndi chikhulupiriro Rahabe, mkazi wadama sanaphedwe pamodzi ndi osamvera aja chifukwa analandira bwino ozonda aja ku nyumba kwake.
Ihali lweteho aje u Rahabu ula umalaya sanga ahangamie peka na wala wasanga wahali wagolosu, ahawaopesheye wawahezele ahwenyelezye ahawa wehsele pinza,
32 Kodi ndinenenso chiyani? Nthawi yandichepera yoti ndinene za Gideoni, Baraki, Samsoni, Yefita, Davide, Samueli ndi aneneri,
Injanje zwoni hani? Amasala sanga gakwela ayanje u Gidioni, u Barak, u Samsoni, u Yeftha, u Daudi, u Samweli na awakuwa,
33 amene ndi chikhulupiriro anagonjetsa mafumu, anakhazikitsa chilungamo ndi kulandira zimene zinalonjezedwa. Anatseka pakamwa pa mikango,
aje ashilile ulweteho wahazimenile umwene wahawombile ihaki na wahaposheye ulusuwelo, wahazinjile amalomu gihanu,
34 anazimitsa moto waukali, ndipo anapulumuka osaphedwa ndi lupanga. Anali ofowoka koma analandira mphamvu; anasanduka amphamvu pa nkhondo, nathamangitsa magulu a ankhondo a adani awo.
wahazimile ingovu zwonti zi moto wahaponjele uwonji wipanga wahapona afume hu mpungo, wahali wadandamazu iwho wahezele awalogo awajenu wahashembeye.
35 Amayi ena analandira anthu awo amene anafa, ataukitsidwanso. Enanso anazunzidwa ndipo anakana kumasulidwa, kuti adzaukenso ndi moyo wabwino.
Awashe wahaposhe awafyewao hwidala la ufufulwe. Awamo wahalawile, saga waheteshe aleshwe shinza aje wawaje uzyoswo amwinza hani.
36 Ena anawaseka ndi kuwakwapula, pamenenso ena anamangidwa ndi kupita ku ndende.
Awamo wahalawile, wahasoshele, wahashetwilwe, nantele wahapinywilwe mwijela.
37 Anagendedwa miyala; anachekedwa pakati; ena anaphedwa ndi lupanga. Iwo anayendayenda atavala zikopa zankhosa ndi zikopa zambuzi, umphawi okhaokha, ozunzidwa ndi kuvutitsidwa.
Wahakhomilwa amawe. Wahawolilwe. Mentu mentu. Wahabudilwe nu panga. Wahajendanga namakwembe gingole na makwembe gi mbuzi ewo wahazanga, wahawalanga shawavyaleye wahawombwelwanga amawiwi
38 Dziko lapansi silinawayenere. Anayendayenda mʼzipululu ndi mapiri, ndiponso mʼmapanga ndi mʼmaenje.
(ewo munsi sagabhahazwanga awe nao), wahaziongolaga ziongolanga mwihombe, mwigamba, magwenya, mmagondi igamusni.
39 Onsewa anayamikidwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo, komabe palibe wa iwo amene analandira zimene analonjezedwa.
Lelo awantu wonti ewo Ungolobhe ahawenteshe wahali nulweteho, sagawahaposheye indangano.
40 Mulungu anatikonzera ife kanthu koposa, kuti iwo asayesedwe angwiro popanda ife.
Ungolobhe ahalongeye hutupele ahantu ahiza, aje bilaante sangawawajie.

< Ahebri 11 >