< Ahebri 11 >

1 Tsopano chikhulupiriro ndi kusakayika konse pa zinthu zimene tikuziyembekeza, ndi kutsimikiza kuti zinthu zimene sitiziona zilipo ndithu.
Ora, a fé é o firme fundamento das coisas que se esperam, e a prova das coisas que se não vêem.
2 Ndi chikhulupiriro chimenechi makolo athu akale anayamikidwa.
Porque por ella os antigos alcançaram testemunho.
3 Ndi chikhulupiriro timazindikira kuti dziko lapansi ndi la mmwamba zinapangidwa ndi Mawu a Mulungu, ndikuti zinthu zoonekazi zinachokera ku zinthu zosaoneka. (aiōn g165)
Pela fé entendemos que os seculos pela palavra de Deus foram creados; de maneira que as coisas que se vêem não foram feitas das que se viam. (aiōn g165)
4 Ndi chikhulupiriro Abele anapereka kwa Mulungu nsembe yoposa imene Kaini anapereka. Ndi chikhulupiriro anatchedwa munthu wolungama Mulungu atayamikira zopereka zake. Ngakhale iye anafa, akuyankhulabe chifukwa cha chikhulupiriro chakecho.
Pela fé Abel offereceu a Deus maior sacrificio do que Caim, pela qual alcançou testemunho de que era justo, porquanto Deus deu testemunho dos seus dons, e, depois de morto, ainda falla por ella.
5 Ndi chikhulupiriro Enoki anatengedwa wamoyo, motero iye sanalawe imfa; sanapezeke chifukwa Mulungu anamutenga. Pakuti asanatengedwe anayamikiridwa kuti ankakondweretsa Mulungu.
Pela fé Enoch foi trasladado para não ver a morte, e não foi achado, porquanto Deus o trasladara; porque antes da sua trasladação alcançou testemunho de que agradava a Deus.
6 Ndipo popanda chikhulupiriro nʼkosatheka kukondweretsa Mulungu, chifukwa aliyense amene amabwera kwa Iye ayenera kukhulupirira kuti Mulungu alipodi ndi kuti Iye amapereka mphotho kwa amene akumufunitsitsa.
Ora, sem fé é impossivel agradar a Deus: porque é necessario que aquelle que se approxima de Deus creia que elle existe, e que é galardoador dos que o buscam.
7 Ndi chikhulupiriro, Nowa atachenjezedwa za zinthu zimene zinali zisanaoneke, anachita mantha napanga chombo kuti apulumutsire banja lake. Ndi chikhulupiriro chake anatsutsa dziko lapansi ndipo analandira chilungamo chimene chimabwera ndi chikhulupiriro.
Pela fé Noé, divinamente advertido das coisas que ainda se não viam, temeu, e, para salvação da sua familia, fabricou a arca, pela qual condemnou o mundo, e foi feito herdeiro da justiça que é segundo a fé.
8 Ndi chikhulupiriro Abrahamu atayitanidwa kuti apite ku dziko limene anamulonjeza kuti lidzakhala lake, anamvera ndi kupita, ngakhale sanadziwe kumene ankapita.
Pela fé Abrahão, sendo chamado, obedeceu, para sair ao logar que havia de receber por herança; e saiu, sem saber para onde ia
9 Ndi chikhulupiriro chomwecho anakhala ngati mlendo mʼdziko lija limene Mulungu anamulonjeza. Anakhala mʼmatenti monganso anachitira Isake ndi Yakobo, amene nawonso analonjezedwanso.
Pela fé habitou na terra da promessa, como em terra alheia, morando em cabanas com Isaac e Jacob, herdeiros com elle da mesma promessa.
10 Pakuti amadikira mudzi wokhala ndi maziko, umene mmisiri ndi womanga wake ndi Mulungu.
Porque esperava a cidade que tem fundamentos, da qual o artifice e fabricador é Deus.
11 Ndi chikhulupiriro Sara analandira mphamvu zokhala ndi pakati ngakhale kuti zaka zake zobala mwana zinali zitapita kale, popeza anamutenga amene analonjeza kukhala wokhulupirika.
Pela fé tambem a mesma Sarah recebeu a virtude de conceber, e deu á luz já fóra da edade; porquanto teve por fiel aquelle que lh'o tinha promettido.
12 Nʼchifukwa chake mwa munthu mmodzi, amene anali ngati wakufa, munatuluka mibado yochuluka ngati nyenyezi ndi yosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Pelo que tambem de um, e esse já amortecido, nasceram em tão grande multidão como as estrellas do céu, e como a areia innumeravel que está na praia do mar.
13 Onsewa anakhalabe mwachikhulupiriro mpaka anafa. Iwo sanalandire zimene Mulungu anawalonjeza; iwo anangozionera chapatali ndi kuzilandira. Ndipo iwo anavomereza kuti analidi alendo ndi osakhazikika pa dziko lapansi.
Todos estes morreram na fé, sem terem recebido as promessas; porém, vendo-as de longe, e crendo-as e abraçando-as, confessaram que eram estrangeiros e peregrinos na terra.
14 Anthu amene amanena zinthu zotere amaonekeratu kuti akufuna dziko lawo lenileni.
Porque os que isto dizem claramente mostram que buscam outra patria.
15 Akanakhala kuti akuganizira za dziko limene analisiya akanapeza mpata obwerera kwawo.
E se, na verdade, se lembrassem d'aquella d'onde haviam saido, teriam tempo de tornar para ella.
16 Mʼmalo mwake, iwo amafunitsitsa dziko labwino, ndilo lakumwamba. Nʼchifukwa chake Mulungu sachita manyazi kutchedwa Mulungu wawo, pakuti Iye anawalonjeza mudzi.
Mas agora desejam uma melhor, isto é, a celestial. Pelo que tambem Deus se não envergonha d'elles, de se chamar seu Deus, porque já lhes apparelhou uma cidade.
17 Ndi chikhulupiriro Abrahamu, Mulungu atamuyesa, anapereka Isake ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu anamulonjeza, anakhala wokonzeka kupereka nsembe mwana wake mmodzi yekhayo.
Pela fé offereceu Abrahão a Isaac, quando foi provado; e aquelle que recebera as promessas offereceu o seu unigenito,
18 Za mwana ameneyu Mulungu anamuwuza iye kuti, “Zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.”
Sendo-lhe dito: Em Isaac será chamada a tua descendencia; considerando que Deus era poderoso para até dos mortos o resuscitar.
19 Abrahamu amazindikira kuti Mulungu angathe kuukitsa akufa, ndipo tingathe kunena mofanizira kuti iye analandiranso Isake ngati wouka kwa akufa.
Por onde tambem em similhança o tornou a recobrar.
20 Ndi chikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau pa zatsogolo lawo.
Pela fé Isaac abençoou Jacob e Esaú, no tocante ás coisas futuras.
21 Ndi chikhulupiriro, pamene Yakobo ankamwalira anadalitsa ana awiri a Yosefe, ndipo anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
Pela fé Jacob, proximo da morte, abençoou cada um dos filhos de José, e adorou encostado á ponta do seu bordão.
22 Ndi chikhulupiriro Yosefe ali pafupi kumwalira anayankhula za kutuluka kwa Aisraeli mu Igupto ndipo anawawuza zoti adzachite ndi mafupa ake.
Pela fé José, proximo da morte, fez menção da saida dos filhos de Israel, e deu ordem ácerca de seus ossos.
23 Ndi chikhulupiriro Mose atabadwa makolo ake anamubisa miyezi itatu, chifukwa iwo anaona kuti mwanayo anali wokongola ndipo sanaope konse lamulo la mfumu.
Pela fé Moysés, já nascido, foi escondido tres mezes por seus paes, porque viram que era um formoso menino; e não temeram o mandamento do rei
24 Ndi chikhulupiriro Mose atakula, anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao.
Pela fé Moysés, sendo já grande, recusou ser chamado filho da filha de Pharaó,
25 Iye anasankha kuzunzika nawo limodzi anthu a Mulungu kuposa kusangalala ndi zokondweretsa za uchimo kwa nthawi yochepa.
Escolhendo antes ser maltratado com o povo de Deus de que por um pouco de tempo ter o gozo do peccado;
26 Anaona kuti kuzunzika chifukwa cha Khristu kunali kwa mtengowapatali kuposa chuma cha ku Igupto, chifukwa amaona mphotho ya mʼtsogolo.
Tendo por maiores riquezas o vituperio de Christo do que os thesouros do Egypto; porque tinha em vista a recompensa.
27 Ndi chikhulupiriro anachoka ku Igupto wosaopa ukali wa mfumu. Iye anapirira chifukwa anamuona Mulungu amene ndi wosaonekayo.
Pela fé deixou o Egypto, não temendo a ira do rei; porque esteve firme, como vendo o invisivel.
28 Ndi chikhulupiriro anachita Paska ndi kuwaza magazi, kuti mngelo wowononga ana oyamba kubadwa asaphe ana oyamba kubadwa a Aisraeli.
Pela fé celebrou a paschoa e o derramamento de sangue, para que o destruidor dos primogenitos os não tocasse.
29 Ndi chikhulupiriro Aisraeli anawoloka Nyanja Yofiira ngati pa mtunda powuma, koma Aigupto atayesa kutero anamizidwa.
Pela fé passaram o Mar Vermelho, como por terra secca; o que intentando os egypcios, se afogaram.
30 Ndi chikhulupiriro mpanda wa Yeriko unagwa, Aisraeli atawuzungulira kasanu ndi kawiri.
Pela fé cairam os muros de Jericó, sendo sitiados durante sete dias.
31 Ndi chikhulupiriro Rahabe, mkazi wadama sanaphedwe pamodzi ndi osamvera aja chifukwa analandira bwino ozonda aja ku nyumba kwake.
Pela fé Rahab, a meretriz, não pereceu com os incredulos, acolhendo em paz os espias.
32 Kodi ndinenenso chiyani? Nthawi yandichepera yoti ndinene za Gideoni, Baraki, Samsoni, Yefita, Davide, Samueli ndi aneneri,
E que mais direi? Faltar-me-hia o tempo, contando de Gideon, e de Barac, e de Sansão, e de Jefthe, e de David, e de Samuel e dos prophetas:
33 amene ndi chikhulupiriro anagonjetsa mafumu, anakhazikitsa chilungamo ndi kulandira zimene zinalonjezedwa. Anatseka pakamwa pa mikango,
Os quaes pela fé venceram reinos, exercitaram justiça, alcançaram promessas, fecharam as boccas dos leões,
34 anazimitsa moto waukali, ndipo anapulumuka osaphedwa ndi lupanga. Anali ofowoka koma analandira mphamvu; anasanduka amphamvu pa nkhondo, nathamangitsa magulu a ankhondo a adani awo.
Apagaram a força do fogo, escaparam do fio da espada, da fraqueza tiraram forças, na batalha se esforçaram, pozeram em fugida os exercitos dos estranhos.
35 Amayi ena analandira anthu awo amene anafa, ataukitsidwanso. Enanso anazunzidwa ndipo anakana kumasulidwa, kuti adzaukenso ndi moyo wabwino.
As mulheres tornaram a receber pela resurreição os seus mortos, e outros foram estirados, não acceitando o seu livramento, para alcançarem uma melhor resurreição.
36 Ena anawaseka ndi kuwakwapula, pamenenso ena anamangidwa ndi kupita ku ndende.
E outros experimentaram escarneos e açoites, e até cadeias e prisões;
37 Anagendedwa miyala; anachekedwa pakati; ena anaphedwa ndi lupanga. Iwo anayendayenda atavala zikopa zankhosa ndi zikopa zambuzi, umphawi okhaokha, ozunzidwa ndi kuvutitsidwa.
Foram apedrejados, serrados, tentados, mortos ao fio da espada; andaram vestidos de pelles de ovelhas e de cabras, desamparados, afflictos e maltratados
38 Dziko lapansi silinawayenere. Anayendayenda mʼzipululu ndi mapiri, ndiponso mʼmapanga ndi mʼmaenje.
(Dos quaes o mundo não era digno), errantes pelos desertos, e montes, e covas e cavernas da terra.
39 Onsewa anayamikidwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo, komabe palibe wa iwo amene analandira zimene analonjezedwa.
E todos estes, tendo testemunho pela fé, não alcançaram a promessa:
40 Mulungu anatikonzera ife kanthu koposa, kuti iwo asayesedwe angwiro popanda ife.
Provendo Deus alguma coisa melhor a nosso respeito, para que sem nós não fossem aperfeiçoados.

< Ahebri 11 >