< Ahebri 10 >
1 Malamulo ndi chithunzithunzi cha zinthu zabwino zimene zikubwera, osati madalitso enieniwo. Pa chifukwa chimenechi sizingatheke konse kuti nsembe zimodzimodzi, zoperekedwa kawirikawiri, kosalekeza ndi chaka ndi chaka, kuti nʼkusandutsa angwiro amene amabwera kudzapembedza.
मूसे रा बिधान आऊणे वाल़िया खरी चीजा रा सिर्फ एक ट्वांवा ए, ये ट्वांवा तिना रा असली रूप निया। तेसरे नियमा रे मुताबिक हर साल लगातार बलि ई बलि चढ़ाई जाओई। बिधान तिना बलिदानो रे जरिए आराधना करने वाल़ेया खे कदी बी सिद्ध नि करी सकदी।
2 Ngati zikanamatero iwowo akanasiya kupereka nsembezo. Pakuti opembedzawo akanamayeretsedwa kamodzi kokha, sibwenzi chikumbumtima chawo chikuwatsutsabe chifukwa cha machimo awo.
जे से सिद्ध करी सकदा तो बलिदाना रा चढ़ाणा बंद ऊई जांदा। जे परमेशरो री आराधना करने वाल़े एक ई बार शुद्ध ऊई जांदे, तो तिना रा विवेक तिना खे पापी नि ठरांदा।
3 Koma nsembezo zimawakumbutsa anthuwo machimo awo chaka ndi chaka.
पर एबे तो तिना बलिया रे जरिए हर साल पापो खे याद करवाया जाओआ।
4 Chifukwa nʼkosatheka kuti magazi angʼombe yayimuna ndi mbuzi yayimuna achotse machimo.
कऊँकि ये ऊई नि सकदा कि जानवरा रा खून पापो खे दूर करो।
5 Nʼchifukwa chake Khristu atabwera pa dziko lapansi anati, “Simunafune nsembe kapena zopereka, koma thupi munandikonzera.
इजी बजअ ते मसीह दुनिया रे आऊँदे बखते बोलोआ, “बलिदान और पेंट तैं नि चायी, पर मेरी खातर एक शरीर त्यार कित्तेया।
6 Simunakondwere nazo nsembe zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo.
ऊम-बलिया और पाप-बलिया ते तूँ खुश नि ऊँदा।
7 Tsono, Ine ndinati, ‘Ndili pano Ine, Inu Mulungu, ndabwera kudzachita zimene mukufuna monga zinalembedwa mʼMalemba.’”
तेबे मैं बोलेया, ‘देख, आऊँ एती ए, पवित्र शास्त्रो रे मेरे बारे रे लिखेया राए ओ परमेशर आँऊ आईगा रा कि तेरी इच्छा पूरी करुँ।’”
8 Poyamba Iye anati, “Nsembe kapena zopereka zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo, Inu simunazifune kapena kukondwera nazo.” Ngakhale kuti Malamulo ndiye amanena kuti ziperekedwe.
मसीह पईले बोलोआ, “ना तैं बलिदान, पेंट, ऊम-बलिया और पाप-बलिया चाईया और ना ई तिना ते खुश ऊआ,” हालाँकि यो बलिदान बिधानो रे मुताबिक चढ़ाए जाओ थे।
9 Pamenepo Iye anati, “Ndili pano Ine, ndabwera kudzachita zimene mukufuna.” Khristu anachotsa nsembe zoyamba zija kuti mʼmalo mwake ayikemo nsembe za mtundu wachiwiri.
तेबे ये बी बोलोआ, “देख, आऊँ आईगा रा, ताकि तेरी इच्छा पूरी करुँ।” तिने पईलका बलिदान टाई ता और मसीह रे बलिदानो खे तिजी री जगा पाँदे राखी ता।
10 Chifukwa chakuti Yesu Khristu anachita zimene Mulungu anafuna kuti achite, ndife oyeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene analipereka kamodzi kokha.
परमेशरो री तेसा ई इच्छा रे मुताबिक प्रभु यीशु मसीह रे शरीरो रे एक ई बार बलिदान चढ़ाणे रे जरिए सदा खे आसे पवित्र कित्ते।
11 Wansembe aliyense amayimirira tsiku ndi tsiku nʼkutumikira, ndipo amapereka nsembe imodzimodzi mobwerezabwereza, nsembe zimene sizingathe kuchotsa machimo.
पुराणी वाचा रे मुताबिक हर एक पुरोईत तो खड़े ऊई की हर-रोज सेवा करोआ और एक ई जेड़े बलिदानो खे बार-बार चढ़ाओआ। पर ये बलिदान पापो खे कदी बी दूर नि करी सकदे।
12 Koma pamene wansembe uyu anapereka kamodzi kokha nsembe imodzi yokha chifukwa cha machimo, Iye anakhala pansi ku dzanja lamanja la Mulungu.
पर आसा रा प्रदान पुरोईत यीशु मसीह पापो रे बदले एक ई बार सदा खे आपणे आपू खे बलिदान करी चुकी रा। एबे से परमेशरो रे दाँणे कनारे बैठीगे।
13 Kumeneko akudikira tsono kuti Mulungu asandutse adani ake kukhala chopondapo mapazi ake.
तेस बखतो तेई एकी खेई न्याल़ने लगी रा, ताकि तेसरे सारे बैरी तेसरे पैरो निठली चौकी बणो।
14 Chifukwa cha nsembe imodzi Iye anasandutsa angwiro kwamuyaya iwo amene akuwayeretsa.
कऊँकि मसीहे एक ई बलिदानो रे जरिए सेयो सदा खे सिद्ध बणाईते जो तिना खे लग कित्ते रे ए।
15 Mzimu Woyera nayenso akuchitira umboni za zimenezi kwa ife. Poyamba Iye anati,
पवित्र आत्मा बी आसा खे येई गवाई देओआ। पईले प्रभुए बोलेया था,
16 “Ili ndi pangano limene ndidzachita nawo atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika malamulo anga mʼmitima mwawo, ndipo ndidzawalemba mʼmaganizo mwawo.”
“प्रभु बोलोआ कि जो वाचा मां तिना दिना ते बाद तिना साथे बानणी, से ये कि मां आपणा बिधान तिना रे दिलो रे लिखणी और मां तिना रे विवेको रे पाणी।”
17 Ndipo akutinso: “Sindidzakumbukiranso konse machimo awo ndi zolakwa zawo.”
फेर से ये बोलोआ, “मां तिना रे पाप और तिना रे बुरे काम फेर कदी बी याद नि करने।”
18 Ndipo pamene machimo akhululukidwa, sipafunikanso nsembe yoperekedwa chifukwa cha machimowo.
और जेबे पापो री माफी ऊईगी री, तो तेबे पापो खे केसी बी बलिदानो री जरूरत निए।
19 Ndipo tsono abale, molimba mtima timalowa mʼMalo Opatulika kwambiri chifukwa cha magazi a Yesu.
ओ साथी विश्वासियो, एबे आसा खे पुरा परोसा ए कि आसे प्रभु यीशुए रे खूनो रे जरिए बड़ी पवित्र जगा रे इम्मता साथे जाई सकोए।
20 Iye anatitsekulira njira yatsopano ndi yamoyo kudutsa chinsalu chotchinga, chimene ndi thupi lake.
यीशुए आसा खे आपणे शारीरिक पड़दे रे जरिए एक नई और जिऊँदी बाट खोली ती।
21 Ndiponso tili ndi wansembe wamkulu woyangʼanira nyumba ya Mulungu.
और इजी खे कि म्हारा एड़ा महान् पुरोईत ए, जो परमेशरो रे मन्दरो रा अक्कदार ए,
22 Tsono tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona ndi wodzaza ndi chikhulupiriro. Popeza mitima yathu yayeretsedwa, ndi yopanda chikumbumtima chotitsutsa, ndiponso matupi athu asambitsidwa ndi madzi woyera.
तो आओ आसे सच्चे मनो ते, पूरे विश्वासो साथे परमेशरो रे नेड़े जाऊँए कऊँकि आसे विवेको रा दोष दूर करने खे दिलो पाँदे मसीह रे खूनो रा छड़काओ लयी की और शरीरो खे साफ पाणिए की तुल़ाईता रा ताकि आसे शुद्ध ऊई जाईए।
23 Tiyeni tigwiritsitse mosagwedezeka zimene timaziyembekezera ndi kuzivomereza, pakuti amene anatilonjezayo ndi wokhulupirika.
और आपणी उम्मीदा रे अंगीकारो खे मजबूतिया रे पकड़ी की राखो। कऊँकि परमेशर जिने वादे कित्ते, से विश्वासो जोगा ए
24 Tiziganizira mmene tingalimbikitsirane wina ndi mnzake pokondana ndi kuchita ntchito zabwino.
आसे ये बी खास त्यान राखिए कि आसे आपू बीचे प्यार और खरे कामो खे करने खे एकी-दूजे खे औंसला देया करो।
25 Tiyeni tisaleke kusonkhana kwathu pamodzi monga mmene ena amachitira, koma tizilimbikitsana makamaka poona kuti tsiku la Ambuye layandikira.
और आराधना रे एकी-दूजे साथे कट्ठा ऊणा नि छाडो, जेड़ी की बऊत जणेया री रवाज ए, पर एकी-दूजे खे समजयांदे रओ और जिंयाँ-जिंयाँ प्रभुए रे वापस आऊणे रे दिनो खे नेड़े आऊँदे देखो, तिंयाँ-तिंयाँ ओर बी जादा एड़ा करेया करो।
26 Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.
सच्चाईया खे पछयाणने रे बाद जे आसे जाणी-बूजी की पाप करदे रऊँए, तो पापो खे फेर कोई ओर बलिदान निए।
27 Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu
आ, परमेशरो रे न्याय रे दण्डो री एक डराऊणी उम्मीद और आगी रा चराकड़ा बाकि ए, जेसा तेसरे सारे बिरोदी स्वा करी देणे।
28 Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu.
तिना दिना रे मूसा रे बिधानो खे ना मानणे वाल़ा दो या तीन जणेया री गवाईया पाँदे, बिना दया ते काया जाओ था।
29 Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo?
एबे सोची लो कि से और बी कितणे बड़े-पारी दण्डो जोगा ऊणा, जिने परमेशरो रा पुत्र पैरो साथे केसेया और वाचा रे खूने की जेतेरे जरिए से पवित्र ठराया था, अपवित्र जाणेया और कृपा री आत्मा री बेज्जती कित्ती।
30 Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.”
कऊँकि आसे तेसखे जाणूंए, परमेशरे बोलेया, “बदला लणा मेरा काम ए, मां ई बदला लणा।” तेबे तिने ये बी बोलेया, “प्रभुए आपणे लोका रा न्याय करना।”
31 Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.
जिऊँदे परमेशरो रे आथो रे पड़ना डराऊणी गल्ल ए।
32 Kumbukirani masiku akale aja mutangowunikiridwa chatsopano, pa nthawi imeneyi munapirira zowawa zambiri.
पर तुसे तिना शुरूआता रे दिना खे याद करो, जिना रे तुसे मसीह री ज्योति पाई और बड़े पारी दु: खो रे बी टीके रे रये।
33 Nthawi zina ankakunyozani pagulu ndi kukuzunzani. Nthawi zina munkamva zowawa pamodzi ndi amene ankasautsidwa chotere.
कदी-कदी तो एड़ा ऊआ कि खुले तौरो पाँदे तुसा री निन्दा ऊई और क्ल़ेश सईन करदे ऊए तुसा रा तमाशा बणेया। कदी-कदी एड़ा ऊआ कि तुसे तिना साथे साजे ऊए जिना रा बऊत बुरा आल करो थे।
34 Munkawamvera chisoni amene anali mʼndende ndiponso munkalola mokondwera kuti akulandeni katundu wanu chifukwa munkadziwa kuti muli nacho chuma choposa ndi chosatha.
कऊँकि तुसे कैदिया रे दु: खो रे बी दु: खी ऊए और आपणी जायदात खुशिया साथे लुटणे दित्ती; ये जाणी की कि तुसा गे स्वर्गो रे एक ओर बी खरी और सदा रणे वाल़ी जायदात ए।
35 Tsono musataye kulimbika mtima kwanuko pakuti mudzalandira nako mphotho yayikulu.
इजी री खातर प्रभुए पाँदे आपणा विश्वास बणाए रे राखो। याद राखो कि इजी रा फल बऊत बड़ा ए।
36 Nʼkofunika kuti mupirire kuti pamene muchita chifuniro cha Mulungu mudzalandire zimene Iye analonjeza.
कऊँकि तुसा खे सब्र राखणा जरूरी ए, ताकि परमेशरो री इच्छा पूरी करी की तुसा खे वादे रा फल मिलो।
37 Pakuti nʼkanthawi kochepa chabe, Iye amene akubwera adzabwera ndipo sadzachedwa ayi.
जिंयाँ कि पवित्र शास्त्र बोलोआ, “एबे बऊत ई थोड़ा जा बखत रई गा रा, जेबे आऊणे वाल़ा आऊणा और तेस देर नि करनी।
38 Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro. Ndipo ngati iye abwerera mʼmbuyo chifukwa cha mantha, Ine sindidzakondwera naye.
पर मेरा तर्मी मांणू विश्वासो साथे जिऊँदा रणा और जे से माणूं डरी की विश्वासो ते पीछे आटी जाओगा, तो मेरा मन तेसते खुश नि ऊणा।”
39 Koma ife sindife amodzi a iwo obwerera mʼmbuyo mwa mantha ndi owonongedwa, koma ndife amodzi a amene akukhulupirira ndi wopulumutsidwa.
आसे तिना लोका बीचा ते निए जो परमेशरो ते पीछे आटी की नाश ऊई जाओ। बल्कि आसे तिना लोका बीचा ते जो आपणे विश्वासो रे जरिए जिन्दगी पाओए।