< Ahebri 10 >
1 Malamulo ndi chithunzithunzi cha zinthu zabwino zimene zikubwera, osati madalitso enieniwo. Pa chifukwa chimenechi sizingatheke konse kuti nsembe zimodzimodzi, zoperekedwa kawirikawiri, kosalekeza ndi chaka ndi chaka, kuti nʼkusandutsa angwiro amene amabwera kudzapembedza.
For the Law having a shadow of the good things coming—not the very image of the matters, every year, by the same sacrifices that they offer continually, is never able to make perfect those coming near,
2 Ngati zikanamatero iwowo akanasiya kupereka nsembezo. Pakuti opembedzawo akanamayeretsedwa kamodzi kokha, sibwenzi chikumbumtima chawo chikuwatsutsabe chifukwa cha machimo awo.
since, would they not have ceased to be offered, because of those serving having no more conscience of sins, having been purified once?
3 Koma nsembezo zimawakumbutsa anthuwo machimo awo chaka ndi chaka.
But in those [sacrifices] is a remembrance of sins every year,
4 Chifukwa nʼkosatheka kuti magazi angʼombe yayimuna ndi mbuzi yayimuna achotse machimo.
for it is impossible for blood of bulls and goats to take away sins.
5 Nʼchifukwa chake Khristu atabwera pa dziko lapansi anati, “Simunafune nsembe kapena zopereka, koma thupi munandikonzera.
For this reason, coming into the world, He says, “Sacrifice and offering You did not will, and a body You prepared for Me;
6 Simunakondwere nazo nsembe zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo.
in burnt-offerings, and concerning sin-offerings, You did not delight.
7 Tsono, Ine ndinati, ‘Ndili pano Ine, Inu Mulungu, ndabwera kudzachita zimene mukufuna monga zinalembedwa mʼMalemba.’”
Then I said, Behold, I come (in a volume of the scroll it has been written concerning Me), to do, O God, Your will”;
8 Poyamba Iye anati, “Nsembe kapena zopereka zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo, Inu simunazifune kapena kukondwera nazo.” Ngakhale kuti Malamulo ndiye amanena kuti ziperekedwe.
saying above, “Sacrifice, and offering, and burnt-offerings, and concerning sin-offering You did not will, nor delight in” (which are offered according to the Law),
9 Pamenepo Iye anati, “Ndili pano Ine, ndabwera kudzachita zimene mukufuna.” Khristu anachotsa nsembe zoyamba zija kuti mʼmalo mwake ayikemo nsembe za mtundu wachiwiri.
then He said, “Behold, I come to do, O God, Your will”; He takes away the first that He may establish the second;
10 Chifukwa chakuti Yesu Khristu anachita zimene Mulungu anafuna kuti achite, ndife oyeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene analipereka kamodzi kokha.
in which will, we have been sanctified through the offering of the body of Jesus Christ once for all,
11 Wansembe aliyense amayimirira tsiku ndi tsiku nʼkutumikira, ndipo amapereka nsembe imodzimodzi mobwerezabwereza, nsembe zimene sizingathe kuchotsa machimo.
and every priest, indeed, has daily stood serving, and offering the same sacrifices many times, that are never able to take away sins.
12 Koma pamene wansembe uyu anapereka kamodzi kokha nsembe imodzi yokha chifukwa cha machimo, Iye anakhala pansi ku dzanja lamanja la Mulungu.
But He, having offered one sacrifice for sin—to the end, sat down at the right hand of God—
13 Kumeneko akudikira tsono kuti Mulungu asandutse adani ake kukhala chopondapo mapazi ake.
as to the rest, expecting until He may place His enemies [as] His footstool,
14 Chifukwa cha nsembe imodzi Iye anasandutsa angwiro kwamuyaya iwo amene akuwayeretsa.
for by one offering He has perfected to the end those being sanctified;
15 Mzimu Woyera nayenso akuchitira umboni za zimenezi kwa ife. Poyamba Iye anati,
and the Holy Spirit also testifies to us, for after that He has said before,
16 “Ili ndi pangano limene ndidzachita nawo atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika malamulo anga mʼmitima mwawo, ndipo ndidzawalemba mʼmaganizo mwawo.”
“This [is] the covenant that I will make with them after those days, says the LORD, giving My laws on their hearts, and I will write them on their minds,”
17 Ndipo akutinso: “Sindidzakumbukiranso konse machimo awo ndi zolakwa zawo.”
and, “I will remember their sins and their lawlessness no more”;
18 Ndipo pamene machimo akhululukidwa, sipafunikanso nsembe yoperekedwa chifukwa cha machimowo.
and where [there is] forgiveness of these, there is no longer offering for sin.
19 Ndipo tsono abale, molimba mtima timalowa mʼMalo Opatulika kwambiri chifukwa cha magazi a Yesu.
Having, therefore, brothers, boldness for the entrance into the holy places, by the blood of Jesus,
20 Iye anatitsekulira njira yatsopano ndi yamoyo kudutsa chinsalu chotchinga, chimene ndi thupi lake.
which [is] the way He initiated for us—new and living, through the veil, that is, His flesh—
21 Ndiponso tili ndi wansembe wamkulu woyangʼanira nyumba ya Mulungu.
and a Great Priest over the house of God,
22 Tsono tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona ndi wodzaza ndi chikhulupiriro. Popeza mitima yathu yayeretsedwa, ndi yopanda chikumbumtima chotitsutsa, ndiponso matupi athu asambitsidwa ndi madzi woyera.
may we draw near with a true heart, in full assurance of faith, having the hearts sprinkled from an evil conscience, and having the body bathed with pure water;
23 Tiyeni tigwiritsitse mosagwedezeka zimene timaziyembekezera ndi kuzivomereza, pakuti amene anatilonjezayo ndi wokhulupirika.
may we hold fast the unwavering profession of the hope (for He who promised [is] faithful),
24 Tiziganizira mmene tingalimbikitsirane wina ndi mnzake pokondana ndi kuchita ntchito zabwino.
and may we consider to provoke one another to love and to good works,
25 Tiyeni tisaleke kusonkhana kwathu pamodzi monga mmene ena amachitira, koma tizilimbikitsana makamaka poona kuti tsiku la Ambuye layandikira.
not forsaking the assembling of ourselves together, as [is] a custom of some, but exhorting, and so much the more as you see the Day coming near.
26 Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.
For [if] we are sinning willingly after receiving the full knowledge of the truth—there remains no more sacrifice for sins,
27 Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu
but a certain fearful looking for of judgment, and fiery zeal, about to devour the opposers;
28 Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu.
anyone having set aside a law of Moses dies without mercies on the basis of two or three witnesses.
29 Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo?
Of how much worse punishment will he be counted worthy who trampled on the Son of God, and counted the blood of the covenant a common thing, by which he was sanctified, and having insulted the Spirit of grace?
30 Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.”
For we have known Him who is saying, “Vengeance [is] Mine, I will repay, says the LORD”; and again, “The LORD will judge His people.”
31 Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.
[It is] fearful to fall into [the] hands of [the] living God.
32 Kumbukirani masiku akale aja mutangowunikiridwa chatsopano, pa nthawi imeneyi munapirira zowawa zambiri.
But call to your remembrance the former days, in which, having been enlightened, you endured much conflict of sufferings;
33 Nthawi zina ankakunyozani pagulu ndi kukuzunzani. Nthawi zina munkamva zowawa pamodzi ndi amene ankasautsidwa chotere.
this indeed, being made spectacles with both insults and afflictions, now this, having become partners of those so living,
34 Munkawamvera chisoni amene anali mʼndende ndiponso munkalola mokondwera kuti akulandeni katundu wanu chifukwa munkadziwa kuti muli nacho chuma choposa ndi chosatha.
for you also sympathized with my bonds, and the robbery of your goods you received with joy, knowing that you have in yourselves a better substance in the heavens, and an enduring one.
35 Tsono musataye kulimbika mtima kwanuko pakuti mudzalandira nako mphotho yayikulu.
You may not cast away, then, your boldness, which has great repayment of reward,
36 Nʼkofunika kuti mupirire kuti pamene muchita chifuniro cha Mulungu mudzalandire zimene Iye analonjeza.
for you have need of patience, that having done the will of God, you may receive the promise.
37 Pakuti nʼkanthawi kochepa chabe, Iye amene akubwera adzabwera ndipo sadzachedwa ayi.
“For yet [in] a very, very little [while], He who is coming will come, and will not linger,”
38 Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro. Ndipo ngati iye abwerera mʼmbuyo chifukwa cha mantha, Ine sindidzakondwera naye.
but, “The righteous will live by faith; and if he may draw back, My soul has no pleasure in him.”
39 Koma ife sindife amodzi a iwo obwerera mʼmbuyo mwa mantha ndi owonongedwa, koma ndife amodzi a amene akukhulupirira ndi wopulumutsidwa.
But we are not of those drawing back to destruction, but of those believing to a preserving of soul.