< Hagai 2 >

1 Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti:
Le septième mois, le vingt-et-unième jour du mois, la parole de Dieu arriva par l’organe du prophète Haggaï en ces termes:
2 “Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti,
"Adresse donc à Zorobabel, fils de Chaltiël, gouverneur de Judée, à Josué, fils de Joçadak, le grand-prêtre, et au reste du peuple les paroles que voici:
3 ‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu?
"Est-II encore parmi vous quelqu’un qui ait vu ce temple dans sa splendeur primitive? Et comment le considérez-vous à présent? N’Est-il pas vrai qu’il est comme rien à vos yeux?
4 Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Toutefois, prends courage, Zorobabel, dit le Seigneur, prends courage, Josué, fils de Joçadak, toi le grand-prêtre, prenez courage, vous les gens de ce pays, dit l’Eternel, et agissez en conséquence, car je suis avec vous, dit l’Eternel-Cebaot.
5 ‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’
Aux termes de l’alliance que j’ai contractée avec vous lors de votre sortie de l’Egypte, mon esprit réside au milieu de vous: ne craignez rien!"
6 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda.
"Oui, ainsi parle l’Eternel-Cebaot, encore un court délai, et je mettrai en mouvement le ciel et la terre, la mer et le continent;
7 Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
je mettrai en mouvement tous les peuples, pour qu’affluent ici les biens les plus précieux de tous ces peuples, et ainsi je remplirai cette maison de splendeur, dit l’Eternel-Cebaot.
8 ‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
A moi appartient l’argent, à moi l’or, dit l’Eternel-Cebaot.
9 ‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
Plus grande sera la splendeur de ce second temple que celle du premier, dit l’Eternel-Cebaot, et en ce lieu je ferai régner la paix, dit l’Eternel-Cebaot."
10 Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti:
Le vingt-quatrième jour du neuvième mois, dans la deuxième année de Darius, la parole de Dieu arriva par l’organe du prophète Haggaï en ces termes:
11 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena:
"Ainsi parle l’Eternel-Cebaot: Interroge donc les prêtres sur le point de doctrine que voici:
12 Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’” Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”
S’Il arrive que quelqu’un transporte de la chair consacrée dans le pan de son habit, et qu’il mette ce pan de vêtement en contact avec du pain, un légume, du vin, de l’huile ou tout autre comestible, ceux-ci contracteront-ils la sainteté?" Les prêtres répondirent en disant: "Non!"
13 Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?” Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”
Haggaï reprit: "Si une personne devenue impure par le contact d’un mort touche ces objets, seront-ils impurs?" Les prêtres répondirent en disant: "Ils seront impurs."
14 Pamenepo Hagai anati, “‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.
Alors Haggaï prit la parole et dit: "Il en est ainsi de ce peuple: voilà comme il paraît à mes yeux, ce peuple, dit l’Eternel, lui et toutes les œuvres de ses mains. Ce qu’ils me présentent là comme offrande est impur!
15 “‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova.
Or ça, observez attentivement ce qui va se passer dans la suite, à partir de ce jour; car jusqu’aujourd’hui on n’avait pas posé pierre sur pierre au sanctuaire de l’Eternel.
16 Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha.
Jadis, on se rendait auprès d’un monceau de vingt gerbes, et il n’y en avait que dix; on se rendait auprès d’une cuve de vin dans l’attente d’y puiser cinquante mesures et elles se réduisaient à vingt.
17 Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova
Je vous avais éprouvés par la rouille, la nielle et la grêle, s’attaquant à toute l’ouvre de vos mains, mais cela ne vous a pas ramenés à moi, dit l’Eternel.
18 ‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino.
Observez donc avec soin ce qui va se passer, à dater de ce jour et ultérieurement, à dater de ce jour qui est le vingt-quatrième du neuvième mois, jour où ont été jetés les fondements du sanctuaire de l’Eternel. Oui, prenez-le bien à cœur!
19 Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso. “‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’”
Avez-vous encore des grains dans le grenier? N’Est-ce pas que ni vigne, ni figuier, ni grenadier, ni olivier n’ont rien donné? Mais à partir de ce jour je vous comblerai de mes bénédictions."
20 Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti:
La parole de l’Eternel s’adressa une seconde fois à Haggaï, le vingt-quatrième jour du mois, en ces termes:
21 “Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi.
"Dis à Zorobabel, gouverneur de Judée, ce qui suit: Je vais faire trembler le ciel et la terre.
22 Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.
Je mettrai sens dessus dessous le trône des royaumes, je détruirai la puissance des empires des nations; je renverserai les chars de guerre et ceux qui y siègent, les coursiers et leurs cavaliers tomberont à terre, frappés les uns par le glaive des autres.
23 “‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
En ce jour, dit l’Eternel-Cebaot, je te prendrai, ô Zorobabel, fils de Chaltiël, toi mon serviteur, dit l’Eternel, et je te considérerai comma un anneau sigillaire, car c’est toi que j’ai élu, dit l’Eternel-Cebaot."

< Hagai 2 >