< Hagai 2 >

1 Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti:
In the seventh [month], on the twenty-first of the month, a word of YHWH has been by the hand of Haggai the prophet, saying,
2 “Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti,
“Now speak to Zerubbabel son of Shealtiel, governor of Judah, and to Joshua son of Josedech, the high priest, and to the remnant of the people, saying,
3 ‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu?
Who among you has been left that saw this house in its former glory? And what are you seeing it now? Is it not, compared with it, as nothing in your eyes?
4 Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And now, be strong, O Zerubbabel,” A declaration of YHWH, “And be strong, O Joshua, son of Josedech, the high priest, And be strong, all you people of the land,” A declaration of YHWH, “And do, for I [am] with you,” A declaration of YHWH of Hosts.
5 ‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’
“The thing that I covenanted with you, In your coming forth from Egypt, And My Spirit is remaining in your midst, do not fear.”
6 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda.
For thus said YHWH of Hosts: “Yet once more—it [is] a little, And I am shaking the heavens and the earth, And the sea, and the dry land,
7 Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And I have shaken all the nations, And they have come [to] the desire of all the nations, And I have filled this house [with] glory,” said YHWH of Hosts.
8 ‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
“The silver [is] Mine, and the gold [is] Mine,” A declaration of YHWH of Hosts.
9 ‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
“Greater is the glory of this latter house, Than of the former,” said YHWH of Hosts, “And I give peace in this place,” A declaration of YHWH of Hosts.
10 Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti:
On the twenty-fourth of the ninth [month], in the second year of Darius, a word of YHWH has been by the hand of Haggai the prophet, saying,
11 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena:
Thus said YHWH of Hosts: “Now ask the priests of the Law, saying,
12 Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’” Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”
Behold, [when] one carries holy flesh in the skirt of his garment, and he has come with his skirt against the bread, or against the stew, or against the wine, or against the oil, or against any food—is it holy?” And the priests answer and say, “No.”
13 Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?” Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”
And Haggai says, “If the unclean of body comes against any of these, is it unclean?” And the priests answer and say, “It is unclean.”
14 Pamenepo Hagai anati, “‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.
And Haggai answers and says, “So [is] this people, and so [is] this nation before Me,” a declaration of YHWH, “and so [is] every work of their hands, and that which they bring near there—it is unclean.
15 “‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova.
And now, please lay [it] to your heart, From this day and onward, Before the laying of stone to stone in the temple of YHWH.
16 Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha.
From that time [one] has come to a heap of twenty, And it has been ten, He has come to the wine vat to draw out fifty measures, And it has been twenty.
17 Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova
I have struck you with blasting, And with mildew, and with hail—All the work of your hands, And there is none of you with Me,” A declaration of YHWH.
18 ‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino.
“Now set [it] to your heart, from this day and onward, from the twenty-fourth day of the ninth [month], even from the day that the temple of YHWH has been founded, set [it] to your heart.
19 Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso. “‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’”
Is the seed yet in the barn? And until now the vine and the fig, And the pomegranate, and the olive-tree, Have not borne—from this day I bless.”
20 Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti:
And there is a word of YHWH a second time to Haggai, on the twenty-fourth of the month, saying,
21 “Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi.
“Speak to Zerubbabel governor of Judah, saying, I am shaking the heavens and the earth,
22 Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.
And have overturned the throne of kingdoms, And I have destroyed the strength of kingdoms of the nations, And overturned chariot and its charioteers, And horses and their riders have come down, Each by the sword of his brother.
23 “‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
In that day,” a declaration of YHWH of Hosts, “I take you, Zerubbabel, son of Shealtiel, My servant,” A declaration of YHWH, “And have set you as a signet, For I have fixed on you,” A declaration of YHWH of Hosts!

< Hagai 2 >