< Hagai 1 >
1 Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
La seconde année du roi Darius, le sixième mois, le premier jour du mois, la parole de l'Éternel fut adressée par Aggée, le prophète, à Zorobabel, fils de Salathiel, gouverneur de Juda, et à Josué, fils de Jéhotsadak, grand sacrificateur, en ces mots:
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
Ainsi parle l'Éternel des armées: Ce peuple dit: Le moment n'est pas encore venu, le moment où la maison de l'Éternel doit être rebâtie.
3 Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
C'est pourquoi la parole de l'Éternel fut adressée par Aggée, le prophète, en ces mots:
4 “Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
Est-ce le moment pour vous-mêmes de vous loger dans vos maisons lambrissées, tandis que cette maison est en ruine?
5 Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
Or ainsi parle l'Éternel des armées: Soyez attentifs à la voie où vous êtes!
6 Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
Vous semez beaucoup et récoltez peu, vous mangez, mais non pas jusqu'à rassasiement, vous buvez, mais non pas votre soûl; vous avez des habits, mais non jusqu'à avoir chaud, et celui qui sert pour un gage, met ses gains dans une bourse trouée.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
Ainsi parle l'Éternel des armées: Soyez attentifs à la voie où vous êtes!
8 Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
Montez à la montagne et en amenez du bois, et bâtissez la maison, afin que j'en aie du plaisir et que gloire me soit rendue, dit l'Éternel.
9 “Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
Vous comptiez sur beaucoup, et voici, vous avez peu; et si vous l'amenez à la maison, je le dissipe. Pourquoi? dit l'Éternel des armées. A cause de ma maison qui est en ruine, tandis que vous êtes empressés chacun pour sa maison.
10 Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
C'est pourquoi au-dessus de vous les Cieux retiennent la rosée, et la terre retient son produit;
11 Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
et j'ai appelé la sécheresse sur le pays et sur les montagnes, et sur le blé, et sur le moût, et sur l'huile, et sur tout ce que produit le sol, et sur l'homme, et sur le bétail, et sur tout le travail des mains.
12 Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
Et Zorobabel, fils de Salathiel, et Josué, fils de Jéhotsadak, grand sacrificateur, et tous les restes du peuple furent dociles à la voix de l'Éternel, leur Dieu, et aux paroles d'Aggée, le prophète, parce que l'Éternel, leur Dieu, l'avait envoyé, et le peuple eut crainte de l'Éternel.
13 Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
Et Aggée, envoyé de l'Éternel, parla en vertu de la mission de l'Éternel au peuple en ces mots: Je suis avec vous, dit l'Éternel.
14 Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
Et l'Éternel donna l'éveil à l'esprit de Zorobabel, fils de Salathiel, gouverneur de Juda, et à l'esprit de Josué, fils de Jéhotsadak, grand sacrificateur, et à l'esprit de tous les restes du peuple, et ils vinrent et se mirent à l'œuvre dans la maison de l'Éternel des armées, leur Dieu,
15 pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.
le vingt-quatrième jour du sixième mois, la seconde année du roi Darius.