< Hagai 1 >
1 Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
Във втората година на цар Дария, в шестия месец, на първия ден от месеца, Господнето слово дойде чрез пророк Агея към управителят на Юда Заровавел Салатиилевия син, и към великият свещеник Исус Иоседековия син, и рече:
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
Така говори Господ на Силите, казвайки: Тия люде думат - Не е още времето, което щяло да дойде, времето да се постои Господният дом.
3 Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
За това, Господнето слово дойде чрез пророк Агея и рече:
4 “Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
Време ли е сами вие Да живеете в своите с дъски обковани къщи, Докато тоя дом остава пуст?
5 Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
Сега прочее така казва Господ на Силите: Помислете за постъпките си.
6 Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
Посеяхте много, но малко събрахте; Ядете, но не се насищате; Пиете, но не се напивате; Обличате се, но никому не му е топло; И надничарят приема заплатата, за да я тури в скъсан мешец.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
Така казва Господ на Силите: Помислете за постъпките си.
8 Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
Качете се на гората, та докарайте дърва И постройте домът; И Аз ще благоволя в него, И ще се прославя, казва Господ.
9 “Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
Очаквахте за много, а, ето, излезе малко; И когато го донесохте у дома си, аз духнах на него. Защо? казва Господ на Силите. Поради Моя дом, който остава пуст, Докато вие тичате всеки в своята къща.
10 Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
И тъй, поради вас небето задържа росата си, И земята възпира плода си;
11 Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
Защото аз повиках суша На земята и по горите, На житото, на виното, и на дървеното масло, На всичко що произвежда земята, На човеците и на добитъка, И на всичките трудове на човешките ръце.
12 Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
Тогава Зоровавел Салатиилевият син, и великият свещеник Исус Иоседековият син, и всичките оцелели люде послушаха гласа на Господа своя Бог и думите на пророк Агея, както го бе изпратил Господ техният Бог; и людете се убояха пред Господа.
13 Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
И Господният пратеник Агей говори на людете с думите на Господнето послание, казвайки: Аз съм с вас, дума Господ.
14 Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
И Господ възбуди духа на управителя на Юда Зоровавел Салатиилевия син, и духа на великия свещеник Исус Иоседековия син, и духа на всички оцелели люде; и те дойдоха та работеха в дома на Господа на Силите, своя Бог,
15 pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.
като започнаха на двадесет и четвъртия ден от шестия месец, във втората година на цар Дария.